< Psalms 33 >

1 Rejoice in the LORD, you righteous! Praise is fitting for the upright.
Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
2 Give thanks to the LORD with the lyre. Sing praises to him with the harp of ten strings.
Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
3 Sing to him a new song. Play skillfully with a shout of joy!
Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
4 For the LORD’s word is right. All his work is done in faithfulness.
Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
5 He loves righteousness and justice. The earth is full of the loving kindness of the LORD.
Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
6 By the LORD’s word, the heavens were made: all their army by the breath of his mouth.
Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
7 He gathers the waters of the sea together as a heap. He lays up the deeps in storehouses.
Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
8 Let all the earth fear the LORD. Let all the inhabitants of the world stand in awe of him.
Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
9 For he spoke, and it was done. He commanded, and it stood firm.
Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
10 The LORD brings the counsel of the nations to nothing. He makes the thoughts of the peoples to be of no effect.
Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
11 The counsel of the LORD stands fast forever, the thoughts of his heart to all generations.
Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
12 Blessed is the nation whose God is the LORD, the people whom he has chosen for his own inheritance.
Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
13 The LORD looks from heaven. He sees all the sons of men.
Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
14 From the place of his habitation he looks out on all the inhabitants of the earth,
kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
15 he who fashions all of their hearts; and he considers all of their works.
Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
16 There is no king saved by the multitude of an army. A mighty man is not delivered by great strength.
Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
17 A horse is a vain thing for safety, neither does he deliver any by his great power.
Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
18 Behold, the LORD’s eye is on those who fear him, on those who hope in his loving kindness,
Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
19 to deliver their soul from death, to keep them alive in famine.
kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
20 Our soul has waited for the LORD. He is our help and our shield.
Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
21 For our heart rejoices in him, because we have trusted in his holy name.
Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
22 Let your loving kindness be on us, LORD, since we have hoped in you.
Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.

< Psalms 33 >