< Exodus 8 >

1 Also the Lord seide to Moises, Entre thou to Farao, and thou schalt seie to hym, The Lord seith these thingis, Delyuere thou my puple, that it make sacrifice to me; sotheli if thou nylt delyuere, lo!
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Ukamuwuze Farao kuti, Lolani anthu anga kuti apite, akandipembedze.
2 Y schal smyte alle thi termys with paddoks;
Ndipo ngati simulola kuti apite Ine ndidzalanga dziko lonse la Igupto polidzaza ndi achule.
3 and the flood schal buyle out paddokis, that schulen stie, and schulen entre in to thin hows, and in to the closet of thi bed, and on thi bed, and in to `the hous of thi seruauntis, and in to thi puple, and in to thin ouenes, and in to the relyues of thi metis;
Mtsinje wa Nailo udzadzaza ndi achule. Achulewo adzatuluka ndi kukalowa mʼnyumba yaufumu, ku chipinda chogona ndi pa bedi lako, mʼnyumba za nduna zako ndi pa anthu ako ndi mophikira buledi ndiponso mopangira bulediyo.
4 and the paddoks schulen entre to thee, and to thi puple, and to alle thi seruauntis.
Achulewo adzakulumphira iwe ndi anthu ako ndiponso nduna zako.”
5 And the Lord seide to Moises, Seie thou to Aaron, Hold forth thin hond on the floodis, and on the streemes, and mareis; and bryng out paddoks on the lond of Egipt.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Loza ndodo yako ku mitsinje, ku ngalande ndi ku zithaphwi ndipo pakhale achule pa dziko lonse la Igupto.’”
6 And Aaron helde forth the hond on the watris of Egipt; and paddoks stieden, and hileden the lond of Egipt.
Kotero Aaroni analoza dzanja lake pa madzi a ku Igupto, ndipo achule anatuluka nadzaza dziko lonse la Igupto.
7 Forsothe and the witchis diden in lijk maner bi her enchauntementis; and thei brouyten forth paddoks on the lond of Egipt.
Koma amatsenga anachita zinthu zomwezo mʼmatsenga awo. Iwonso anatulutsa achule mʼdziko lonse la Igupto.
8 Forsothe Farao clepide Moises and Aaron, and seide to hem, Preie ye the Lord, that he do a wei the paddoks fro me, and fro my puple; and Y schal delyuere the puple, that it make sacrifice to the Lord.
Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”
9 And Moises seide to Farao, Ordeyne thou a tyme to me, whanne Y schal preie for thee, and for thi seruauntis, and for thi puple, that the paddokis be dryuun awei fro thee, and fro thin hows, and fro thi seruauntis, and fro thi puple; and dwelle oneli in the flood.
Mose anati kwa Farao, “Inu mungonditchulira nthawi imene mukufuna kuti ndikupempherereni, nduna zanu pamodzi ndi anthu anu kuti achule achoke mʼnyumba zanu ndi kuti atsale okhawo ali mu mtsinje wa Nailo.”
10 And he answeride, To morewe. And Moises seide, Y schal do bi thi word, that thou wite, that noon is as oure Lord God; and the paddoks schulen go awei fro thee,
Farao anati, “Mawa.” Mose anamuyankha kuti, “Chabwino zidzakhala monga mwaneneramu, kuti mudzadziwe kuti palibe wina wofanana ndi Yehova Mulungu wathu.
11 and fro thin hous, and fro thi children, and fro thi seruauntis, and fro thi puple; and tho schulen dwelle oneli in the flood.
Achule adzachoka mʼnyumba yanu, mʼnyumba za nduna zanu pamodzi ndi za anthu anu. Koma adzatsala mu mtsinje wa Nailo basi.”
12 And Moises and Aaron yeden out fro Farao. And Moises criede to the Lord, for the biheest of paddoks, which he hadde seid to Farao.
Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao.
13 And the Lord dide bi the word of Moises; and the paddoks weren deed fro housis, and fro townes, and fro feeldis;
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa
14 and thei gaderiden tho in to grete heepis, and the lond was rotun.
Aigupto anawunjika achulewo milumilu ndipo dziko linanunkha.
15 Sotheli Farao seiy that reste was youun, and he made greuous his herte, and herde not hem, as the Lord comaundide.
Koma Farao ataona kuti zinthu zinayambanso kukhala bwino, anawumitsanso mtima wake ndipo sanamverenso mawu a Mose ndi Aaroni, monga momwe Yehova ananenera.
16 And the Lord seide to Moises, Spek thou to Aaron, Holde forth thi yerde, and smyte the dust of erthe, and litle flies, ether gnattis, be in al the lond of Egipt.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti akweze ndodo yake ndi kumenya fumbi la pa nthaka, ndipo fumbilo lidzasanduka nsabwe pa dziko lonse la Igupto.”
17 And thei diden so; and Aaron helde forth the hond, and helde the yerde, and smoot the duste of erthe; and gnattis weren maad in men, and in werk beestis; al the dust of erthe was turned in to gnattis bi al the lond of Egipt.
Iwo anachita momwemo, ndipo pamene Aaroni anakweza ndodo yake ndi kumenya fumbi, nsabwe zinafika pa munthu aliyense ndi pa ziweto. Fumbi lonse la mʼdziko la Igupto linasanduka nsabwe.
18 And witchis diden in lijk maner bi her enchauntementis, that thei schulden brynge forth gnattis, and thei miyten not; and gnattis weren as wel in men as in werk beestis.
Koma amatsenga atayesa kupanga nsabwe mwa matsenga awo, analephera. Ndipo nsabwezo zinali pa munthu aliyense ndi pa ziweto zawo.
19 And the witchis seiden to Farao, This is the fyngur of God. And the herte of Farao was maad hard, and he herde not hem, as the Lord comaundide.
Amatsenga anati kwa Farao, “Izi wachita ndi Mulungu.” Koma mtima wa Farao unali wowumabe ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananenera.
20 And the Lord seide to Moises, Rise thou eerli, and stonde bifore Farao, for he schal go out to the watris; and thou schalt seie to hym, The Lord seith these thingis, Delyuere thou my puple, that it make sacrifice to me;
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mmawa, upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso pamene azidzapita ku madzi ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Lola anthu anga kuti apite akandipembedze.
21 that if thou schalt not delyuere the puple, lo! Y schal sende in to thee, and in to thi seruauntis, and in to thi puple, and in to thin housis, al the kynde of flies; and the housis of Egipcians schulen be fillid with flies of dyuerse kyndis, and al the lond in which thei schulen be.
Koma ngati suwalola anthu anga kuti apite, Ine ndidzatumiza pa iwe ntchentche zoluma ndi pa nduna zako ndi anthu ako ndi mʼnyumba zanu. Mʼnyumba za Aigupto mudzadzaza ntchentche zoluma. Ngakhale pa nthaka pamene akhalapo padzadzaza ndi ntchentche zoluma.’”
22 And in that dai Y schal make wondurful the lond of Gessen, in which my puple is, that flies be not there; and that thou wite that Y am the Lord in the myddis of erthe;
“Koma pa tsikulo ndidzapatula dera la Goseni, kumene kumakhala anthu anga, motero kuti sikudzakhala ntchentche zoluma. Choncho iwe udzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndikulamulira dziko lino.
23 and Y schal sette departyng bitwixe my puple and thi puple; this signe schal be to morewe.
Ndidzasiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako. Chizindikiro chozizwitsa ichi chidzachitika mawa.”
24 And the Lord dide so. And a moost greuouse flie cam in to the hows of Farao, and of hise seruauntis, and in to al the lond of Egipt; and the lond was corrupt of siche flies.
Ndipo Yehova anachita zimenezi: Ntchentche zoluma zochuluka zinalowa mʼnyumba yaufumu ya Farao ndi nyumba za nduna zake. Choncho ntchentche zolumazi zinawononga dziko lonse la Igupto.
25 And Farao clepide Moises and Aaron, and seide to hem, Go ye, make ye sacrifice to `youre Lord God in this lond.
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kaperekeni nsembe kwa Mulungu wanu mʼdziko lomwe lino.”
26 And Moises seide, It may not be so, for `we schulen offre to oure God the abhomynaciouns of Egipcians; that if we schulen sle bifore Egipcians tho thingis whiche thei worschipen, thei schulen `ouerleie vs with stoonus.
Koma Mose anati, “Sitingathe kutero pakuti nsembe zathu kwa Yehova Mulungu ndi zowayipira Aigupto. Ngati tipereke nsembe zowayipira Aigupto mʼmaso mwawo, adzatiponya miyala kuti tife.
27 We schulen go the weie of thre daies in to wildirnesse, and we schulen make sacrifice to oure Lord God, as he comaundide vs.
Ife tiyenera kuyenda ulendo wa masiku atatu kupita ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wathu monga anatilamulira.”
28 And Farao seide, Y schal delyuere you, that ye make sacrifice to `youre Lord God in deseert; netheles go ye not ferthere; preie ye for me.
Farao anati, “Ine ndikulolani kuti mupite ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma musapite kutali kwambiri. Tsopano ndipempherereni.”
29 And Moises seide, Y schal go out fro thee, and Y schal preie the Lord; and the fli schal go awei fro Farao, and fro hise seruauntis, and puple to morewe; netheles nyle thou more disseyue me, that thou delyuere not the puple to make sacrifice to the Lord.
Mose anayankha kuti, “Ine ndikangochoka pano, ndikapemphera kwa Yehova ndipo mawa lomweli ntchentche zoluma zidzachoka kwa Farao, nduna zake pamodzi ndi anthu ake. Koma Farao, onetsetsani kuti musachitenso zachinyengo ndi kuwakaniza anthu kuti asakapereke nsembe kwa Yehova.”
30 And Moises yede out fro Farao, and preiede the Lord, whiche dide bi the word of Moyses,
Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova.
31 and took awei flies fro Farao, and fro hise seruauntis, and puple; noon lefte, `sotheli nether oon.
Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala.
32 And the herte of Farao was maad hard, so that he delyueride not the puple, sothli nethir in this tyme.
Koma nthawi imeneyinso Farao anawumitsa mtima wake ndipo sanalole kuti anthu atuluke.

< Exodus 8 >