< Esther 9 >

1 Au douzième mois, qui est le mois d'Adar, le treizième jour du mois, lorsque l'ordre du roi et son décret furent sur le point d'être exécutés, le jour où les ennemis des Juifs espéraient les vaincre (mais il arriva que le contraire se produisit, et que les Juifs vainquirent ceux qui les haïssaient),
Pa mwezi wa 12, mwezi wa Adara pa tsiku la 13 la mwezi womwewo, tsiku limene lamulo loyamba lija la mfumu linayembekezereka kuti litsatidwe, pamene adani a Ayuda anati awononge Ayudawo, zinthu zinasintha. Ayuda ndiwo anawononga adani awo.
2 les Juifs se rassemblèrent dans leurs villes, dans toutes les provinces du roi Assuérus, pour porter la main sur ceux qui leur voulaient du mal. Personne ne pouvait leur résister, car la peur d'eux était tombée sur tout le peuple.
Ayuda anasonkhana mʼmizinda ya zigawo zonse za Mfumu Ahasiwero kuthira nkhondo onse amene anafuna kuwawononga. Palibe amene akanalimbana nawo chifukwa anthu onse a mitundu ina anachita nawo mantha.
3 Tous les princes des provinces, les gouverneurs locaux, les gouverneurs et ceux qui s'occupaient des affaires du roi aidaient les Juifs, car la crainte de Mardochée était tombée sur eux.
Ndipo akuluakulu onse a zigawo, akalonga, akazembe ndi ogwira ntchito za mfumu anathandiza Ayuda, chifukwa anachita mantha ndi Mordekai.
4 Car Mardochée était grand dans la maison du roi, et sa renommée se répandait dans toutes les provinces, car l'homme Mardochée devenait de plus en plus grand.
Pajatu Mordekai anali munthu wamkulu mʼnyumba ya ufumu. Mbiri yake inafalikira zigawo zonse, ndipo mphamvu zake zinakulirakulirabe.
5 Les Juifs frappaient tous leurs ennemis par le coup de l'épée, par le massacre et la destruction, et ils faisaient ce qu'ils voulaient à ceux qui les haïssaient.
Motero Ayuda anakantha adani awo onse ndi lupanga, kuwapha ndi kuwawononga, ndipo anachita chimene chinawakomera kwa adani awo.
6 Dans la citadelle de Suse, les Juifs tuèrent et détruisirent cinq cents hommes.
Ku likulu la mzinda wa Susa, Ayuda anapha ndi kuwononga anthu 500.
7 Ils tuèrent Parshandatha, Dalphon, Aspatha,
Ayuda anaphanso Parisandata, Dalifoni, Asipata,
8 Poratha, Adalia, Aridatha,
Porata, Adaliya, Aridata,
9 Parmashta, Arisai, Aridai et Vaizatha,
Parimasita, Arisai, Aridai ndi Vaisata,
10 les dix fils de Haman, fils de Hammedatha, l'ennemi des Juifs, mais ils ne mirent pas la main sur le butin.
ana khumi a Hamani, mwana wa Hamedata, mdani wa Ayuda. Koma sanalande katundu wawo.
11 Ce jour-là, on apporta au roi le nombre de ceux qui avaient été tués dans la citadelle de Suse.
Tsiku lomwelo anawuza mfumu chiwerengero cha anthu amene anaphedwa mu likulu la mzinda wa Susa.
12 Le roi dit à la reine Esther: « Les Juifs ont tué et détruit cinq cents hommes dans la citadelle de Suse, y compris les dix fils d'Haman; qu'ont-ils donc fait dans le reste des provinces du roi? Quelle est ta requête? Elle vous sera accordée. Quelle est votre autre requête? Elle sera exécutée. »
Mfumu inati kwa mfumukazi Estere, “Ayuda apha ndi kuwononga anthu 500 ndi ana khumi a Hamani mu likulu la mzinda wa Susa. Nanga ku zigawo zina zonse za mfumu achitako chiyani? Kodi tsopano ukupemphanso chiyani? Chimene ukupempha ndidzakupatsa. Kodi ukufuna chiyani? Chimene ukufuna ndidzakupatsa.”
13 Alors Esther dit: « Si le roi le veut, qu'il soit accordé aux Juifs qui sont à Suse de faire demain aussi selon le décret d'aujourd'hui, et que les dix fils d'Haman soient pendus au gibet. »
Estere anayankha kuti, “Ngati chingakukomereni mfumu, apatseni chilolezo Ayuda okhala mu Susa kuti achitenso zimene achita lerozi mawa, potsata lamulo ndipo mulole kuti ana khumi a Hamani aja mitembo yawo ipachikidwe pa mtanda.”
14 Le roi ordonna que cela se fasse. Un décret fut publié à Suse, et l'on pendit les dix fils d'Haman.
Choncho mfumu inalamula kuti izi zichitike. Anapereka lamulo mu Susa ndipo mitembo ya ana khumi a Hamani anayipachika pa mtanda.
15 Les Juifs qui étaient à Suse se rassemblèrent le quatorzième jour du mois d'Adar et tuèrent trois cents hommes à Suse, mais ils ne mirent pas la main sur le butin.
Ayuda a mu mzinda wa Susa anasonkhana pamodzi pa tsiku la 14 la mwezi wa Adara ndipo anapha anthu 300 mu Susa, koma sanatenge katundu wawo.
16 Les autres Juifs qui étaient dans les provinces du roi se rassemblèrent, défendirent leur vie, se reposèrent de leurs ennemis et tuèrent soixante-quinze mille de ceux qui les haïssaient; mais ils ne mirent pas la main sur le butin.
Tsono Ayuda ena onse amene anali mu zigawo za mfumu anasonkhananso kudziteteza ndipo sanasautsidwenso ndi adani popeza anapha anthu 75,000 koma sanalande zofunkha zawo.
17 Cela se passa le treizième jour du mois d'Adar, et le quatorzième jour de ce mois, ils se reposèrent et en firent un jour de fête et de réjouissance.
Zonsezi zinachitika pa tsiku la 13 la mwezi wa Adara ndipo pa tsiku la 14 anapumula ndi kupanga tsikuli kuti likhale la madyerero ndi chikondwerero.
18 Mais les Juifs qui étaient à Suse s'assemblèrent le treizième et le quatorzième jour du mois; et le quinzième jour de ce mois, ils se reposèrent, et en firent un jour de fête et de réjouissance.
Koma Ayuda okhala mu Susa anasonkhana pa tsiku la 13 ndi la 14 ndipo anakonza tsiku la 15 kuti likhale tsiku la madyerero ndi chikondwerero.
19 C'est pourquoi les Juifs des villages, qui habitent dans les villes non fortifiées, font du quatorzième jour du mois d'Adar un jour de fête et de réjouissance, un jour férié, et un jour où l'on s'envoie des présents alimentaires.
Ichi ndi chifukwa chake Ayuda a ku midzi, amene amakhala mʼzithando amasunga tsiku la 14 la mwezi wa Adara ngati la madyerero ndi chikondwerero, tsiku lopatsana mphatso.
20 Mardochée écrivit ces choses, et il envoya des lettres à tous les Juifs qui se trouvaient dans toutes les provinces du roi Assuérus, tant de près que de loin,
Mordekai analemba mawu awa mʼmakalata ndipo anawatumiza kwa Ayuda onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero, a pafupi ndi a kutali:
21 pour leur enjoindre de célébrer chaque année les quatorzième et quinzième jours du mois d'Adar,
Anati chaka chilichonse, Ayudawo azisunga tsiku la 14 ndi 15 la mwezi wa Adara,
22 comme des jours où les Juifs se sont reposés de leurs ennemis, et comme le mois qui a été transformé pour eux de tristesse en joie, et de deuil en fête; Ils en firent des jours de festin et d'allégresse, où l'on s'envoyait des vivres et des dons aux indigents.
ngati masiku amene Ayuda anapulumutsidwa kwa adani awo, ndiponso ngati mwezi umene chisoni chawo chinasandulika chimwemwe ndi kulira kwawo kunasandulika chikondwerero. Anawalembera kuti azisunga masikuwa ngati masiku a madyerero ndi chikondwerero, masiku opatsana mphatso zachakudya kwa wina ndi mnzake komanso opereka mphatso kwa osauka.
23 Les Juifs acceptèrent la coutume qu'ils avaient commencée, comme Mardochée le leur avait écrit,
Choncho Ayuda anavomereza kusunga masikuwa ngati a chikondwerero monga analembera Mordekai.
24 car Haman, fils d'Hammedatha, l'Agaguite, ennemi de tous les Juifs, avait formé un complot contre les Juifs pour les détruire, et il avait jeté le Pur, c'est-à-dire le sort, pour les consumer et les faire périr;
Hamani mwana wa Hamedata, Mwagagi, mdani wa Ayuda onse, anakonza chiwembu chakupha ndi kuwononga Ayuda ndipo anachita maere otchedwa Purimu kuti awaphe ndi kuwawononga.
25 mais lorsque le roi en eut connaissance, il ordonna par lettres que le mauvais projet qu'il avait formé contre les Juifs retombe sur sa tête, et que lui et ses fils soient pendus au gibet.
Koma mfumu itazindikira za chiwembuchi, inalamula kuti zilembedwe mʼmakalata kuti chiwembu chimene Hamani anakonzera Ayuda chigwere pa iye mwini, ndi kuti iye pamodzi ndi ana ake apachikidwe pa mtanda.
26 C'est pourquoi ils appelèrent ces jours « Purim », du mot « Pur ». C'est pourquoi, à cause de toutes les paroles de cette lettre, de ce qu'ils avaient vu à ce sujet et de ce qui leur était parvenu,
Ndi chifukwa chake masiku amenewa amatchedwa masiku a Purimu potsata dzina lakuti Purimu. Chifukwa cha kalata ya Mordekai ndiponso chifukwa cha zimene anaziona ndi kuwachitikira,
27 les Juifs établirent et imposèrent à eux-mêmes, à leurs descendants et à tous ceux qui se joindraient à eux, de ne pas manquer de célébrer chaque année ces deux jours selon ce qui était écrit et selon le temps fixé;
Ayuda onse anagwirizana kukhazikitsa lamulo lokhudza iwo, zidzukulu zawo ndi onse amene adzapanga nawo ubale kuti asalephere kusunga masiku awiri amenewa chaka chilichonse monga zinalembedweramo ndiponso potsata nthawi imene anayika.
28 et que l'on se souvienne de ces jours et qu'on les garde dans toutes les générations, dans toutes les familles, dans toutes les provinces et dans toutes les villes, et que ces jours de Pourim ne disparaissent pas du milieu des Juifs, et que leur souvenir ne disparaisse pas de leur descendance.
Azisunga ndi kukumbukira masiku amenewa mu mʼbado uliwonse ndi banja lililonse, mʼchigawo chilichonse ndi mu mzinda uliwonse. Ndipo Ayuda asadzasiye kukondwerera masiku a Purimuwa ndiponso zidzukulu zawo zisadzaleke kuwakumbukira.
29 Alors la reine Esther, fille d'Abihail, et Mardochée, le Juif, écrivirent avec toute l'autorité voulue pour confirmer cette seconde lettre des Pourim.
Choncho mfumukazi Estere, mwana wa mkazi wa Abihaili, pamodzi ndi Mordekai Myuda analemba ndi ulamuliro onse kutsimikizira kalata iyi yachiwiri yokhudza Purimu.
30 Il envoya des lettres à tous les Juifs des cent vingt-sept provinces du royaume d'Assuérus, avec des paroles de paix et de vérité,
Ndipo Mordekai anatumiza makalata kwa Ayuda onse ku zigawo 127 za ufumu wa Ahasiwero. Kalatayi inali ya mawu a mtendere ndiponso a kukhulupirika
31 pour confirmer ces jours de Pourim dans leurs temps fixés, comme l'avaient décrété le Juif Mardochée et la reine Esther, et comme ils l'avaient imposé à eux-mêmes et à leurs descendants en ce qui concerne les jeûnes et les deuils.
kuti azisunga masiku a Purimu pa nyengo imene inavomerezeka monga mmene Mordekai Myuda ndi mfumukazi Estere anawalamulira ndiponso monga anadziyikira eni okha ndi zidzukulu zawo zonena za nthawi zawo za kusala zakudya ndi kulira.
32 L'ordre d'Esther confirma ces affaires de Pourim, et cela fut écrit dans le livre.
Lamulo la Estere linakhazikitsa mwambo wa Purimuwu ndipo zinalembedwa mʼmabuku.

< Esther 9 >