< Josué 1 >

1 Après la mort de Moïse, serviteur de Yahvé, Yahvé parla à Josué, fils de Nun, serviteur de Moïse, en disant:
Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
2 « Moïse, mon serviteur, est mort. Maintenant, lève-toi, passe ce Jourdain, toi et tout ce peuple, pour aller dans le pays que je vais leur donner, aux enfants d'Israël.
“Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
3 Je vous ai donné tous les lieux que la plante de votre pied pourra fouler, comme je l'ai dit à Moïse.
Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
4 Depuis le désert et ce Liban jusqu'au grand fleuve, le fleuve Euphrate, tout le pays des Héthiens, et jusqu'à la grande mer vers le coucher du soleil, telle sera votre frontière.
Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
5 Aucun homme ne pourra se tenir devant toi tous les jours de ta vie. Comme j'ai été avec Moïse, je serai avec toi. Je ne te laisserai pas tomber et je ne t'abandonnerai pas.
Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
6 « Sois fort et courageux, car tu feras en sorte que ce peuple hérite du pays que j'ai juré à ses pères de lui donner.
“Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
7 Seulement, soyez forts et très courageux. Prends soin d'observer et de faire selon toute la loi que Moïse, mon serviteur, t'a prescrite. Ne vous en détournez ni à droite ni à gauche, afin que vous ayez du succès partout où vous irez.
Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
8 Ce livre de la loi ne s'éloignera pas de ta bouche, mais tu le méditeras jour et nuit, afin d'observer et de mettre en pratique tout ce qui y est écrit; car c'est alors que tu feras prospérer ton chemin, et c'est alors que tu auras du succès.
Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
9 Ne t'ai-je pas ordonné? Sois fort et courageux. N'aie pas peur. Ne t'effraie pas, ne t'effraie pas, car Yahvé ton Dieu est avec toi partout où tu iras. »
Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
10 Alors Josué donna cet ordre aux officiers du peuple:
Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
11 « Passez au milieu du camp et donnez cet ordre au peuple: « Préparez des vivres, car dans trois jours vous passerez ce Jourdain pour entrer en possession du pays dont Yahvé votre Dieu vous donne la propriété. »"
“Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
12 Josué parla aux Rubénites, aux Gadites et à la demi-tribu de Manassé, et dit:
Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
13 « Souvenez-vous de la parole que Moïse, serviteur de Yahvé, vous a prescrite, en disant: « Yahvé, votre Dieu, vous donne du repos et vous donne ce pays.
“Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
14 Vos femmes, vos petits enfants et vos troupeaux vivront dans le pays que Moïse vous a donné de l'autre côté du Jourdain; mais vous passerez devant vos frères en armes, tous les vaillants hommes, et vous les aiderez
Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
15 jusqu'à ce que Yahvé ait donné à vos frères du repos, comme il vous en a donné, et qu'ils aient aussi possédé le pays que Yahvé votre Dieu leur donne. Alors tu retourneras dans le pays qui t'appartient et tu le posséderas, celui que Moïse, serviteur de Yahvé, t'a donné au-delà du Jourdain, vers le lever du soleil.'"
Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
16 Ils répondirent à Josué en disant: « Nous ferons tout ce que tu nous as ordonné, et nous irons partout où tu nous enverras.
Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
17 De même que nous avons écouté Moïse en toutes choses, de même nous t'écouterons. Seulement, que Yahvé ton Dieu soit avec toi, comme il a été avec Moïse.
Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
18 Quiconque se rebellera contre ton commandement, et n'écoutera pas tes paroles dans tout ce que tu lui ordonneras, sera lui-même mis à mort. Seulement, sois fort et courageux. »
Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”

< Josué 1 >