< Amos 7 >

1 Ceci est la vision que m'a envoyé le Seigneur Dieu; voilà une nuée de sauterelles qui vient de l'orient, et voilà de grandes sauterelles sur les champs du roi Gog.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
2 Et quand elles eurent achevé de dévorer l'herbe de la terre, je dis: Seigneur, Seigneur, sois miséricordieux. Qui relèvera Jacob? car il est réduit à rien.
Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
3 Seigneur, repens-Toi pour cela. Et cela ne sera point, dit le Seigneur.
Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
4 Ceci est la vision que m'a envoyé le Seigneur: Voilà que le Seigneur appela le châtiment par la flamme, et le feu dévora une grande part de l'abîme, et il consuma l'héritage du Seigneur. Ceci est la vision que m'a envoyé le Seigneur
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
5 Je dis: Seigneur, cesse donc; qui relèvera Jacob, car il est réduit à rien?
Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
6 Seigneur, repens-Toi pour cela. Et cela ne sera point, dit le Seigneur.
Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
7 Ceci est la vision que m'a envoyé le Seigneur: Voilà que le Seigneur Se tient debout sur un mur de diamant, et Il avait un diamant à la main.
Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
8 Et le Seigneur me dit: Que vois-tu, Amos? et je dis; Un diamant; et le Seigneur me dit: Voilà que Je mets un diamant sur un diamant entre Moi et Mon peuple d'Israël; Je ne continuerai plus de Me montrer à lui.
Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
9 Mais les autels de la division seront effacés; et les fêtes d'Israël seront délaissées; et Je Me lèverai avec le glaive contre la maison de Jéroboam.
“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
10 Or Amasias, prêtre de Béthel, envoya au roi d'Israël Jéroboam, disant: Amos fait des complots contre toi, au milieu de la maison d'Israël; la terre ne pourrait pas souffrir toutes ses paroles.
Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
11 Car voilà ce que dit Amos: Jéroboam périra par le glaive, et Israël sera emmené captif hors de sa terre.
Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
12 Et Amasias dit à Amos: Ô Voyant, pars, retire-toi dans la terre de Juda; c'est là que tu vivras, et là que tu prophétiseras.
Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
13 Tu ne continueras plus de prophétiser en Béthel; c'est la ville sainte du roi, et la demeure royale.
Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
14 Et Amos répondit, et dit à Amasias: Je n'étais point prophète, ni fils de prophète, mais chevrier; et je cueillais des mûres.
Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
15 Et le Seigneur m'a pris au milieu de mon troupeau, et le Seigneur m'a dit: Pars et prophétise à Mon peuple Israël.
Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
16 Et maintenant écoute la parole du Seigneur: Tu dis: Ne prophétise point sur Israël, et n'ameute pas la foule contre la maison de Jacob.
Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
17 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur: Ta femme se prostituera dans la ville, et tes fils et tes filles périront par le glaive, et tes champs seront partagés au cordeau, et tu mourras en une terre impure, et Israël sera emmené captif hors de sa terre.
“Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”

< Amos 7 >