< Ecclésiaste 10 >

1 Des mouches mortes gâtent une fiole d'huile parfumée; mieux vaut un peu de sagesse qu'une grande gloire avec de la folie.
Monga ntchentche zakufa zimayika fungo loyipa mʼmafuta onunkhira, choncho kupusa pangʼono kumawononganso nzeru ndi ulemu.
2 Le cœur du sage est dans sa main droite; le cœur de l'impie est dans sa main gauche.
Mtima wa munthu wanzeru umamutsogolera bwino, koma mtima wa munthu wopusa umamusocheretsa.
3 Même quand l'insensé chemine dans sa voie, le cœur lui manque, et tout ce qu'il pense n'est que folie.
Chitsiru ngakhale chikamayenda mu msewu, zochita zake ndi zopanda nzeru ndipo chimaonetsa aliyense kuti icho ndi chitsirudi.
4 Si le courroux de celui qui a le pouvoir s'élève contre toi, ne quitte point ta demeure; car le silence sera le meilleur remède à tes offenses.
Ngati wolamulira akukwiyira, usachoke pa ntchito yako; kufatsa kumakonza zolakwa zazikulu.
5 Il est encore un mal que j'ai vu sous le soleil, sortant comme involontairement de la face de celui qui a le pouvoir.
Pali choyipa chimene ndinachiona pansi pano, kulakwitsa kumene kumachokera kwa wolamulira:
6 L'insensé a été promu aux grandeurs, et les riches seront assis au dernier rang.
Zitsiru amazipatsa ntchito zambiri zapamwamba, pamene anthu olemera amawapatsa ntchito zotsika.
7 J'ai vu des serviteurs à cheval, et des princes marcher à pied comme des esclaves.
Ndaona akapolo atakwera pa akavalo, pamene akalonga akuyenda pansi ngati akapolo.
8 celui qui creuse une fosse y tombera, et celui qui détruit une haie, le serpent le mordra.
Amene amakumba dzenje adzagwamo yekha; amene amabowola khoma adzalumidwa ndi njoka.
9 Celui qui ramasse des pierres s'y blessera lui-même, et celui qui fend du bois se met en péril.
Amene amaphwanya miyala adzapwetekedwa ndi miyalayo; amene amawaza nkhuni adzapwetekedwa nazo.
10 Si son fer lui échappe, il en a le visage troublé; cependant il rassemble ses forces, mais alors sa sagesse ne profite pas à cet homme.
Ngati nkhwangwa ili yobuntha yosanoledwa, pamafunika mphamvu zambiri potema, koma luso limabweretsa chipambano.
11 Un charmeur ne tire pas grand profit de son art, si un serpent le mord sans siffler.
Nʼkopanda phindu kudziwa kuseweretsa njoka ngati njokayo yakuluma kale.
12 La grâce découle de la bouche du sage, et les lèvres de l'insensé le font trébucher.
Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa, koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.
13 Il commence par les folies de sa langue; il finit par les méchancetés de ses lèvres.
Chitsiru chimayamba ndi mawu opusa; potsiriza pake zoyankhula zake ndi zamisala
14 Car l'insensé multiplie les paroles. L'homme ne sait ni le passé ni l'avenir; et ce qui viendra après lui, qui le lui prédira?
ndipo chitsiru chimachulukitsa mawu. Palibe amene amadziwa zimene zikubwera mʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika iye akadzafa?
15 Le travail des insensés leur sera funeste, comme celui de l'homme qui ne sait pas le chemin pour aller à la ville.
Chitsiru chimatopa msanga ndi ntchito yochepa; ndipo sichikhala ndi mphamvu zobwererera ku mudzi.
16 Malheur à toi, ville dont le roi est jeune, et où les princes sont à table dès le matin!
Tsoka kwa iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ikali mwana, ndipo atsogoleri ako amakhala pa madyerero mmamawa.
17 Heureuse es-tu, terre dont le roi sera fils d'hommes généreux, et où les princes mangeront au temps opportun, pour soutenir leurs forces, et n'auront pas à rougir de leurs excès.
Wodala iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ndi mwana wolemekezeka ndipo atsogoleri ako amadya pa nthawi yake, kuti apeze mphamvu osati kuti aledzere.
18 Le plancher du paresseux s'affaissera, et, à cause de l'inertie de ses mains, dans sa maison tombera la pluie goutte à goutte.
Ngati munthu ndi waulesi, denga lake limaloshoka; ngati manja ake ndi alobodo nyumba yake imadontha.
19 On leur prépare du pain pour les réjouir, du vin et de l'huile pour égayer leur vie; et ainsi tout obéit à leur argent, mais pour leur honte.
Phwando ndi lokondweretsa anthu, ndipo vinyo ndi wosangalatsa moyo, koma ndalama ndi yankho la chilichonse.
20 Toutefois, même dans le secret de la conscience, ne maudis point le roi; dans ta chambre à coucher, ne maudis point le riche, car quelque oiseau du ciel rapporterait tes paroles, quelque insecte ailé publierait tes discours.
Usanyoze mfumu ngakhale mu mtima mwako, kapena kutukwana munthu wachuma mʼchipinda chako, pakuti mbalame yamlengalenga itha kutenga mawu ako nʼkukafotokoza zomwe wanena.

< Ecclésiaste 10 >