< Ézéchiel 33 >

1 Et la parole du Seigneur me vint, disant:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Fils de l'homme, parle aux enfants de ton peuple, et dis-leur: En toute terre où je conduirai le glaive, et où le peuple, ayant pris l'un de ses hommes, l'aura mis en sentinelle;
“Iwe mwana wa munthu awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Paja zimati ndikatumiza nkhondo mʼdziko anthu a mʼdzikomo amasankha munthu mmodzi pakati pawo kuti akhale mlonda.
3 Si cet homme, voyant le glaive venir sur cette terre, sonne de la trompette pour donner l'alarme au peuple,
Tsono iyeyo amati akaona nkhondo ikubwera amaliza lipenga kuti achenjeze anthuwo.
4 Et si celui qui entend le son de la trompette prête l'oreille et ne se met point sur ses gardes, le glaive viendra et le surprendra; et son sang retombera sur sa tête.
Wina aliyense akamva lipenga koma osasamala, mdani uja akabwera nʼkumupha, ndiye kuti wadziphetsa yekha.
5 Si donc, après avoir entendu le son de la trompette, il ne s'est pas mis sur ses gardes, son sang retombera sur lui; et tel autre qui se sera mis sur ses gardes aura sauvé son âme.
Iye anamva kulira kwa lipenga koma sanalabadire. Ndiye kuti wadziphetsa yekha. Akanasamala kuchenjeza kwa mlonda akanapulumuka.
6 Et si la sentinelle, ayant vu le glaive venir, n'a point sonné de la trompette, si le peuple ne s'est pas mis sur ses gardes, si le glaive, survenant parmi eux, prend une âme, cette âme est prise à cause de son iniquité; mais tout ce sang, je le réclamerai de la main de la sentinelle.
Koma ngati mlondayo aona lupanga likubwera ndipo osawomba lipengalo kuchenjeza anthu, ndipo lupanga libwera ndi kuchotsa moyo wa mmodzi mwa iwo, munthu ameneyo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma ndidzamuyimba mlandu mlondayo chifukwa cha imfa ya mnzakeyo.’
7 Et toi, fils de l'homme, je t'ai mis en sentinelle pour la maison de Jacob, et tu écouteras toute parole de ma bouche.
“Tsono iwe mwana wa munthu, ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Choncho imva mawu amene ndikuyankhula ndipo uwachenjeze.
8 Si je dis au pécheur: Tu mourras de mort; et que tu ne parles pas pour avertir l'impie de se retirer de ses voies, lui-même, l'impie, mourra en son iniquité; mais son sang, je le réclamerai de ta main.
Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe munthu woyipa, udzafa ndithu,’ ndipo iwe osayankhula kumuchenjeza kuti aleke njira zake, munthu wochimwayo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
9 Que si tu as averti l'impie de se retirer de sa voie, et qu'il ne s'en retire pas, il mourra en son impiété, mais tu auras sauvé ton âme.
Koma ngati uchenjeza munthu woyipa kuti aleke njira zake, ndipo iye osatero, adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
10 Et toi, fils de l'homme, dis à la maison d'Israël: Voici ce que vous dites: Nos fautes et nos iniquités sont sur nous, nous languissons à cause d'elles; et comment vivrons-nous?
“Iwe mwana wa munthu, akumbutse Aisraeli mawu awo akuti, ‘Ife talemedwa ndi zolakwa zathu ndi machimo athu, ndipo tikuwonda chifukwa cha zimene tachita. Kodi tingakhale ndi moyo bwanji?’”
11 Réponds-leur: Par ma vie, dit le Seigneur, je ne désire point la mort des impies; je désire bien plus que l'impie se retire de sa voie, et qu'il vive. Retirez-vous tous de votre voie; car pourquoi péririez-vous, maison d'Israël?
Uwawuze kuti, Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Pali Ine wamoyo, sindikondwera ndi imfa ya munthu woyipa. Ndimakondwera ndikamaona munthu woyipa akuleka zoyipa zake kuti akhale ndi moyo. Tembenukani! Tembenukani, siyani makhalidwe anu oyipa! Muferanji, Inu Aisraeli?
12 Dis aux enfants de mon peuple: La justice du juste ne le sauvera point le jour où il s'égare; l'iniquité de l'impie ne le perdra pas le jour où il sortira de son iniquité; et le juste même ne pourra être sauvé.
“Tsono iwe mwana wa munthu, awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Ngati munthu wolungama achimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwino zija sizidzamupulutsa. Koma wochimwa akaleka ntchito zake zoyipazo, sadzalangidwa konse. Ndithu ngati munthu wolungama ayamba kuchimwa sadzatha kukhala ndi moyo chifukwa cha ntchito zake zabwino zija.’
13 Lorsque j'aurai dit au juste: Tu vivras; si, se confiant à sa justice, il commet une iniquité, toutes ses actions justes seront mises en oubli; il mourra dans l'iniquité qu'il aura commise.
Ngati ndiwuza munthu wolungama kuti adzafa ndithu, koma iyeyo nʼkumadalira ntchito zake zabwino zimene anachita kale ndi kuyamba kuchimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwinozo zidzayiwalika. Iye adzafa chifukwa cha machimo ake.
14 Lorsque j'aurai dit à l'impie: Tu mourras de mort; s'il se retire de son péché, je le jugerai et le traiterai avec justice et discernement.
Ndipo ngati ndiwuza munthu woyipa kuti, ‘Udzafa ndithu,’ tsono iye nʼkutembenuka kuleka machimo ake ndi kuyamba kuchita zimene Yehova afuna,
15 S'il rend le gage, s'il restitue ce qu'il a dérobé, s'il marche dans les commandements de vie et ne fait rien d'inique, il vivra et ne mourra point.
monga kubweza chimene anatenga ngati chikole cha ngongole, kubweza chimene anaba, kutsatira malamulo omwe amapereka moyo ndi kuleka kuchita zoyipa, iye adzakhala ndithu ndi moyo; sadzafa.
16 Tous ses péchés seront mis en oubli; et parce qu'il aura pratiqué l'équité et la justice, il vivra dans sa justice et son équité.
Ndidzakhululuka machimo ake onse anachita. Iye wachita zimene ndi zolungama ndi zoyenera ndipo iye adzakhala ndi moyo ndithu.
17 Les fils de mon peuple diront encore: La voie du Seigneur n'est pas droite. Mais c'est leur voie qui n'est pas droite!
“Komabe anthu a mtundu wako akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, koma makhalidwe awo ndiwo ali osalungama.
18 Le juste qui se détournera de sa justice et fera des iniquités mourra dans ses iniquités.
Ngati munthu wolungama atembenuka ndi kuleka ntchito zake zolungama ndi kuyamba kuchita zoyipa, adzafa nazo.
19 Le pécheur qui sortira de son iniquité et agira selon l'équité et la justice, vivra dans la justice et l'équité.
Ndipo ngati munthu woyipa atembenuka ndi kuleka ntchito zake zoyipa ndi kuyamba kuchita zolungama ndi zoyenera, iye adzakhala ndi moyo pochita zimenezo.
20 Et voici ce que vous dites: La voie du Seigneur n'est pas droite! Je vous jugerai tous, chacun selon sa voie, maison d'Israël.
Koma Inu Aisraeli, mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, inu Aisraeli, Ine ndidzaweruza aliyense wa inu potsata ntchito zake.”
21 Et en la douzième année de notre captivité, le douzième mois, le cinquième jour du mois, un homme qui s'était sauvé de Jérusalem vint me trouver, disant: La ville est prise!
Pa tsiku lachisanu la mwezi wakhumi, chaka chakhumi ndi chiwiri cha ukapolo wathu, munthu wina amene anapulumuka ku Yerusalemu anabwera kudzandiwuza kuti, “Mzinda wagwa!”
22 Et avant qu'il vînt, le soir, la main du Seigneur avait été sur moi; et le Seigneur m'ouvrit la bouche, quand le matin cet homme vint chez moi. Et ma bouche ouverte ne put se contenir.
Tsono madzulo ake munthuyo asanafike, dzanja la Yehova linali pa ine. Koma mmawa mwake munthuyo atabwera Yehova anatsekula pakamwa panga, motero kuti sindinakhalenso wosayankhula.
23 Et la parole du Seigneur me vint, disant:
Ndipo Yehova anandiyankhula kuti:
24 Fils de l'homme, ceux qui habitent les villes dévastées de la terre d'Israël disent: Abraham était seul, et il a possédé cette terre; nous, nous sommes nombreux; c'est donc à nous que cette terre a été donnée pour héritage.
“Iwe mwana wa munthu, anthu amene akukhala mʼmizinda ya mabwinja ya dziko la Israeli akunena kuti, ‘Abrahamu anali munthu mmodzi yekha, ndipo anamupatsa dziko lonse. Koma ife tilipo ambiri, motero tsono dzikolo ndi lathu.’
25 À cause de cela, réponds-leur: Voici ce que dit le Seigneur Maître:
Choncho iwe uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Inu mumadya nyama ili ndi magazi ake, ndipo mumapembedza mafano ndi kukhetsa magazi, kodi tsono inu nʼkulandira dzikoli?
26 Par ma vie, ceux qui sont en ces villes désolées périront par le glaive; et ceux qui demeurent aux champs seront donnés en pâture aux bêtes sauvages; et je ferai mourir de mort ceux qui sont dans des forteresses et dans des cavernes.
Mumadalira lupanga lanu, mumachita zinthu zonyansa, ndipo aliyense wa inu amachita chigololo ndi mkazi wa mnzake. Kodi inu nʼkulandira dzikoli?’
27 Par ma vie, ceux qui sont en ces villes désolées périront par le glaive; et ceux qui demeurent aux champs seront donnés en pâture aux bêtes sauvages; et je ferai mourir de mort ceux qui sont dans des forteresses et dans des cavernes.
“Uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Ndithu pali Ine wamoyo, anthu amene anatsala mʼmizinda ya mabwinja adzaphedwa ndi lupanga, amene ali ku midzi ndidzawapereka kuti adzadyedwe ndi zirombo zakuthengo, ndipo amene ali mʼmalinga ndi mʼmapanga adzafa ndi mliri.
28 Et je ferai de la terre un désert; et la superbe de leur force périra; et les montagnes d'Israël seront une solitude, car nul n'y passera plus.
Ndidzalisandutsa chipululu dzikolo, ndipo mphamvu zake zimene amanyadira zidzatheratu, ndipo mapiri a Yerusalemu adzasanduka chipululu, kotero kuti palibe amene adzatha kudutsako.
29 Et ils sauront que je suis le Seigneur; et je ferai de leur héritage un désert, et il sera dévasté à cause de toutes les abominations qu'ils y ont commises.
Ndikadzasandutsa dzikolo chipululu chifukwa cha zonyansa zimene ankachita, pamenepo ndiye adzadziwa kuti ndine Yehova.’
30 Et toi, fils de l'homme, les enfants de ton peuple parlent de toi dans leurs demeures, et devant les portes de leurs maisons, et ils se disent l'un à l'autre: Allons ensemble, et écoutons quelles paroles nous viennent aujourd'hui du Seigneur!
“Koma kunena za iwe, mwana wa munthu, anthu a mtundu wako akumayankhula za iwe akakhala pa makoma a mzinda ndi pa makomo a nyumba zawo. Akumawuzana kuti, ‘Tiyeni tikamve uthenga umene wachokera kwa Yehova.’
31 Ils s'approchent de toi comme un peuple qui s'assemble, et ils s'assoient devant toi, et ils écoutent tes paroles, mais ils ne les pratiquent point; car le mensonge est dans leur bouche, et leur cœur marche à la suite de leur impureté.
Anthu anga amabwera kwa iwe, monga momwe amachitira nthawi zonse anthu anga, ndipo amakhala pansi pamaso pako kumvetsera mawu ako. Koma zimene akumvazo sazichita. Zokamba zawo zimaonetsa chikondi, koma mitima yawo imakhala pa phindu lawo.
32 Et tu es pour eux comme le son d'une harpe douce et harmonieuse; et ils écoutent tes paroles, mais ils ne les pratiquent point.
Kunena zoona, kwa iwowo sindiwe kanthu konse, ndiwe munthu wamba chabe womangoyimba nyimbo zachikondi ndi liwu lokoma poyimba zeze. Kumva amamva mawu ako koma sawagwiritsa ntchito.
33 Et quand le jour sera venu ils diront: Voilà que les choses sont accomplies; et ils sauront alors qu'au milieu d'eux il y avait un prophète.
“Koma zonsezi zikadzachitika, ndipo zidzachitika ndithu, pamenepo adzadziwa kuti mneneri anali pakati pawo.”

< Ézéchiel 33 >