< Jérémie 18 >

1 Parole du Seigneur qui est venue à Jérémie, disant:
Yehova anawuza Yeremiya kuti,
2 Lève-toi et entre dans la maison d'un potier, et là tu entendras mes paroles.
“Pita ku nyumba ya munthu wowumba mbiya, ndipo kumeneko ndikakuwuza mawu anga.”
3 Et je descendis dans la maison d'un potier, et voilà qu'il était à l'ouvrage sur sa roue.
Choncho ndinatsikira ku nyumba ya wowumba mbiya, ndipo ndinamuona akuwumba mbiya pa mkombero.
4 Et le vase qu'il faisait se rompit dans ses mains, et il fit aussitôt un autre vase, comme il lui plut de le faire.
Tsono amati ngati mbiya imene waumba ikhala yosawumbika bwino ankayiphwanya nʼkuwumbanso ina monga mmene afunira ndi dothi lake lomwe lija.
5 Et la parole du Seigneur vint à moi, disant:
Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
6 Maison d'Israël, ne puis-je faire avec vous comme ce potier? Voilà que vous êtes dans mes mains comme l'argile du potier.
“Inu Aisraeli, kodi Ine sindingathe kuchita nanu monga amachitira wowumba mbiya?” akutero Yehova. “Inu muli mʼmanja mwanga ngati mtapo mʼmanja mwa wowumba mbiya.
7 Je prononcerai mon souverain jugement contre un peuple ou un royaume, pour le perdre et le détruire.
Ngati nditalengeza kuti mtundu wina wa anthu kapena ufumu wina ndiwuzula, kuwugwetsa ndi kuwuwononga,
8 Mais si cette nation se détourne de tous ses péchés, moi aussi, je me repentirai du mal que je songeais à lui faire;
ndipo ngati mtundu wa anthu umene ndawuchenjezawo ulapa zoyipa zawo, ndiye kuti Ine ndidzaleka ndipo sindidzabweretsa pa anthuwo mavuto amene ndinakonzekera kuwachitira.
9 Et je prononcerai mon jugement contre un peuple ou un royaume, pour le réédifier et le planter.
Ndipo ngati ndilengeza kuti ndikufuna kumanga ndi kukhazikitsa mtundu wa anthu kapena ufumu.
10 Mais s'ils font le mal devant moi, en désobéissant à ma voix, je me repentirai du bien que j'avais promis de leur faire.
Koma mtunduwo ukachita choyipa pamaso panga nʼkusandimvera, ndiye kuti sindidzawuchitiranso zabwino zimene ndimafuna ndiwuchitire.
11 Et maintenant j'ai dit aux hommes de Juda et aux habitants de Jérusalem: Voilà que je forge pour vous des maux, et mes pensées sont contre vous; que chacun se détourne de sa mauvaise voie, et faites des œuvres meilleures.
“Ndipo tsopano kawawuze anthu a ku Yuda ndi amene akukhala mu Yerusalemu kuti, ‘Yehova akuti, Taonani! Ndikukukonzerani mavuto, ndi kuganizira zoti ndikulangeni. Kotero siyani makhalidwe anu oyipa aliyense wa inu, ndipo mukonzenso makhalidwe anu ndi zochita zanu.’
12 Et ils ont répondu: Nous nous conduirons en hommes, et nous irons à ce qui nous fait dévier; et chacun de nous fera ce qui est agréable à son cœur perverti.
Koma iwo adzayankha kuti, ‘Zimenezo nʼzosathandiza. Ife tidzapitiriza kuchita zomwe takonzekera; aliyense wa ife adzatsatira zoyipa za mtima wake wokanika.’”
13 A cause de cela, voici ce que dit le Seigneur: Demandez maintenant, parmi les gentils, qui a jamais entendu parler de choses aussi horribles que celles qu'a faites la vierge d'Israël?
Yehova akuti, “Uwafunse anthu a mitundu ina kuti: Kodi ndani anamvapo zinthu zofanana ndi zimenezi? Israeli amene anali ngati namwali wanga wachita chinthu choopsa kwambiri.
14 Les réservoirs manquent-ils jamais aux rochers, ou la neige au Liban? L'eau poussée par un vent violent se détourne-t-elle de sa voie?
Kodi chisanu chimatha pa matanthwe otsetsereka a phiri la Lebanoni? Kodi madzi ozizira amitsinje ochokera ku phiri la Lebanoni adzamphwa?
15 Mon peuple m'a oublié; ils ont encensé de vaines idoles; ils ont défailli dans leurs voies, abandonnant les sentiers battus, pour marcher en des chemins impraticables;
Komatu anthu anga andiyiwala; akufukiza lubani kwa mafano achabechabe. Amapunthwa mʼnjira zawo zakale. Amayenda mʼnjira zachidule ndi kusiya njira zabwino.
16 Et ils font de leur terre une désolation et un éternel sujet de raillerie; tous ceux qui la traverseront en seront stupéfaits, et ils secoueront la tête.
Dziko lawo amalisandutsa chipululu, chinthu chochititsa manyazi nthawi zonse; onse odutsapo adzadabwa kwambiri ndipo adzapukusa mitu yawo.
17 Comme je disperse un vent brûlant, je les disperserai devant leurs ennemis; je leur ferai voir le jour de leur destruction.
Ngati mphepo yochokera kummawa, ndidzawabalalitsa pamaso pa adani awo; ndidzawafulatira osawathandiza pa tsiku la mavuto awo.”
18 Et ils ont dit: Allons et formons des desseins contre Jérémie. Car la loi ne périra pas chez le prêtre, ni les conseils chez l'homme intelligent, ni la parole chez le prophète; allons, frappons-le de la langue, puis nous entendrons tous ses discours.
Anthuwo anati, “Tiyeni, tipangane zoti timuchitire Yeremiya; pakuti ansembe otiphunzitsa malamulo tidzakhala nawobe. Anthu anzeru otilangiza tidzakhala nawo, ndiponso aneneri otilalikira mawu. Choncho tiyeni timupezere chifukwa ndipo tisamvere chilichonse chimene akunena.”
19 Écoutez-moi, Seigneur, écoutez la voix de ma justification.
Ndipo ndinapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, ndimvereni; imvani zimene adani anga akunena za ine!
20 Est-ce que l'on doit rendre le mal pour le bien, pour qu'ils aient dit des paroles contre mon âme et qu'ils m'aient caché la punition qu'ils me réservent? Souvenez-vous que je me suis tenu devant votre face, pour vous parler en leur faveur et détourner d'eux votre colère.
Kodi chinthu choyipa nʼkukhala dipo la chinthu chabwino? Komabe iwo andikumbira dzenje. Kumbukirani kuti ndinadzayima pamaso panu kudzawapempherera kuti muwachotsere mkwiyo wanu.
21 A cause de cela, faites que leurs fils soient consumés par la faim, et rassemblez-les pour les livrer aux mains armées de glaives. Que leurs femmes deviennent stériles et veuves; que leurs époux soient frappés de mort, que leurs jeunes gens tombent percés de l'épée dans le combat.
Choncho langani ana awo ndi njala; aperekeni kuti aphedwe ndi lupanga. Akazi awo asanduke opanda ana ndi amasiye; amuna awo aphedwe ndi mliri, anyamata awo aphedwe ndi lupanga ku nkhondo.
22 Qu'il y ait des cris en leurs demeures; amenez soudain sur eux des brigands, parce qu'ils ont cherché à me surprendre, et ont caché des filets sous mes pas.
Kulira kumveke kuchokera mʼnyumba zawo mutawatumizira gulu lankhondo mwadzidzidzi kuti liwakanthe. Iwo andikumbira dzenje kuti ndigweremo ndipo atchera msampha mapazi anga.
23 Et vous, Seigneur, vous connaissez leur dessein de me mettre à mort; ne les absolvez pas de leurs iniquités, et que leurs péchés ne soient pas effacés devant vos yeux; qu'ils soient impuissants devant vous, et que votre colère éclate sur eux en son temps.
Koma Inu Yehova, mukudziwa ziwembu zawo zonse zofuna kundipha. Musawakhululukire zolakwa zawo kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu. Agonjetsedwe pamaso panu; muwalange muli wokwiya.”

< Jérémie 18 >