< Job 33 >

1 Cependant Job écoute mes paroles, prête une oreille attentive à ce que je vais dire.
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 Tu vois j'ouvre la bouche et ma langue se meut.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 La pureté de mon cœur se manifestera en mes discours; mes lèvres ne laisseront passer que des sentences irréprochables.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 L'esprit divin m'anime; le souffle du Tout-Puissant m'a instruit.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 Tu me répondras, si tu le peux; attends et tenons-nous face à face.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Je suis comme toi formé de boue; nous provenons du même Créateur.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 Je ne veux ni me faire craindre, ni te troubler; ma main ne te sera pas pesante.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 Je n'ai rien perdu de ta défense, mes oreilles l'ont recueillie tout entière; tu as dit:
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 Je suis pur, je ne pèche point; je suis irréprochable, car j'observe les lois.
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Dieu a trouvé sujet de m'accuser; il m'a jugé comme un ennemi.
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 Il a mis mon pied dans une entrave; il a posé des sentinelles sur toutes mes voies.
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 Comment as-tu osé dire: Je suis juste et Dieu ne m'a pas exaucé? L'Eternel n'est-il pas au-dessus de tous les humains?
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Tu as dit: Pourquoi Dieu n'a-t-il pas écouté un seul mot de ma cause?
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 Ce que le Seigneur a dit une fois, il le répète encore.
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 En nos songes ou dans nos méditations nocturnes, à l'heure où les hommes assoupis sur leur couche ressentent une terreur surnaturelle,
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 Il découvre leurs pensées; il donne une forme à leurs craintes secrètes; il les épouvante;
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 Il les détourne de l'iniquité; il préserve leur corps de la chute.
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 A de tels humains, il a déjà sauvé la vie; il l'a empêché de succomber dans les batailles.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 Pour le blâmer derechef, il l'étend malade sur son lit; il engourdit tous ses os.
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 Et l'homme ne peut goûter d'aucun aliment; et son âme en désirera,
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 Jusqu'à ce que ses chairs pourrissent et que ses os vides de mœlle se montrent à nu.
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 Son âme s'est approchée de la mort et sa vie de l'enfer. (questioned)
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 Mais, y eût-il là mille anges exterminateurs, pas un seul ne le blessera, si son cœur songe à se convertir à Dieu: le Seigneur lui fera connaître ce qu'il lui reproche; il lui montrera sa folie;
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 Il empêchera la mort de le saisir; il renouvellera son corps comme l'enduit d'un mur; il remplira ses os de mœlle;
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 Il lui rendra des chairs délicates comme celles d'un enfant; il lui rendra sa virilité parmi les hommes.
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 Ses prières au Seigneur seront exaucées; il verra le front serein, les manifestations de Dieu; il rendra justice à ses semblables.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 Alors il se fera des reproches en lui-même, disant: Qu'ai-je fait? Je n'ai point été puni comme le méritaient mes péchés.
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 Mon Dieu, préservez mon âme d'entrer dans la perdition, et ma vie verra la lumière.
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 Voilà donc ce que, de trois manières, le Tout-Puissant fait pour chacun des mortels.
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 C'est lui qui a protégé mon âme contre la mort, afin qu'à la lumière, ma vie chante ses louanges.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Prête l'oreille, Job; écoute-moi, garde le silence, c'est à moi seul de parler.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 Cependant, si tu as de bonnes raisons, réponds-moi; parle, je veux avec toi être juste;
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 Sinon, écoute; garde le silence et je t'instruirai.
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< Job 33 >