< Psaumes 19 >

1 Jusqu'à la Fin, psaume de David. Les cieux racontent la gloire du Seigneur, et le firmament fait connaître l'œuvre de ses mains.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
2 Le jour parle de lui au jour; la nuit montre sa science à la nuit.
Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
3 Il n'y a langage ni paroles dont leur voix ne soit entendue.
Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
4 Leur voix s'est répandue sur toute la terre; leur parole est parvenue au bout du monde. Il a tendu son tabernacle dans le soleil;
Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
5 Et le soleil ressemble au jeune époux sortant de son lit nuptial, il a tressailli de joie comme un géant pour courir dans sa voie.
Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
6 Il sort de l'extrémité du ciel; et son issue est à l'autre extrémité; et nul ne peut se mettre à l'abri de sa chaleur.
Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
7 La loi du Seigneur est immaculée, elle convertit les âmes; le témoignage du Seigneur est fidèle, il donne la sagesse aux enfants.
Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
8 La justice du Seigneur est droite, elle réjouit le cœur; les préceptes du Seigneur brillent d'un vif éclat, ils éclairent les yeux.
Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
9 La crainte du Seigneur est sainte, elle persiste dans les siècles des siècles; les jugements du Seigneur sont vrais, et justifiés en eux-mêmes.
Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
10 Ils sont infiniment plus désirables que l'or et les pierres précieuses; ils sont plus doux que le miel et que les rayons de miel.
ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
11 Aussi ton serviteur les garde-t-il; à les garder on gagne un riche salaire.
Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
12 Qui a conscience de ses chutes? Purifies-moi de mes fautes les plus cachées.
Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
13 Préserve ton serviteur des vices des étrangers. S'ils ne me dominent pas, alors je serai sans souillure et lavé d'un grand péché.
Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
14 Alors les paroles de ma bouche te plairont, et les pensées de mon cœur seront toujours agréables devant toi. Seigneur, tu es mon aide et mon Rédempteur.
Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.

< Psaumes 19 >