< Job 25 >

1 Bildad de Schuach prit la parole et dit:
Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 La puissance et la terreur appartiennent à Dieu; Il fait régner la paix dans ses hautes régions.
“Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu, Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
3 Ses armées ne sont-elles pas innombrables? Sur qui sa lumière ne se lève-t-elle pas?
Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka? Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
4 Comment l’homme serait-il juste devant Dieu? Comment celui qui est né de la femme serait-il pur?
Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu? Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
5 Voici, la lune même n’est pas brillante, Et les étoiles ne sont pas pures à ses yeux;
Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni, ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
6 Combien moins l’homme, qui n’est qu’un ver, Le fils de l’homme, qui n’est qu’un vermisseau!
nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi, mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”

< Job 25 >