< 1 Chroniques 21 >

1 Mais Satan s'éleva contre Israël, et incita David à faire le dénombrement d'Israël.
Satana anafuna kuvutitsa Aisraeli choncho anawutsa mtima wa Davide kuti awerenge Aisraeli.
2 Et David dit à Joab et aux principaux du peuple: Allez [et] dénombrez Israël, depuis Béer-sebah jusqu'à Dan, et rapportez-le moi, afin que j'en sache le nombre.
Choncho Davide anati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo, “Pitani mukawerenge Aisraeli kuyambira ku Beeriseba mpaka ku Dani. Ndipo mudzandiwuze kuti ndidziwe chiwerengero chawo.”
3 Mais Joab répondit: Que l'Eternel veuille augmenter son peuple cent fois autant qu'il est, ô Roi mon Seigneur! tous ne sont-ils pas serviteurs de mon Seigneur? Pourquoi mon Seigneur cherche-t-il cela? [et] pourquoi cela serait-il imputé comme un crime à Israël?
Yowabu anayankha kuti, “Yehova achulukitse ankhondo ake kukhala miyandamiyanda. Mbuye wanga mfumu, kodi anthu onsewa sali pansi panu? Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mukufuna kuchita zimenezi? Nʼchifukwa chiyani mukufuna kuchimwitsa Israeli?”
4 Mais la parole du Roi l'emporta sur Joab; et Joab partit, et alla par tout Israël; puis il revint à Jérusalem.
Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu, kotero Yowabu anapita mu Israeli monse ndipo kenaka anabwera ku Yerusalemu.
5 Et Joab donna à David le rôle du dénombrement du peuple, et il se trouva de tout Israël onze cent mille hommes tirant l'épée, et de Juda, quatre cent soixante et dix mille hommes, tirant l'épée.
Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa Davide: Mu Israeli monse munali anthu ankhondo 1,100,000 amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga, kuphatikizapo anthu 470,000 a fuko la Yuda.
6 Bien qu'il n'eût pas compté entr'eux Lévi ni Benjamin, parce que Joab exécutait la parole du Roi à contre-cœur.
Koma Yowabu sanaphatikizepo fuko la Levi ndi fuko la Benjamini pa chiwerengerochi, pakuti lamulo la mfumu linamuyipira.
7 Or cette chose déplut à Dieu, c'est pourquoi il frappa Israël.
Lamulo limeneli silinakomerenso Mulungu. Kotero Iye analanga Israeli.
8 Et David dit à Dieu: J'ai commis un très-grand péché d'avoir fait une telle chose; je te prie pardonne maintenant l'iniquité de ton serviteur, car j'ai agi très-follement.
Choncho Davide anati kwa Mulungu, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”
9 Et l'Eternel parla à Gad, le Voyant de David, en disant:
Yehova anati kwa Gadi, mlosi wa Davide,
10 Va, parle à David, et lui dis: Ainsi a dit l'Eternel, je te propose trois choses; choisis l'une d'elles, afin que je te la fasse.
“Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’”
11 Et Gad vint à David, et lui dit: Ainsi a dit l'Eternel:
Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa Iye, “Yehova akuti, ‘Musankhepo chimene mungakonde kuti chichitike:
12 Choisis ou la famine durant l'espace de trois ans; ou d'être consumé, durant trois mois, étant poursuivi de tes ennemis, en sorte que l'épée de tes ennemis t'atteigne; ou que l'épée de l'Eternel, c'est-à-dire, la mortalité, soit durant trois jours sur le pays, et que l'Ange de l'Eternel fasse le dégât dans toutes les contrées d'Israël. Maintenant donc regarde ce que j'aurai à répondre à celui qui m'a envoyé.
mʼdziko mukhale njala zaka zitatu, mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu, akukukanthani ndi lupanga la Yehova, kapena mʼdziko mukhale mliri kwa masiku atatu, mngelo wa Yehova akuwononga Israeli yense.’ Ndipo tsono ganizirani bwino chomwe ndikamuyankhe amene wandituma.”
13 Alors David répondit à Gad: Je suis dans une très-grande angoisse; que je tombe, je te prie, entre les mains de l'Eternel, parce que ses compassions sont en très grand nombre; mais que je ne tombe point entre les mains des hommes!
Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ine andilange ndi Yehova, pakuti chifundo chake ndi chachikulu kwambiri; koma ndisalangidwe ndi anthu.”
14 L'Eternel envoya donc la mortalité sur Israël; et il tomba soixante et dix mille hommes d'Israël.
Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, ndipo unapha Aisraeli 70,000.
15 Dieu envoya aussi l'Ange à Jérusalem pour y faire le dégât; et comme il faisait le dégât, l'Eternel regarda, [et] se repentit de ce mal; et il dit à l'Ange qui faisait le dégât: C'est assez; retire à présent ta main. Et l'Ange de l'Eternel était auprès de l'aire d'Ornan Jébusien.
Ndipo Mulungu anatumiza mngelo kuti awononge Yerusalemu. Koma pamene mngeloyo amachita zimenezi, Yehova anaona ndipo anavutika mu mtima chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
16 Or David élevant ses yeux vit l'Ange de l'Eternel qui était entre la terre et le ciel, ayant dans sa main son épée nue, tournée contre Jérusalem. Et David et les Anciens couverts de sacs, tombèrent sur leurs faces.
Davide anakweza maso ake ndipo anaona mngelo wa Yehova atayima pakati pa dziko lapansi ndi kumwamba, mʼdzanja lake muli lupanga lotambalitsa kuloza ku Yerusalemu. Ndipo Davide ndi akuluakulu, atavala ziguduli, anadzigwetsa pansi chafufumimba.
17 Et David dit à Dieu: N'est-ce pas moi qui ai commandé qu'on fit le dénombrement du peuple? c'est donc moi qui ai péché et qui ai très-mal agi; mais ces brebis qu'ont-elles fait? Eternel mon Dieu! je te prie que ta main soit contre moi, et contre la maison de mon père, mais qu'elle ne soit pas contre ton peuple, pour le détruire.
Davide anati kwa Mulungu, “Kodi si ine amene ndinalamula kuti ankhondo awerengedwe? Ine mʼbusa ndi amene ndachimwa, ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Inu Yehova Mulungu wanga, langani ineyo pamodzi ndi banja langa, koma musalole kuti mliriwu ukhale pa anthu anuwa.”
18 Alors l'Ange de l'Eternel commanda à Gad de dire à David, qu'il montât pour dresser un autel à l'Eternel, dans l'aire d'Ornan Jébusien.
Pamenepo mngelo wa Yehova analamula Gadi kuti awuze Davide kuti akamange guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
19 David donc monta selon la parole que Gad [lui] avait dite au nom de l'Eternel.
Ndipo Davide anapita pomvera mawu amene Gadi ananena mʼdzina la Yehova.
20 Et Ornan s'étant retourné, et ayant vu l'Ange, se tenait caché avec ses quatre fils. Or Ornan foulait du blé.
Pamene Arauna ankapuntha tirigu, anatembenuka ndipo anaona mngelo ndipo ana ake anayi aamuna amene anali naye anabisala.
21 Et David vint jusqu'à Ornan; et Ornan regarda, et ayant vu David, il sortit de l'aire, et se prosterna devant lui, le visage en terre.
Davide anayandikira, ndipo Arauna atayangʼana ndi kumuona, anachoka popunthira tirigupo ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi pamaso pa Davide.
22 Et David dit à Ornan: Donne-moi la place de cette aire, et j'y bâtirai un autel à l'Eternel; donne-la-moi pour le prix qu'elle vaut, afin que cette plaie soit arrêtée de dessus le peuple.
Davide anati kwa Arauna, “Undipatse malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe, kuti mliri uli pa anthuwa usiye. Undigulitse ine pa mtengo woyenera ndithu.”
23 Et Ornan dit à David: Prends-la, et que le Roi mon Seigneur fasse tout ce qui lui semblera bon. Voici, je donne ces bœufs pour les holocaustes, et ces instruments à fouler du blé, au lieu de bois, et ce blé pour le gâteau; je donne toutes ces choses.
Arauna anati kwa Davide, “Tengani! Mbuye wanga mfumu achite chomukomera. Taonani ine ndidzapereka ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, zopunthira tirigu zidzakhala nkhuni ndipo tiriguyu adzakhala chopereka chachakudya. Ndidzapereka zonsezi.”
24 Mais le Roi David lui répondit: Non; mais certainement j'achèterai [tout] cela au prix qu'il vaut; car je ne présenterai point à l'Eternel ce qui est à toi, et je n'offrirai point un holocauste d'une chose que j'aie eue pour rien.
Koma mfumu Davide inayankha Arauna kuti, “Ayi, ine ndikuti ndipereka mtengo wathunthu. Sindingatenge chinthu chako ndi kuchipereka kwa Yehova, kapena kupereka nsembe imene sindinayigule.”
25 David donna donc à Ornan pour cette place, six cents sicles d'or de poids.
Choncho Davide analipira Arauna masekeli agolide 600 chifukwa cha malowo.
26 Puis il bâtit là un autel à l'Eternel, et il offrit des holocaustes, et des sacrifices de prospérités, et il invoqua l'Eternel, qui l'exauça par le feu envoyé des cieux sur l'autel de l'holocauste.
Davide anamangira Yehova guwa lansembe pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Iye anapemphera kwa Yehova, ndipo Yehova anayankha potumiza moto pa guwa lansembe zopsereza kuchokera kumwamba.
27 Alors l'Eternel commanda à l'Ange; et l'Ange remit son épée dans son fourreau.
Tsono Yehova anayankhula kwa mngelo, ndipo analowetsa lupanga lake mʼchimake.
28 En ce temps-là David voyant que l'Eternel l'avait exaucé dans l'aire d'Ornan Jébusien, y sacrifia.
Pa nthawi imeneyo, Davide ataona kuti Yehova wamuyankha pa malo opunthira tirigu a Arauna Myebusi, anapereka nsembe pamenepo.
29 [Or] le pavillon de l'Eternel que Moïse avait fait au désert, et l'autel des holocaustes étaient en ce temps-là dans le haut lieu de Gabaon.
Tenti ya Yehova imene Mose anapanga mʼchipululu, ndi guwa lansembe zopsereza pa nthawi imeneyi zinali pa phiri ku Gibiyoni.
30 Mais David ne put point aller devant cet autel pour invoquer Dieu, parce qu'il avait été troublé à cause de l'épée de l'Ange de l'Eternel.
Koma Davide sanathe kupita kumeneko kuti akapemphere pamaso pa Yehova, chifukwa amaopa lupanga la mngelo wa Yehova.

< 1 Chroniques 21 >