< Deutéronome 5 >

1 Moïse donc appela tout Israël, et leur dit: Ecoute, Israël, les statuts et les droits que je te prononce aujourd'hui, vous les entendant, afin que vous les appreniez, et que vous les gardiez pour les faire.
Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati: Tamverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuwuzeni lero. Muwaphunzire ndi kuonetsetsa kuti mukuwatsata.
2 L'Eternel notre Dieu a traité alliance avec nous en Horeb.
Yehova Mulungu wathu anachita pangano ndi ife ku Horebu.
3 Dieu n'a point traité cette alliance avec nos pères, mais avec nous, qui sommes ici aujourd'hui tous vivants.
Yehova sanachite pangano ndi makolo athu koma ndi ife, tonse amene tili moyo lero.
4 L'Eternel vous parla face à face sur la montagne, du milieu du feu.
Yehova anayankhula nanu maso ndi maso kuchokera mʼmoto pa phiri paja.
5 Je me tenais en ce temps-là entre l'Eternel et vous, pour vous rapporter la parole de l'Eternel; parce que vous aviez peur de ce feu, vous ne montâtes point sur la montagne, [et le Seigneur] dit:
(Pa nthawi imeneyo ine ndinayimirira pakati pa Yehova ndi inu kuti ndikuwuzeni mawu a Yehova, chifukwa inu munkachita mantha ndi moto ndipo simunakwere ku phiri). Ndipo Iye anati:
6 Je suis l'Eternel ton Dieu, qui t'ai tiré du pays d'Egypte, de la maison de servitude.
“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.
7 Tu n'auras point d'autres dieux devant ma face.
“Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.
8 Tu ne te feras point d'image taillée, ni aucune ressemblance des choses qui sont là-haut aux cieux, ni ici bas sur la terre, ni dans les eaux qui sont sous la terre.
“Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko.
9 Tu ne te prosterneras point devant elles, et tu ne les serviras point; car je suis l'Eternel ton Dieu, le [Dieu] Fort qui est jaloux, [et ] qui punis l'iniquité des pères sur les enfants, jusqu'à la troisième et à la quatrième [génération] de ceux qui me haïssent.
Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane,
10 Et qui fais miséricorde jusqu'à mille [générations] à ceux qui m'aiment et qui gardent mes commandements.
koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda ndi kusunga malamulo anga.
11 Tu ne prendras point le Nom de l'Eternel ton Dieu en vain; car l'Eternel ne tiendra point pour innocent celui qui aura pris son Nom en vain.
“Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.
12 Garde le jour du repos pour le sanctifier, ainsi que l'Eternel ton Dieu te l'a commandé.
“Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika monga momwe Yehova Mulungu wako anakulamulira.
13 Tu travailleras six jours, et tu feras toute ton œuvre;
Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi,
14 Mais le septième jour [est] le repos de l'Eternel ton Dieu; tu ne feras aucune œuvre en ce jour-là, ni toi, ni ton fils, ni ta fille, ni ton serviteur, ni ta servante, ni ton bœuf, ni ton âne, ni aucune de tes bêtes, ni ton étranger qui [est] dans tes portes, afin que ton serviteur et ta servante se reposent comme toi.
koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi kapena wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu kapena ngʼombe yanu kapena bulu wanu kapena ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu, motero ndiye kuti wantchito wanu wamwamuna ndi wantchito wanu wamkazi adzapumula monga inuyo.
15 Et qu'il te souvienne que tu as été esclave au pays d'Egypte, et que l'Eternel ton Dieu t'en a retiré à main forte, et à bras étendu; c'est pourquoi l'Eternel ton Dieu t'a commandé de garder le jour du repos.
Kumbukira kuti unali kapolo ku Igupto ndipo Yehova Mulungu wako anakutulutsa kumeneko ndi dzanja lamphamvu ndi lotambasuka. Choncho Yehova Mulungu wako akukulamula kuti uzisunga tsiku la Sabata.
16 Honore ton père et ta mère, comme l'Eternel ton Dieu te l'a commandé, afin que tes jours soient prolongés, et afin que tu prospères sur la terre que l'Eternel ton Dieu te donne.
“Lemekeza abambo ako ndi amayi ako monga Yehova Mulungu wako wakulamulira iwe kuti ukhale ndi moyo wautali ndi kuti zikuyendere bwino mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.
17 Tu ne tueras point.
“Usaphe.
18 Et tu ne paillarderas point.
“Usachite chigololo.
19 Et tu ne déroberas point.
“Usabe.
20 Et tu ne diras point de faux témoignage contre ton prochain.
“Usapereke umboni womunamizira mnzako.
21 Tu ne convoiteras point la femme de ton prochain, tu ne souhaiteras point la maison de ton prochain, ni son champ, ni son serviteur, ni sa servante, ni son bœuf, ni son âne, ni aucune chose qui soit à ton prochain.
“Usasirire mkazi wa mnzako. Usasirire nyumba ya mnzako kapena munda wake, wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”
22 L'Eternel prononça ces paroles à toute votre assemblée sur la montagne, du milieu du feu, de la nuée et de l'obscurité, avec une voix forte, et il ne prononça rien davantage; puis il les écrivit dans deux Tables de pierre, qu'il me donna.
Awa ndi malamulo amene Yehova anayankhula ndi mawu okweza kwa gulu lanu lonse pa phiri paja mʼmoto, mtambo ndi mdima woopsa, sanawonjezerepo kanthu. Ndipo anawalemba pa mapale awiri amiyala ndi kundipatsa.
23 r il arriva qu'aussitôt que vous eûtes entendu cette voix du milieu de l'obscurité, parce que la montagne était toute en feu, vous vous approchâtes de moi, [savoir] tous les chefs de vos Tribus et vos anciens;
Mutamva mawu kuchokera mu mdimawo, phiri lili moto lawilawi, atsogoleri onse a mafuko anu ndi akuluakulu anu anabwera kwa ine.
24 Et vous dîtes: Voici, l'Eternel notre Dieu nous a fait voir sa gloire et sa grandeur, et nous avons entendu sa voix du milieu du feu; aujourd'hui nous avons vu que Dieu a parlé avec l'homme, et que l'homme est demeuré en vie.
Ndipo munati, “Yehova Mulungu wathu wationetsa ulemerero ndi ukulu wake, ndipo tamva mawu ake kuchokera mʼmoto. Lero taona kuti munthu akhoza kukhala ndi moyo ngakhale Mulungu atayankhula naye.
25 Et maintenant pourquoi mourrions-nous? Car ce grand feu-là nous consumera; si nous entendons encore une fois la voix de l'Eternel notre Dieu, nous mourrons.
Koma tsopano tife chifukwa chiyani? Moto waukuluwu utinyeketsa, ndipo tifa tikapitirirabe kumva mawu a Yehova Mulungu wathu.
26 Car qui est l'homme, quel qu'il soit, qui ait entendu, comme nous, la voix du Dieu vivant, parlant du milieu du feu, et qui soit demeuré en vie?
Pakuti ndi munthu uti wolengedwa amene anamvapo mawu a Mulungu wamoyo akuyankhula kuchokera mʼmoto, monga tachitiramu, nakhala ndi moyo?
27 Approche-toi, et écoute tout ce que l'Eternel notre Dieu dira; puis tu nous rediras tout ce que l'Eternel notre Dieu t'aura dit, nous l'entendrons, et nous le ferons.
Pita pafupi kuti ukamvetsere zonse zimene Yehova Mulungu wathu akunena. Kenaka udzatiwuze chilichonse chimene Yehova Mulungu wathu akunena ndipo tidzamvera ndi kuchita.”
28 Et l'Eternel ouït la voix de vos paroles pendant que vous me parliez, et l'Eternel me dit: J'ai ouï la voix des discours de ce peuple, lesquels ils t'ont tenu; tout ce qu ils ont dit, ils l'ont bien dit.
Yehova anakumvani pamene munkayankhula kwa ine ndipo Yehova anati kwa ine, “Ndamva zimene anthuwa anena kwa iwe. Chilichonse chimene anena ndi chabwino.
29 Ô! s'ils avaient toujours ce même cœur pour me craindre, et pour garder tous mes commandements, afin qu'ils prospérassent, eux et leurs enfants à jamais.
Zikanakhala bwino akanakhala ndi mtima wondiopa ndi kusunga malamulo anga nthawi zonse kuti zinthu ziziwayendera bwino, iwowo pamodzi ndi ana awo kwamuyaya.
30 Va, dis-leur: Retournez-vous-en dans vos tentes.
“Pita uwawuze kuti abwerere ku matenti awo.
31 Mais toi, demeure ici avec moi, et je te dirai tous les commandements, les statuts, et les droits que tu leur enseigneras, afin qu'ils les fassent au pays que je leur donne pour le posséder.
Koma iwe ukhale kuno ndi ine kuti ndikupatse malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene azitsatira mʼdziko limene ndiwapatse kuti alitenge.”
32 Vous prendrez donc garde de les faire; comme l'Eternel votre Dieu vous l'a commandé; vous ne vous en détournerez ni à droite ni à gauche.
Choncho samalirani kuchita zimene Yehova Mulungu wanu akukulamulirani inu, musapatukire kudzanja lamanja kapena lamanzere.
33 Vous marcherez dans toute la voie que l'Eternel votre Dieu vous a prescrite, afin que vous viviez, et que vous prospériez, et que vous prolongiez vos jours au pays que vous posséderez.
Muyende mʼnjira yonse imene Yehova Mulungu wanu wakulamulirani kuti mukhale ndi moyo ndi kupambana, ndi kuti masiku anu achuluke mʼdziko limene mudzatengelo.

< Deutéronome 5 >