< Ecclésiaste 8 >

1 Qui est tel que le sage? et qui sait ce que veulent dire les choses? La sagesse de l'homme fait reluire son visage, et son regard farouche en est changé.
Ndani angafanane ndi munthu wanzeru? Ndani angadziwe kutanthauzira zinthu? Nzeru imabweretsa chimwemwe pa nkhope ya munthu ndipo imasintha maonekedwe ake awukali.
2 Prends garde (je te le dis) à la bouche du Roi, et à la parole du jurement de Dieu.
Ine ndikuti, mvera lamulo la mfumu, chifukwa unalumbira pamaso pa Mulungu.
3 Ne te précipite point de te retirer de devant sa face; et ne persévère point en une chose mauvaise; car il fera tout ce qu'il lui plaira.
Usafulumire kuchoka pamaso pa mfumu. Usawumirire chinthu choyipa, pakuti mfumu idzachita chilichonse chomwe imasangalatsidwa nacho.
4 En quelque lieu qu'est la parole du Roi, là est la puissance; et qui lui dira: Que fais-tu?
Popeza mawu a mfumu ali ndi mphamvu, ndani anganene kwa mfumuyo kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
5 Celui qui garde le commandement, ne sentira aucun mal; et le cœur du sage discerne le temps, et ce qui est juste.
Aliyense amene amamvera lamulo lake sadzapeza vuto lililonse, ndipo munthu wanzeru amadziwa nthawi yoyenera ndi machitidwe ake.
6 Car dans toute affaire il y a un temps à considérer la justice de la chose, autrement mal sur mal tombe sur l'homme.
Pakuti pali nthawi yoyenera ndiponso machitidwe a chinthu chilichonse, ngakhale kuti mavuto ake a munthu amupsinja kwambiri.
7 Car il ne sait pas ce qui arrivera; et même qui est-ce qui lui déclarera quand ce sera?
Popeza palibe munthu amene amadziwa zamʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika mʼtsogolo?
8 L'homme n'est point le maître de son esprit pour le pouvoir retenir; il n'a point de puissance sur le jour de la mort; et il n'y a point de délivrance en une telle guerre; et la méchanceté ne délivrera point son maître.
Palibe munthu amene ali ndi mphamvu yolamulira mpweya wa moyo kuti athe kuwusunga, choncho palibe amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa yake. Nkhondo sithawika; tsono anthu ochita zoyipa, kuyipa kwawoko sikudzawapulumutsa.
9 J'ai vu tout cela, et j'ai appliqué mon cœur à toute œuvre qui s'est faite sous le soleil. Il y a un temps auquel un homme domine sur l'autre, à son malheur.
Zonsezi ndinaziona pamene ndinalingalira mu mtima mwanga, zonse zimene zimachitika pansi pano. Ilipo nthawi imene ena amalamulira anzawo mwankhanza.
10 Et alors j'ai vu les méchants ensevelis, et puis retournés; et ceux qui étaient venus du lieu du Saint, [et] qui avaient bien fait, être mis en oubli dans la ville. Cela aussi est une vanité.
Kenaka, ndinaona anthu oyipa akuyikidwa mʼmanda, iwo amene ankalowa ndi kumatuluka mʼmalo opatulika ndipo ankatamandidwa mu mzindawo pamene ankachita zimenezi. Izinso ndi zopandapake.
11 Parce que la sentence contre les mauvaises œuvres ne s'exécute point incontinent, à cause de cela le cœur des hommes est plein au-dedans d'eux-mêmes [d'envie] de mal faire.
Pamene chigamulo cha anthu opalamula mlandu chikuchedwa, mitima ya anthu imadzaza ndi malingaliro ochita zolakwa.
12 Car le pécheur fait mal cent fois, et [Dieu] lui donne du délai; mais je connais aussi qu'il sera bien à ceux qui craignent Dieu, et qui révèrent sa face:
Ngakhale munthu woyipa apalamule milandu yambirimbiri, nʼkumakhalabe ndi moyo wautali, ine ndikudziwa kuti anthu owopa Mulungu zinthu zidzawayendera bwino, omwe amapereka ulemu pamaso pa Mulungu.
13 Mais qu'il ne sera pas bien au méchant, et qu'il ne prolongera point ses jours, non plus que l'ombre, parce qu'il ne révère point la face de Dieu.
Koma popeza oyipa saopa Mulungu zinthu sizidzawayendera bwino, ndipo moyo wawo sudzakhalitsa monga mthunzi.
14 Il y a une vanité qui arrive sur la terre, c'est qu'il y a des justes, à qui il arrive selon l'œuvre des méchants; et il y a aussi des méchants, à qui il arrive selon l'œuvre des justes; j'ai dit que cela aussi est une vanité.
Palinso chinthu china chopanda phindu chomwe chimachitika pa dziko lapansi: anthu olungama amalangidwa ngati anthu osalungama. Pamene oyipa amalandira zabwino ngati kuti ndi anthu abwino.
15 C'est pourquoi j'ai prisé la joie, parce qu'il n'y a rien sous le soleil de meilleur à l'homme, que de manger et de boire, et de se réjouir; c'est aussi ce qui lui demeurera de son travail durant les jours de sa vie, que Dieu lui donne sous le soleil.
Nʼchifukwa chake ndikuti munthu azikondwerera moyo, pakuti munthu alibe chinanso chabwino pansi pano choposa kudya, kumwa ndi kumadzikondweretsa. Akamatero, munthuyo adzakhala ndi chimwemwe pa ntchito yake masiku onse a moyo wake amene Mulungu wamupatsa pansi pano.
16 Après avoir appliqué mon cœur à connaître la sagesse, et à regarder les occupations qu'il y a sur la terre, (car même ni jour, ni nuit, [l'homme] ne donne point de repos à ses yeux.)
Pamene ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe nzeru ndi kuonetsetsa ntchito za munthu pa dziko lapansi, osapeza tulo usana ndi usiku,
17 Après avoir, [dis-je], vu toute l'œuvre de Dieu, [et] que l'homme ne peut trouver l'œuvre qui se fait sous le soleil, pour laquelle l'homme se travaille en la cherchant, et il ne la trouve point, et même si le sage se propose de la savoir, il ne la peut trouver.
pamenepo ndinaona zonse zimene Mulungu anazichita. Palibe munthu amene angathe kuzimvetsa zonse zimene zimachitika pansi pano. Ngakhale munthu ayesetse kuzifufuza, sangathe kupeza tanthauzo lake. Ngakhale munthu wanzeru atanena kuti iye amadziwa, sangathe kuzimvetsetsa zinthuzo.

< Ecclésiaste 8 >