< Ézéchiel 44 >

1 Puis il me ramena au chemin de la porte extérieure du Sanctuaire, laquelle regardait l'Orient, et elle était fermée.
Munthu uja anabwerera nane ku chipata chakunja kwa malo opatulika, chomwe chimayangʼana kummawa. Chipatacho chinali chotseka.
2 Et l'Eternel me dit: cette porte-ci sera fermée, [et] ne sera point ouverte, et personne n'y passera, parce que l'Eternel le Dieu d'Israël est entré par cette porte; elle sera donc fermée.
Yehova anandiwuza kuti, “Chipata ichi chikhale chotseka, chisatsekulidwe. Wina asalowerepo chifukwa Yehova, Mulungu wa Israeli walowera pomwepa.
3 [Elle sera] pour le Prince: le Prince sera le seul qui s'y assiéra pour manger devant l'Eternel; il entrera par le chemin de l'allée de cette porte-là, et sortira par le même chemin.
Kalonga yekha angathe kukhala mʼmenemo ndi kumadya chakudya pamaso pa Yehova. Iye adzalowere pa njira ya ku khonde lamʼkati ndi kutulukiranso njira yomweyo.”
4 Et il me fit revenir par le chemin de la porte du Septentrion jusque sur le devant de la maison, et je regardai, et voici, la gloire de l'Eternel avait rempli la maison de l'Eternel, et je me prosternai sur ma face.
Kenaka munthuyo anandidzeretsa pa chipata chakumpoto ndipo tinafika kumaso kwa Nyumba ya Mulungu. Nditapenyetsetsa ndinangoona ulemerero wa Yehova utadzaza mʼNyumba ya Mulungu, ndipo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba.
5 Alors l'Eternel me dit: fils d'homme, applique ton cœur, et regarde de tes yeux, et écoute de tes oreilles tout ce dont je te vais parler, touchant toutes les ordonnances et toutes les lois qui concernent la maison de l'Eternel: applique ton cœur à ce qui concerne l'entrée de la maison par toutes les sorties du Sanctuaire.
Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, samala bwino ndipo uyangʼanitsitse ndi kumvetsa bwino zonse zimene ndikuwuze zokhudza malamulo ndi malangizo a Nyumbayi. Usamalitse za amene angalowe ndi kutuluka mʼNyumbayi.
6 Tu diras donc à [ceux qui sont extrêmement] rebelles, [savoir] à la maison d'Israël: ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: maison d'Israël! Qu'il vous suffise qu'entre toutes vos abominations,
Uwuze mtundu wopanduka wa Israeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu Aisraeli, andikwana machitidwe anu onyansawo!
7 Vous ayez fait entrer les enfants de l'étranger, qui étaient incirconcis de cœur, et incirconcis de chair, pour être dans mon Sanctuaire, afin de profaner ma maison, quand vous avez offert ma viande, [savoir] la graisse et le sang, et ils ont enfreint mon alliance, outre toutes vos [autres] abominations.
Munalowetsa alendo osachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi momwe mʼNyumba yanga ndipotu anayipitsa Nyumba yanga. Pamene inu munkandipatsa chakudya changa ndi magazi omwe kuwonjezera pa zonyansa zanu zonse ndiye kuti munaphwanya pangano langa.
8 Et vous n'avez point donné ordre que mes choses saintes fussent observées, mais vous avez établi comme il vous a plu dans mon Sanctuaire, des gens pour y être les gardes des choses que j'avais commandé de garder.
Mʼmalo moti muzisamalira zinthu zanga zopatulika, mwayika alendo kuti aziyangʼanira malo anga opatulika.
9 Ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: pas un de tous ceux qui seront enfants d'étranger, incirconcis de cœur, et incirconcis de chair, n'entrera dans mon Sanctuaire, même pas un d'entre tous les enfants d'étranger, qui seront parmi les enfants d'Israël.
Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Palibe mlendo wosachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi ngakhalenso mlendo amene amakhala pakati pa Aisraeli amene adzalowe mʼmalo anga opatulika.
10 Mais les Lévites qui se sont éloignés de moi, lorsque Israël s'est égaré, et qui se sont égarés de moi pour suivre leurs idoles, porteront [la peine de] leur iniquité.
“Ndiponso Alevi amene anandisiya kutali pa nthawi imene Israeli anasochera potsata mafano, adzalangidwa chifukwa cha tchimo lawo.
11 Toutefois ils seront employés dans mon Sanctuaire aux charges qui sont vers les portes de la maison, et ils feront le service de la maison; ils égorgeront pour le peuple [les bêtes pour] l'holocauste, et [pour] les [autres] sacrifices, [et] se tiendront [prêts] devant lui pour le servir.
Adzangokhala atumiki chabe mʼmalo anga opatulika. Azidzayangʼanira zipata za Nyumba ya Mulungu ndi kugwira ntchito kumeneko. Azidzapha nyama za nsembe zopsereza ndi za nsembe zina za anthu. Choncho azidzayimirira pamaso pa anthu nʼkumawatumikira.
12 Parce qu'ils les ont servis [se présentant] devant leurs idoles, et qu'ils ont été une occasion de chute dans le crime à la maison d'Israël, à cause de cela j'ai levé ma main [en jurant] contre eux, dit le Seigneur l'Eternel, qu'ils porteront [la peine de] leur iniquité.
Iwowa ankatumikira anthu popembedza mafano awo, ndipo anachititsa Aisraeli kugwa mu uchimo. Nʼchifukwa chake Ine ndikulumbira kuti iwowa ayenera kulangidwa chifukwa cha machimo awo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
13 Tellement qu'ils n'approcheront plus de moi pour m'exercer la sacrificature, ni pour approcher d'aucune de mes choses saintes aux lieux les plus saints, mais ils porteront leur confusion et leurs abominations, lesquelles ils ont commises.
Iwo sayenera kufika pafupi ndi Ine ndi kunditumikira ngati ansembe, kapena kuyandikira chilichonse cha zinthu zanga zopatulika, kapenanso zopereka zanga zopatulika kwambiri. Iwo adzachititsidwa manyazi chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
14 C'est pourquoi je les établirai pour avoir la garde de la maison pour tout son service, et pour tout ce qui s'y fait.
Komabe ndidzawayika kuti aziyangʼanira Nyumba yanga ndi kutumikira pa ntchito zake zonse zoyenera kuti zigwiridwe mʼmenemo.
15 Mais quant aux Sacrificateurs Lévites, enfants de Tsadok, qui ont soigneusement administré ce qu'il fallait faire dans mon Sanctuaire, lorsque les enfants d'Israël se sont éloignés de moi, ceux-là s'approcheront de moi pour faire mon service, et se tiendront devant moi pour m'offrir la graisse et le sang, dit le Seigneur l'Eternel.
“Koma ansembe, a fuko la Levi, a banja la Zadoki amene ankatumikira mokhulupirika ku malo anga opatulika pa nthawi imene Aisraeli anasochera ndi kundisiya Ine; iwowa adzasendera kwa Ine kudzanditumikira. Adzafika pamaso panga kuti apereke nsembe za mafuta ndi magazi. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
16 Ceux-là entreront dans mon Sanctuaire, et ceux-là s'approcheront de ma table, pour faire mon service, et ils administreront soigneusement ce que j'ai ordonné de faire.
Okhawa ndiwo adzalowe ku malo anga opatulika ndi kudzayandikira tebulo langa kuti adzanditumikire. Amenewa okha ndiwo adzasamalire zinthu zanga.
17 Et il arrivera que quand ils entreront aux portes des parvis intérieurs, ils se vêtiront de robes de lin; et il n'y aura point de laine sur eux pendant qu'ils feront le service aux portes des parvis intérieurs et dans le Temple.
“Pamene alowa ku zipata za bwalo lamʼkati azivala zovala zabafuta. Asamavale chovala china chilichonse cha ubweya wankhosa pamene akutumikira pa zipata za bwalo la mʼkati kapena kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
18 Ils auront des ornements de lin sur leur tête, et des caleçons de lin sur leurs reins, [et] ne se ceindront point à l'endroit où l'on sue.
Azivala nduwira za bafuta ndi kabudula wabafuta mʼkati. Asavale chilichonse chowachititsa thukuta.
19 Mais quand ils sortiront au parvis extérieur, au parvis, [dis-je], extérieur, vers le peuple, ils se dévêtiront de leurs habits, avec lesquels ils font le service, et les poseront dans les chambres saintes, et se revêtiront d'autres habits, afin qu'ils ne sanctifient point le peuple avec leurs habits.
Pamene atuluka ndi kupita ku bwalo lakunja kumene kuli anthu, azivula zovala zimene amatumikira nazo, ndipo azisiye zovalazo mu zipinda zopatulika. Pambuyo pake avale zovala zina, kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu enawo ndi zovala zawozo.
20 Ils ne se raseront point la tête, ni ne laisseront point croître leurs cheveux, mais simplement ils tondront leurs têtes.
“‘Ansembe asamamete mpala kapena kusunga tsitsi lalitali kwambiri, koma azingoliyepula.
21 Pas un des Sacrificateurs ne boira du vin, quand ils entreront au parvis intérieur.
Wansembe asamwe vinyo pamene ali pafupi kulowa mʼbwalo la mʼkati.
22 Ils ne prendront point pour femme une veuve, ni une répudiée; mais ils prendront des vierges, de la race de la maison d'Israël, ou une veuve qui soit veuve d'un Sacrificateur.
Iwo asakwatire akazi amasiye kapena osudzulidwa; koma azikwatira anamwali osadziwa mwamuna a fuko la Israeli kapena akazi amasiye a ansembe anzawo.
23 Et ils enseigneront à mon peuple la différence qu'il y a entre la chose sainte et la chose profane, et leur feront entendre la différence qu'il y a entre ce qui est souillé et ce qui est net.
Ansembe aziphunzitsa anthu anga kusiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, ndiponso pakati pa zinthu zoyenera ndi zosayenera kuperekedwa nsembe.
24 Et quand il surviendra quelque procès, ils assisteront au jugement, et jugeront suivant les lois que j'ai données; et ils garderont mes lois et mes statuts dans toutes mes solennités, et ils sanctifieront mes Sabbats.
“‘Pakakhala milandu, ansembe azikhala oweruza ndipo agamule milanduyo potsata malamulo anga. Atsate malamulo anga ndi malangizo anga pa za masiku anga onse a chikondwerero. Asamalirenso kuti masiku anga a Sabata akhale oyera.
25 [Pas un des Sacrificateurs] n'entrera vers le corps mort d'aucun homme, de peur d'en être souillé, si ce n'est que ce soit pour leur père, pour leur mère, pour leur fils, pour leur fille, pour leur frère, et pour leur sœur qui n'aura point eu de mari.
“‘Wansembe asadziyipitse pokhudza munthu wakufa, pokhapokha ngati wakufayo ndi abambo ake kapena amayi ake, mwana wake wamwamuna kapena wamkazi, mʼbale wake kapena mlongo wake wosakwatiwa.
26 Et après que chacun d'eux se sera purifié, on lui comptera sept jours;
Atatha kuyeretsedwa adikirebe masiku asanu ndi awiri kuti ayere ndithu.
27 Et le jour qu'il entrera aux lieux saints, [savoir] au parvis intérieur pour faire le service aux lieux saints, il offrira un [sacrifice pour] son péché, dit le Seigneur l'Eternel.
Pa tsiku lomwe akukalowa mʼbwalo la mʼkati la malo opatulika kuti akatumikire, apereke nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
28 Et cela leur sera pour héritage. Ce sera moi qui serai leur héritage, car vous ne leur donnerez aucune possession en Israël, et ce sera moi qui serai leur possession.
“‘Ansembe asadzakhale ndi cholowa chilichonse ayi. Cholowa chawo ndi Ine. Musadzawapatse chuma mu Israeli; Ine ndidzakhala chuma chawo.
29 Ils mangeront donc les gâteaux et [ce qui s'offrira pour] le péché, et [ce qui s'offrira pour] le délit; et tout interdit en Israël leur appartiendra.
Iwo azidzadya nsembe ya chakudya, nsembe yopereka chifukwa cha tchimo ndi nsembe yopepesera machimo. Zinthu zonse zoperekedwa kwa Yehova mu Israeli zidzakhala zawo.
30 Et les prémices de tout ce qui est produit le premier en toutes choses, et de tout ce qui sera présenté en offrande élevée de toutes choses, d'entre toutes vos offrandes élevées, appartiendront aux Sacrificateurs; vous donnerez aussi les prémices de vos pâtes aux Sacrificateurs, afin qu'ils fassent reposer la bénédiction sur la maison de chacun de vous.
Zabwino za zipatso zanu zoyambirira kucha ndiponso mphatso zanu zonse zapadera zidzakhala za ansembe. Inu muziwapatsa chigawo choyamba cha ufa wanu kuti pa nyumba panu pakhale madalitso.
31 Les Sacrificateurs ne mangeront point de chair d'aucune bête morte d'elle-même, ni rien de déchiré, soit oiseau, soit bête à quatre pieds.
Ansembe sayenera kudya kalikonse kofa kokha, kaya mbalame, kapena nyama. Kapena yochita kujiwa.’”

< Ézéchiel 44 >