< Esdras 3 >

1 Or le septième mois approchant, et les enfants d'Israël étant dans leurs villes, le peuple s'assembla à Jérusalem comme si ce n'eût été qu'un seul homme.
Utafika mwezi wa chisanu ndi chiwiri Aisraeli atakhala kale mʼmidzi yawo, anthu anasonkhana ku Yerusalemu ndi cholinga chimodzi.
2 Alors Jésuah, fils de Jotsadak, se leva avec ses frères les Sacrificateurs, et Zorobabel fils de Salathiel, avec ses frères, et ils bâtirent l'autel du Dieu d'Israël, pour y offrir les holocaustes, ainsi qu'il est écrit dans la Loi de Moïse, homme de Dieu.
Kenaka Yesuwa mwana wa Yozadaki ndi ansembe anzake pamodzi ndi Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi abale ake anayamba kumanga guwa lansembe la Mulungu wa Israeli. Anatero pofuna kuti aziperekapo nsembe zopsereza monga analembera mʼbuku la Mose, munthu wa Mulungu uja.
3 Et ils posèrent l'autel de Dieu sur sa base, parce qu'ils avaient peur en eux-mêmes des peuples du pays, et ils y offrirent des holocaustes à l'Eternel, les holocaustes du matin et du soir.
Ndi mantha ndi mantha chifukwa cha anthu a mʼmayikomo, iwo anamanga guwalo pa maziko ake akale, ndipo anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu pa guwapo mmawa ndi madzulo.
4 Ils célébrèrent aussi la fête solennelle des Tabernacles, en la manière qu'il est écrit [dans la Loi]; et ils [offrirent] les holocaustes chaque jour, autant qu'il en fallait, selon que portait l'ordinaire de chaque jour;
Ankasunga tsiku la chikondwerero cha misasa monga momwe zinalembedwera. Ankaperekanso nsembe za tsiku ndi tsiku monga mwa chiwerengero chake potsata mwambo wake wa tsiku ndi tsiku monga zinalembedwa.
5 Après cela, l'holocauste continuel, et ceux des nouvelles lunes, et de toutes les fêtes solennelles de l'Eternel, lesquelles on sanctifiait, et de tous ceux qui présentaient une offrande volontaire à l'Eternel.
Pambuyo pake, ankapereka nsembe zopsereza, nsembe zopereka pa nthawi ya mwezi watsopano ndi za pa masiku onse a chikondwerero oyikidwa kutamandira Yehova, kudzanso nsembe zaufulu zopereka kwa Yehova.
6 Dès le premier jour du septième mois ils commencèrent à offrir des holocaustes à l'Eternel; bien que le Temple de l'Eternel ne fût pas encore fondé.
Kuyambira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, iwo anayambanso kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova, ngakhale kuti maziko a Nyumba ya Yehova anali asanamangidwe.
7 Mais ils donnèrent de l'argent aux tailleurs de pierres et aux charpentiers, [ils donnèrent] aussi à manger et à boire, et de l'huile, aux Sidoniens et aux Tyriens, afin qu'ils amenassent du bois de cèdre du Liban à la mer de Japho, selon la permission que Cyrus, Roi de Perse, leur en avait donnée.
Ndipo anapereka ndalama kwa amisiri a miyala ndi kwa amisiri a matabwa, ndi chakudya, chakumwa ndi mafuta kwa anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo, kuti abweretse mitengo ya mkungudza pa nyanja kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Yopa. Zonsezi anachita malinga ndi chilolezo chimene analandira kuchokera kwa Koresi, mfumu ya Peresiya.
8 Et la seconde année de leur arrivée en la maison de Dieu à Jérusalem, au second mois, Zorobabel, fils de Salathiel, et Jésuah, fils de Jotsadak, et le reste de leurs frères, les Sacrificateurs, et les Lévites, et tous ceux qui étaient venus de la captivité à Jérusalem, commencèrent [à fonder le Temple]; et ils établirent des Lévites, depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, pour presser l'ouvrage de la maison de l'Eternel.
Tsono mu chaka chachiwiri atabwera ku Yerusalemu, ku malo akale a Nyumba ya Yehova, mwezi wachiwiri Zerubabeli mwana wa Sealatieli, Yesuwa mwana wa Yozadaki pamodzi ndi abale awo onse, ansembe, Alevi ndi onse amene anabwera ku Yerusalemu kuchokera ku ukapolo, anayamba kugwira ntchito. Iwo anasankha Alevi a zaka zoyambira makumi awiri kuti aziyangʼanira ntchito ya kumanga Nyumba ya Yehova.
9 Et Jésuah assistait avec ses fils et ses frères, et Kadmiel avec ses fils, enfants de Juda, pour presser ceux qui faisaient l'ouvrage en la maison de Dieu; [et] les fils de Hémadad, avec leurs fils et leurs frères, Lévites.
Yesuwa ndi ana ake aamuna kudzanso abale ake, Kadimieli ndi ana ake (ana a Yuda) onse pamodzi anasenza udindo woyangʼanira antchito ku Nyumba ya Mulungu, kuphatikizanso ana a Henadadi komanso Alevi, ana awo ndi abale awo.
10 Et lorsque ceux qui bâtissaient fondaient le Temple de l'Eternel, on y fit assister les Sacrificateurs revêtus, ayant leurs trompettes; et les Lévites, enfants d'Asaph, avec les cymbales, pour louer l'Eternel, selon l'institution de David, Roi d'Israël.
Amisiri omanga nyumba atamanga maziko a Nyumba ya Yehova, ansembe anabwera akuyimba malipenga, atavala zovala zaunsembe. Ndipo Alevi, zidzukulu za Asafu, anadza akuyimba matambolini ndi kutenga udindo wawo wotamanda Yehova, potsata malangizo a Davide mfumu ya Aisraeli.
11 Et ils s'entre-répondaient en louant et célébrant l'Eternel, [chantant]: Qu'il est bon, parce que sa gratuité demeure à toujours sur Israël. Et tout le peuple jeta de grands cris de joie en louant l'Eternel, parce qu'on fondait la maison de l'Eternel.
Iwo ankayimba motamanda ndi mothokoza Yehova nyimbo iyi: “Yehova ndi wabwino; chikondi chake pa Israeli ndi chamuyaya.” Ndipo anthu onse ankafuwula kwambiri kumutamanda Yehova, chifukwa maziko a Nyumba ya Yehova anali kumangidwa.
12 Mais plusieurs des Sacrificateurs et des Lévites, et des Chefs des pères qui étaient âgés, [et] qui avaient vu la première maison sur son fondement, se représentant cette maison-là, pleuraient à haute voix; mais plusieurs élevaient leur voix avec des cris de réjouissance, et d'allégresse.
Koma ambiri mwa ansembe, Alevi ndiponso atsogoleri amabanja, akuluakulu amene anaona Nyumba ya Yehova yakale, analira mokweza pamene anaona maziko a nyumbayi akumangidwa. Komanso ena ambiri ankafuwula mosangalala.
13 Et le peuple ne pouvait discerner la voix des cris de joie, et d'allégresse, d'avec la voix des pleurs du peuple; cependant le peuple jetait de grands cris de joie, en sorte que la voix fut entendue bien loin.
Choncho panalibe amene ankatha kusiyanitsa liwu lofuwula mokondwerera ndi liwu la anthu olira, chifukwa anthuwo ankafuwula kwambiri. Ndipo liwu lofuwulalo limamveka kutali.

< Esdras 3 >