< Isaïe 12 >

1 Et tu diras en ce jour-là; Eternel! je te célébrerai, parce qu'ayant été courroucé contre moi, ta colère s'est apaisée, et tu m'as consolé.
Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati: “Ndikukuyamikani, Inu Yehova; chifukwa ngakhale munandipsera mtima, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mwanditonthoza.
2 Voici, le [Dieu] Fort est ma délivrance, j'aurai confiance, et je ne serai point effrayé; car l'Eternel, l'Eternel [est] ma force et ma louange, et il a été mon Sauveur.
Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga; ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.”
3 Et vous puiserez des fontaines de cette délivrance des eaux avec joie.
Mudzakondwera popeza Yehova ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
4 Et vous direz en ce jour-là; Célébrez l'Eternel, réclamez son Nom, faites connaître parmi les peuples ses exploits, faites souvenir que son Nom est une haute retraite.
Tsiku limenelo mudzati: “Yamikani Yehova, tamandani dzina lake; mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
5 Psalmodiez à l'Eternel, car il a fait des choses magnifiques; cela est connu dans toute la terre.
Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu; zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
6 Habitante de Sion, égaye-toi, et te réjouis avec chant de triomphe; car le Saint d'Israël est grand au milieu de toi.
Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni; pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”

< Isaïe 12 >