< Joël 2 >

1 Sonnez du cor en Sion, et sonnez avec un retentissement bruyant en la montagne de ma sainteté; que tous les habitants du pays tremblent; car la journée de l'Eternel vient; car elle est proche.
Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
2 Journée de ténèbres et d'obscurité; journée de nuées et de brouillards. Comme l'aube du jour s'étend sur les montagnes, [ainsi s'étend] un peuple grand et puissant, auquel il n'[y a] point eu de semblable de tout temps, et après lequel il n'y en aura point [de semblable] dans la suite des siècles.
tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
3 Le feu dévore devant sa face, et derrière lui la flamme brûle; le pays était avant sa venue comme le jardin d'Héden; et après qu'il sera parti [il sera comme] un désert de désolation; et même il n'y aura rien qui lui échappe.
Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
4 C'est, à le voir, comme si on voyait des chevaux, et ils courront comme des gens de cheval;
Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
5 Et ils sauteront menant un bruit semblable à celui des chariots sur les sommets des montagnes, et au bruit d'une flamme de feu, qui dévore du chaume; et ils seront comme un peuple puissant rangé en bataille.
Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
6 Les peuples trembleront en le voyant; tous les visages en deviendront pâles et livides.
Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
7 Ils courront comme des gens vaillants, et monteront sur la muraille comme des gens de guerre; ils marcheront chacun en son rang, et ne se détourneront point de leurs chemins.
Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
8 L'un ne pressera point l'autre, mais chacun marchera dans son chemin, ils se jetteront au travers des épées, et ne seront point blessés.
Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
9 Ils iront çà et là par la ville, ils courront sur la muraille, ils monteront sur les maisons, ils entreront par les fenêtres comme le larron.
Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
10 La terre tremblera devant lui, les cieux seront ébranlés, le soleil et la lune seront obscurcis, et les étoiles retireront leur lueur.
Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
11 Aussi l'Eternel fera entendre sa voix devant son armée, parce que son camp sera très-grand; car l'exécuteur de sa parole [sera] puissant; certainement la journée de l'Eternel est grande et terrible; et qui la pourra soutenir?
Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
12 Maintenant donc aussi, dit l'Eternel, retournez-vous jusqu'à moi de tout votre cœur, avec jeûne, avec larmes, et lamentation.
“Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
13 Et déchirez vos cœurs, et non pas vos vêtements, et retournez à l'Eternel votre Dieu; car il est miséricordieux et pitoyable, tardif à colère, et abondant en miséricorde, et qui se repent d'avoir affligé.
Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
14 Qui sait si l'Eternel votre Dieu ne viendra point à se repentir, et s'il ne laissera point après soi bénédiction, gâteau, et aspersion?
Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
15 Sonnez du cor en Sion, sanctifiez le jeûne, publiez l'assemblée solennelle.
Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
16 Assemblez le peuple, sanctifiez la congrégation, amassez les anciens, assemblez les enfants, et ceux qui sucent les mamelles; que le nouveau marié sorte de son cabinet, et la nouvelle mariée de sa chambre nuptiale.
Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
17 Que les Sacrificateurs qui font le service de l'Eternel pleurent entre le porche et l'autel, et qu'ils disent: Eternel, pardonne à ton peuple, et n'expose point ton héritage à l'opprobre, tellement que les nations en fassent le sujet de leurs railleries. Pourquoi dirait-on entre les peuples: Où est leur Dieu?
Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
18 Or l'Eternel a été jaloux de sa terre, et il a été ému de compassion envers son peuple.
Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
19 Et l'Eternel a répondu et a dit à son peuple: Voici, je vous enverrai du froment, du bon vin, et de l'huile, et vous en serez rassasiés, et je ne vous exposerai plus à l'opprobre entre les nations.
Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
20 J'éloignerai de vous [l'armée venue] du Septentrion, et je la pousserai en un pays sec et désolé; la partie antérieure vers la mer Orientale; et celle de derrière, vers la mer Occidentale; sa puanteur montera, et son infection s'élèvera, après avoir fait de grandes choses.
“Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
21 Ne crains point, terre; égaye-toi et te réjouis; car l'Eternel a fait de grandes choses.
Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
22 Ne craignez point, bêtes des champs, car les pâturages du désert ont poussé leur jet, et même les arbres ont pousse leur fruit; le figuier et la vigne ont poussé avec vigueur.
Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
23 Et vous enfants de Sion égayez-vous, et vous réjouissez en l'Eternel votre Dieu; car il vous a donné la pluie selon la justice, et même il a fait couler sur vous la pluie [de la première saison], et celle de la dernière, au premier mois.
Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
24 Et les aires seront remplies de froment, et les cuves regorgeront de moût et d'huile.
Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
25 Ainsi je vous rendrai les [fruits des années] que la sauterelle, le hurebec, le vermisseau, et le hanneton, ma grande armée, que j'avais envoyée contre vous, avait broutés.
“Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
26 Vous aurez donc abondamment de quoi manger et être rassasiés; et vous louerez le nom de l'Eternel votre Dieu, qui vous aura fait des choses merveilleuses; et mon peuple ne sera point confus à toujours.
Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
27 Et vous saurez que je suis au milieu d'Israël, et que je suis l'Eternel votre Dieu, et qu'il n'y en a point d'autre; et mon peuple ne sera point confus à toujours.
Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
28 Et il arrivera après ces choses que je répandrai mon Esprit sur toute chair; et vos fils et vos filles prophétiseront; vos vieillards songeront des songes, et vos jeunes gens verront des visions.
“Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
29 Et même en ces jours-là je répandrai mon Esprit sur les serviteurs et sur les servantes.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
30 Et je ferai des prodiges dans les cieux et sur la terre, du sang et du feu, et des colonnes de fumée.
Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
31 Le soleil sera changé en ténèbres et la lune en sang, avant que le jour grand et terrible de l'Eternel vienne.
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
32 Et il arrivera que quiconque invoquera le Nom de l'Eternel sera sauvé; car le salut sera en la montagne de Sion, et dans Jérusalem, comme l'Eternel a dit, et dans les résidus que l'Eternel aura appelés.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.

< Joël 2 >