< Nombres 3 >

1 Or ce sont ici les générations d'Aaron et de Moïse, au temps que l'Eternel parla à Moïse sur la montagne de Sinaï.
Iyi ndi mbiri ya banja la Aaroni ndi Mose pa nthawi yomwe Yehova anayankhula ndi Mose pa phiri la Sinai.
2 Et ce sont ici les noms des enfants d'Aaron; Nadab, qui était l'aîné, Abihu, Eléazar, et Ithamar.
Mayina a ana aamuna a Aaroni anali Nadabu, woyamba kubadwa, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
3 Ce sont là les noms des enfants d'Aaron Sacrificateurs, qui furent oints et consacrés pour exercer la Sacrificature.
Amenewa ndi mayina a ana aamuna a Aaroni, ansembe odzozedwa omwe anapatulidwa kuti azitumikira ngati ansembe.
4 Mais Nadab et Abihu moururent en la présence de l'Eternel, quand ils offrirent un feu étranger devant l'Eternel au désert de Sinaï, et ils n'eurent point d'enfants; mais Eléazar et Ithamar exercèrent la Sacrificature en la présence d'Aaron leur père.
Koma Nadabu ndi Abihu, anagwa nafa pamaso pa Yehova pamene ankapereka nsembe ndi moto wachilendo pamaso pa Yehova mʼchipululu cha Sinai. Iwowo analibe ana aamuna. Choncho Eliezara ndi Itamara ndiwo amene ankatumikira ngati ansembe nthawi imene Aaroni abambo awo anali moyo.
5 Et l'Eternel parla à Moïse, en disant:
Yehova anati kwa Mose,
6 Fais approcher la Tribu de Lévi, et fais qu'elle se tienne devant Aaron Sacrificateur, afin qu'ils le servent.
“Bweretsa fuko la Levi ndipo ulipereke kwa Aaroni wansembe kuti lizimutumikira.
7 Et qu'ils aient la charge de ce qu'il leur ordonnera de garder, et de ce que toute l'assemblée leur ordonnera de garder, devant le Tabernacle d'assignation, en faisant le service du Tabernacle.
Azigwira ntchito yothandiza iyeyo ndi gulu lonse ku tenti ya msonkhano pogwira ntchito ya ku Chihema.
8 Et qu'ils gardent tous les ustensiles du Tabernacle d'assignation, et ce qui leur sera donné en charge par les enfants d'Israël, pour faire le service du Tabernacle.
Azisamalira zipangizo zonse za mu tenti ya msonkhano, ndipo azigwirira ntchito Aisraeli potumikira mu tenti.
9 Ainsi tu donneras les Lévites à Aaron et à ses fils; ils lui sont absolument donnés d'entre les enfants d'Israël.
Pereka Alevi kwa Aaroni ndi kwa ana ake aamuna. Amenewa ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwa iye kwathunthu.
10 Tu donneras donc la surintendance à Aaron et à ses fils, et ils exerceront leur Sacrificature. Que si quelque étranger en approche, on le fera mourir.
Usankhe Aaroni ndi ana ake aamuna kuti azitumikira pa ntchito ya unsembe. Koma wina aliyense woyandikira malo opatulika aphedwe.”
11 Et l'Eternel parla à Moïse, en disant:
Yehova anawuzanso Mose kuti,
12 Voici, j'ai pris les Lévites d'entre les enfants d'Israël, au lieu de tout premier-né qui ouvre la matrice entre les enfants d'Israël; c'est pourquoi les Lévites seront à moi.
“Pakati pa Aisraeli onse ndatenga Alevi kulowa mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa kwa amayi a Chiisraeli. Alevi ndi anga,
13 Car tout premier-né m'appartient, depuis que je frappai tout premier-né au pays d'Egypte; je me suis sanctifié tout premier-né en Israël, depuis les hommes jusqu'aux bêtes; ils seront à moi, je suis l'Eternel.
pakuti ana onse oyamba kubadwa ndi anga. Nditakantha ana onse oyamba kubadwa mu Igupto, ndinadzipatulira ndekha mwana aliyense woyamba kubadwa mu Israeli, wa munthu ndi nyama. Azikhala anga. Ine ndine Yehova.”
14 L'Eternel parla aussi à Moïse au désert de Sinaï, en disant:
Yehova anawuza Mose mʼchipululu cha Sinai kuti,
15 Dénombre les enfants de Lévi, par les maisons de leurs pères, [et] par leurs familles, en comptant tout mâle depuis l'âge d'un mois, et au dessus.
“Werenga Alevi monga mwa mabanja awo ndi mafuko awo. Werenga mwamuna aliyense kuyambira wa mwezi umodzi kapena kupitirirapo.”
16 Moïse donc les dénombra selon le commandement de l'Eternel, ainsi qu'il lui avait été commandé.
Choncho Mose anawawerenga potsatira zomwe Yehova anamulamulira.
17 r ce sont ici les fils de Lévi selon leurs noms: Guerson, Kéhath, et Mérari.
Mayina a ana aamuna a Levi ndi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
18 Et ce sont ici les noms des fils de Guerson, selon leurs familles, Libni, et Simhi.
Mayina a ana a Geresoni potsata mabanja awo ndi awa: Libini ndi Simei.
19 Et les fils de Kéhath selon leurs familles, Hamram, Jitshar, Hébron et Huziel.
Ana a Kohati potsata mabanja awo ndi awa: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli.
20 Et les fils de Mérari, selon leurs familles, Mahli et Musi; ce sont là les familles de Lévi, selon les maisons de leurs pères.
Ana a Merari potsata mabanja awo ndi awa: Mali ndi Musi. Amenewa ndiwo anali mabanja a Alevi monga mwa makolo awo.
21 De Guerson [est sortie] la famille des Libnites, et la famille des Simhites; ce sont les familles des Guersonites;
Kwa Geresoni kunali banja la Alibini, banja la Asimei. Amenewa ndiwo anali mabanja a Ageresoni.
22 Desquelles ceux dont on fit le dénombrement, après le compte [qui fut fait] de tous les mâles depuis l'âge d'un mois et au dessus, furent au nombre de sept mille cinq cents.
Chiwerengero cha amuna onse amene anawawerenga a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 7,500.
23 Les familles des Guersonites camperont derrière le Tabernacle à l'Occident.
Mabanja a Ageresoni azimanga misasa yawo kumadzulo, kumbuyo kwa Chihema.
24 Et Eliasaph, fils de Laël, sera le chef de la maison des pères des Guersonites.
Mtsogoleri wa mabanja a Ageresoni anali Eliyasafu mwana wa Laeli.
25 Et les enfants de Guerson auront en charge au Tabernacle d'assignation, la tente, le Tabernacle, sa couverture, la tapisserie de l'entrée du Tabernacle d'assignation;
Ntchito imene Ageresoni anapatsidwa ku tenti ya msonkhano inali yosamalira Chihema ndi tenti, pamodzi ndi zophimbira zake, katani ya pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
26 Et les courtines du parvis avec la tapisserie de l'entrée du parvis, qui servent pour le pavillon et pour l'autel, tout autour, et son cordage, pour tout son service.
ndi makatani wotchinga bwalo, katani ya pa chipata cholowera ku bwalo lozungulira Chihema ndi guwa lansembe, zingwe ndi zonse zokhudzana ndi ntchito yawo.
27 Et de Kéhath [est sortie] la famille des Hamramites, la famille des Jitsharites, la famille des Hébronites, et la famille des Huziélites; ce furent là les familles des Kéhathites;
Kwa Kohati kunali mabanja a Amramu, Aizihara, Ahebroni ndi Auzieli. Awa ndiye anali mabanja a Akohati.
28 Dont tous les mâles depuis l'âge d'un mois, et au dessus, furent au nombre de huit mille six cents, ayant la charge du Sanctuaire.
Chiwerengero cha amuna onse a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 8,600. Akohati ankagwira ntchito yosamalira malo wopatulika.
29 Les familles des enfants de Kéhath camperont du côté du Tabernacle vers le Midi.
Mabanja a ana a Kohati ankamanga misasa yawo kummwera kwa Chihema.
30 Et Elitsaphan, fils de Huziel, [sera] le chef de la maison des pères des familles des Kéhathites.
Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Kohati anali Elizafani mwana wa Uzieli.
31 Et ils auront en charge l'Arche, la Table, le chandelier, les autels, et les ustensiles du Sanctuaire avec lesquels on fait le service, et la tapisserie, avec tout ce qui y sert.
Iwo ankagwira ntchito yosamalira Bokosi la Chipangano, tebulo, choyikapo nyale, maguwa, zipangizo za kumalo wopatulika zimene ansembe ankagwiritsa ntchito, katani, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito.
32 Et le chef des chefs des Lévites [sera] Eléazar, fils d'Aaron Sacrificateur; qui aura la surintendance sur ceux qui auront la charge du Sanctuaire.
Mtsogoleri wamkulu wa Alevi anali Eliezara mwana wa Aaroni wansembe. Iye anasankhidwa kukhala woyangʼanira omwe ankasamalira malo wopatulika.
33 Et de Mérari [est sortie] la famille des Mahlites, et la famille des Musites; ce furent là les familles de Mérari;
Kwa Merari kunali banja la Mali ndi banja la Musi. Amenewa ndiye anali mabanja a Amerari.
34 Desquelles ceux dont on fit le dénombrement [après] le compte [qui fut fait] de tous les mâles, depuis l'âge d'un mois et au dessus, furent six mille deux cents.
Chiwerengero cha amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 6,200.
35 Et Esuriel, fils d'Abihaïl, sera le chef de la maison des pères des familles des Mérarites; ils camperont du côté du Tabernacle vers l'Aquilon.
Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Amerari anali Zuriyeli mwana wa Abihaili. Iwo ankamanga misasa yawo kumpoto kwa Chihema.
36 Et on donnera aux enfants de Mérari la charge des ais du Tabernacle, de ses barres, de ses piliers, de ses soubassements, et de tous ses ustensiles, avec tout ce qui y sera;
Amerari anapatsidwa ntchito yosamalira mitengo ya chihema, nsichi zake, mizati yake, matsinde ake, ndi zida zake zonse, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito,
37 Et des piliers du parvis tout autour, avec leurs soubassements, leurs pieux, et leurs cordes.
pamodzi ndi mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema ndi zingwe zake.
38 Et Moïse, et Aaron, et ses fils ayant la charge du Sanctuaire, pour la garde des enfants d'Israël, camperont devant le Tabernacle d'assignation vers l'Orient. Que si quelque étranger en approche, on le fera mourir.
Mose ndi Aaroni ndi ana ake aamuna ankamanga misasa yawo kummawa kwa chihema, kuyangʼana kotulukira dzuwa, kutsogolo kwa tenti ya msonkhano. Anali ndi ntchito yosamalira malo wopatulika mʼmalo mwa Aisraeli. Aliyense woyandikira malo wopatulika ankayenera kuphedwa.
39 Tous ceux des Lévites dont on fit le dénombrement, lesquels Moïse et Aaron comptèrent par leurs familles, suivant le commandement de l'Eternel, tous les mâles de l'âge d'un mois et au dessus, furent de vingt-deux mille.
Alevi onse amene Mose ndi Aaroni anawawerenga potsatira lamulo la Yehova monga mwa magulu a mabanja awo, amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo anali 22,000.
40 Et l'Eternel dit à Moïse: Fais le dénombrement de tous les premiers-nés mâles des enfants d'Israël, depuis l'âge d'un mois, et au dessus, et lève le compte de leurs noms.
Yehova anawuza Mose kuti, “Werenga ana onse aamuna oyamba kubadwa mu Israeli, omwe ali ndi mwezi umodzi kapena kupitirirapo ndipo ulembe mndandanda wa mayina awo.
41 Et tu prendras pour moi, je suis l'Eternel, les Lévites, au lieu de tous les premiers-nés qui sont entre les enfants d'Israël; [tu prendras] aussi les bêtes des Lévites, au lieu de tous les premiers-nés des bêtes des enfants d'Israël.
Unditengere Alevi onse mʼmalo mwa ana oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso ziweto zazimuna za Alevi mʼmalo mwa ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa za Aisraeli. Ine ndine Yehova.”
42 Moïse donc dénombra, comme l'Eternel lui avait commandé, tous les premiers-nés qui étaient entre les enfants d'Israël.
Choncho Mose anawerenga ana aamuna onse oyamba kubadwa a Aisraeli monga momwe Yehova anamulamulira.
43 Et tous les premiers-nés des mâles, le compte des noms étant fait, depuis l'âge d'un mois et au dessus, selon qu ils furent dénombrés, furent vingt-deux mille deux cent soixante et treize.
Chiwerengero chonse cha ana aamuna oyamba kubadwa kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 22, 273.
44 Et l'Eternel parla à Moïse, en disant:
Ndipo Yehova anawuzanso Mose kuti,
45 Prends les Lévites au lieu de tous les premiers-nés qui sont entre les enfants d'Israël, et les bêtes des Lévites, au lieu de leurs bêtes; et les Lévites seront à moi; je suis l'Eternel.
“Tenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso zoweta zonse za Alevi mʼmalo mwa zoweta za Aisraeli. Alevi ndi anga. Ine ndine Yehova.
46 Et quant à ceux qu'il faudra racheter des premiers-nés des enfants d'Israël, qui sont deux cent soixante et treize, plus que les Lévites;
Pofuna kuwombola ana aamuna 273 oyamba kubadwa a Aisraeli amene anaposa chiwerengero cha aamuna a fuko la Levi,
47 Tu prendras cinq sicles par tête, tu les prendras selon le sicle du Sanctuaire; le sicle est de vingt oboles.
utenge masekeli asanu pa munthu aliyense. Masekeliwo akhale ofanana ndi masekeli a ku malo wopatulika, kumene sekeli imodzi imakwanira magera makumi awiri.
48 Et tu donneras à Aaron et à ses fils l'argent de ceux qui auront été rachetés, passant le nombre des Lévites.
Ndalama zimenezi uzipereke kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kuti ukhale mtengo woombolera Aisraeli woonjezerawo.”
49 Moïse donc prit l'argent du rachat de ceux qui étaient de plus, outre ceux qui avaient été rachetés par l'échange des Lévites.
Choncho Mose anatenga ndalama zowombolera zija kuchokera kwa Aisraeli amene chiwerengero chawo chinaposa chiwerengero cha omwe anawomboledwa ndi Alevi.
50 Et il reçut l'argent des premiers-nés des enfants d'Israël, qui fut mille trois cent soixante-cinq sicles, selon le sicle du Sanctuaire.
Anatenga masekeli a siliva okwana 1,365 molingana ndi masekeli a ku malo opatulika, kuchokera kwa ana aamuna oyamba kubadwa a Aisraeli.
51 Et Moïse donna l'argent des rachetés à Aaron, et à ses fils, selon le commandement de l'Eternel, ainsi que l'Eternel le lui avait commandé.
Mose anapereka ndalama zowombolera zija kwa Aaroni ndi ana ake aamuna monga mwa mawu amene Yehova analamulira.

< Nombres 3 >