< Psaumes 126 >

1 Cantique de Mahaloth. Quand l'Eternel ramena les captifs de Sion, nous étions comme ceux qui songent.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
2 Alors notre bouche fut remplie de joie, et notre langue de chant de triomphe, alors on disait parmi les nations: l'Eternel a fait de grandes choses à ceux-ci;
Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
3 L'Eternel nous a fait de grandes choses; nous [en] avons été réjouis.
Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
4 Ô Eternel! ramène nos prisonniers, [en sorte qu'ils soient] comme les courants [des eaux] au pays du Midi.
Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
5 Ceux qui sèment avec larmes, moissonneront avec chant de triomphe.
Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
6 Celui qui porte la semence pour la mettre en terre, ira son chemin en pleurant, mais il reviendra avec chant de triomphe, quand il portera ses gerbes.
Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.

< Psaumes 126 >