< Psaumes 135 >

1 Louez le Nom de l’Eternel; vous serviteurs de l'Eternel, louez-le.
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 Vous qui assistez en la maison de l'Eternel, aux parvis de la maison de notre Dieu,
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Louez l'Eternel, car l'Eternel est bon; psalmodiez à son Nom, car il est agréable.
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 Car l'Eternel s'est choisi Jacob, et Israël pour son plus précieux joyau.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 Certainement je sais que l'Eternel est grand, et que notre Seigneur [est] au-dessus de tous les dieux.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 L'Eternel fait tout ce qu'il lui plaît, dans les cieux et sur la terre, dans la mer, et dans tous les abîmes.
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 C'est lui qui fait monter les vapeurs du bout de la terre; il fait les éclairs pour la pluie; il tire le vent hors de ses trésors.
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 C'est lui qui a frappé les premiers-nés d'Egypte, tant des hommes que des bêtes;
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 Qui a envoyé des prodiges et des miracles au milieu de toi, ô Egypte! contre Pharaon, et contre tous ses serviteurs;
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 Qui a frappé plusieurs nations, et tué les puissants Rois;
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 [Savoir], Sihon le roi des Amorrhéens, et Hog le roi de Hasan, et ceux de tous les Royaumes de Canaan;
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 Et qui a donné leur pays en héritage, en héritage, [dis-je], à Israël son peuple.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 Eternel, ta renommée est perpétuelle; Eternel, la mémoire qu'on a de toi est d'âge en âge.
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 Car l'Eternel jugera son peuple, et se repentira à l'égard de ses serviteurs.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 Les dieux des nations ne sont que de l'or et de l'argent, un ouvrage de mains d'homme.
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 Ils ont une bouche, et ne parlent point; ils ont des yeux, et ne voient point;
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 Ils ont des oreilles, et n'entendent point; il n'y a point aussi de souffle dans leur bouche.
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Que ceux qui les font, [et] tous ceux qui s'y confient, leur soient faits semblables.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 Maison d'Israël, bénissez l'Eternel; maison d'Aaron, bénissez l'Eternel.
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 Maison des Lévites, bénissez l'Eternel; vous qui craignez l'Eternel, bénissez l'Eternel.
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Béni soit de Sion l'Eternel qui habite dans Jérusalem. Louez l'Eternel.
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psaumes 135 >