< Psaumes 146 >

1 Louez l'Eternel. Mon âme, loue l'Eternel.
Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
2 Je louerai l'Eternel durant ma vie, je psalmodierai à mon Dieu tant que je vivrai.
Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
3 Ne vous assurez point sur les principaux [d'entre les peuples, ni] sur [aucun] fils d'homme, à qui [il n'appartient] point de délivrer.
Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
4 Son esprit sort, [et l'homme] retourne en sa terre, [et] en ce jour-là ses desseins périssent.
Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
5 Ô que bienheureux est celui à qui le [Dieu] Fort de Jacob est en aide, [et] dont l'attente est en l'Eternel son Dieu;
Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
6 Qui a fait les cieux et la terre, la mer, et tout ce qui y est, [et] qui garde la vérité à toujours!
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
7 Qui fait droit à ceux à qui on fait tort; et qui donne du pain à ceux qui ont faim. L'Eternel délie ceux qui sont liés.
Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
8 L'Eternel ouvre [les yeux] aux aveugles; l'Eternel redresse ceux qui sont courbés; l'Eternel aime les justes.
Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
9 L'Eternel garde les étrangers, il maintient l'orphelin et la veuve, et renverse le train des méchants.
Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
10 L'Eternel régnera à toujours. Ô Sion! ton Dieu est d'âge en âge. Louez l'Eternel.
Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.

< Psaumes 146 >