< 2 Rois 15 >

1 La vingt-septième année de Jéroboam, roi d'Israël, Asaria, fils d'Amatsia, roi de Juda, devint roi.
Mʼchaka cha 27 cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Azariya mwana wa Amaziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Il était âgé de seize ans quand il commença à régner, et il régna cinquante-deux ans à Jérusalem. Sa mère s'appelait Jécolia, et elle était de Jérusalem.
Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 16 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 52. Amayi ake anali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
3 Il fit ce qui est droit aux yeux de l'Éternel, tout comme Amatsia, son père.
Iyeyo anachita zabwino pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
4 Seulement les hauts lieux ne furent point ôtés. Le peuple sacrifiait encore, et faisait des encensements sur les hauts lieux.
Komabe malo opembedzerako mafano sanawachotse ndipo anthu anapitirizabe kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 Mais l'Éternel frappa le roi, qui fut lépreux jusqu'au jour de sa mort, et demeura dans une maison écartée; et Jotham, fils du roi, avait l'intendance du palais et jugeait le peuple du pays.
Ndipo Yehova analanga mfumu ndi nthenda ya khate mpaka tsiku limene inamwalira. Tsono mfumuyo inkakhala mʼnyumba yakeyake yapadera. Mwana wake Yotamu ndiye amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu ndiponso ndiye amene ankalamulira anthu mʼdzikomo.
6 Le reste des actions d'Asaria, tout ce qu'il fit, n'est-il pas écrit au livre des Chroniques des rois de Juda?
Ntchito zina za Azariya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
7 Or Asaria s'endormit avec ses pères, et fut enseveli avec ses pères, dans la cité de David; et Jotham, son fils, régna à sa place.
Azariya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
8 La trente-huitième année d'Asaria, roi de Juda, Zacharie, fils de Jéroboam, devint roi sur Israël à Samarie, et il régna six mois.
Mʼchaka cha 38 cha Azariya mfumu ya Yuda, Zekariya mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya ndipo analamulira miyezi isanu ndi umodzi.
9 Il fit ce qui est mauvais aux yeux de l'Éternel, comme avaient fait ses pères. Il ne se détourna point des péchés de Jéroboam, fils de Nébat, par lesquels il avait fait pécher Israël.
Ndipo iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira makolo ake. Iye sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
10 Or Shallum, fils de Jabèsh, fit une conspiration contre lui, le frappa en présence du peuple, et le tua; et il devint roi à sa place.
Salumu mwana wa Yabesi anachitira chiwembu Zekariya. Anamukantha anthu akuona, namupha, ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
11 Quant au reste des actions de Zacharie, voici, cela est écrit au livre des Chroniques des rois d'Israël.
Ntchito zina za Zekariya, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
12 C'est là la parole que l'Éternel avait adressée à Jéhu, en disant: Tes fils seront assis sur le trône d'Israël jusqu'à la quatrième génération. Il en fut ainsi.
Awa ndiwo mawu a Yehova amene anayankhula kwa Yehu kuti, “Ana ako adzalamulira Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
13 Shallum, fils de Jabèsh, devint roi la trente-neuvième année d'Ozias, roi de Juda, et il régna un mois à Samarie.
Salumu mwana wa Yabesi anakhala mfumu mʼchaka cha 39 cha ulamuliro wa Uziya mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Samariya mwezi umodzi.
14 Et Ménahem, fils de Gadi, monta de Thirtsa, entra à Samarie, frappa Shallum, fils de Jabèsh, à Samarie, et le tua; et il devint roi à sa place.
Ndipo Menahemu mwana wa Gadi anachoka ku Tiriza napita ku Samariya nakantha Salumu mwana wa Yabesi ku Samariya, namupha ndipo iye analowa ufumu mʼmalo mwake.
15 Le reste des actions de Shallum, et la conspiration qu'il fit, voici, cela est écrit au livre des Chroniques des rois d'Israël.
Ntchito zina za Salumu ndiponso za chiwembu chimene anachita, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
16 Alors Ménahem frappa Thiphsach, et tous ceux qui y étaient, et sa contrée depuis Thirtsa, parce qu'elle ne lui avait pas ouvert ses portes. Il la frappa, et éventra toutes ses femmes enceintes.
Nthawi imeneyo Menahemu, kuchokera ku Tiriza, anakathira nkhondo mzinda wa Tipisa ndi anthu onse amene anali mʼmenemo ndi dera lonse lozungulira chifukwa iwo anakana kutsekula zipata zawo. Iye anatenga katundu yense mu mzinda wa Tipisa ndi kutumbula akazi onse oyembekezera.
17 La trente-neuvième année d'Asaria, roi de Juda, Ménahem, fils de Gadi, devint roi sur Israël, et il régna dix ans à Samarie.
Mʼchaka cha 39 cha Azariya mfumu ya Yuda, Menahemu mwana wa Gadi anakhala mfumu ya Israeli ndipo analamulira mu Samariya zaka khumi.
18 Il fit ce qui est mauvais aux yeux de l'Éternel. Pendant toute sa vie, il ne se détourna pas des péchés de Jéroboam, fils de Nébat, par lesquels il avait fait pécher Israël.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Nthawi yonse ya ulamuliro wake sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
19 Pul, roi d'Assyrie, étant venu contre le pays, Ménahem donna mille talents d'argent à Pul pour qu'il lui aidât à affermir la royauté entre ses mains.
Tsono Puli mfumu ya ku Asiriya inadzathira nkhondo dzikolo ndipo Menahemu anapatsa Puliyo makilogalamu 34,000 a siliva kuti amuthandize ndi kulimbikitsa ufumu wake.
20 Or, Ménahem tira cet argent d'Israël, de tous ceux qui étaient puissants en biens, pour le donner au roi d'Assyrie: de chacun cinquante sicles d'argent. Ainsi le roi d'Assyrie s'en retourna, et ne s'arrêta point dans le pays.
Menahemu anapeza ndalamazo kudzera mu msonkho umene ankakhometsa Aisraeli. Munthu aliyense wachuma ankapereka masekeli a siliva makumi asanu kwa mfumu ya ku Asiriya. Choncho mfumu ya ku Asiriya inabwerera ndipo sinakhalenso mʼdzikomo.
21 Le reste des actions de Ménahem, et tout ce qu'il fit, cela n'est-il pas écrit au livre des Chroniques des rois d'Israël?
Ntchito zina za Menahemu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
22 Et Ménahem s'endormit avec ses pères, et Pékachia, son fils, régna à sa place.
Menahemu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Pekahiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
23 La cinquantième année d'Asaria, roi de Juda, Pékachia, fils de Ménahem, devint roi sur Israël à Samarie, et il régna deux ans.
Mʼchaka cha makumi asanu a Azariya mfumu ya Yuda, Pekahiya mwana wa Menahemu anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka ziwiri.
24 Il fit ce qui est mauvais aux yeux de l'Éternel. Il ne se détourna point des péchés de Jéroboam, fils de Nébat, par lesquels il avait fait pécher Israël.
Pekahiya anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Iye sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, omwe anachimwitsa nawo Israeli.
25 Et Pékach, fils de Rémalia, son officier, fit une conspiration contre lui et le frappa, à Samarie, dans le palais de la maison du roi, avec Argob et Arié, ayant avec lui cinquante hommes des enfants des Galaadites. Ainsi il le tua, et il régna à sa place.
Ndipo Peka mwana wa Remaliya, mtsogoleri wake wa ankhondo, anamuchita chiwembu. Iye pamodzi ndi anthu makumi asanu a ku Giliyadi anapha Pekahiya pamodzi ndi Arigobu ndi Ariyeli mʼchipinda choteteza nyumba ya mfumu mu Samariya. Kotero Peka anapha Pekahiya ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
26 Le reste des actions de Pékachia, et tout ce qu'il fit, voici, cela est écrit au livre des Chroniques des rois d'Israël.
Ntchito zina za Pekahiya ndi zonse zimene anachita zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
27 La cinquante-deuxième année d'Asaria, roi de Juda, Pékach, fils de Rémalia, devint roi sur Israël, à Samarie, et il régna vingt ans.
Mʼchaka cha 52 cha Azariya mfumu ya Yuda, Peka mwana wa Remaliya anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya ndipo analamulira zaka makumi awiri.
28 Il fit ce qui est mauvais aux yeux de l'Éternel; et il ne se détourna point des péchés de Jéroboam, fils de Nébat, par lesquels il avait fait pécher Israël.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
29 Du temps de Pékach, roi d'Israël, Tiglath-Piléser, roi d'Assyrie, vint et prit Ijjon, Abel-Beth-Maaca, Janoach, Kédès, Hatsor, Galaad, la Galilée, tout le pays de Nephthali, et il en transporta le peuple en Assyrie.
Nthawi ya Peka mfumu ya Israeli, Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kudzalanda Iyoni, Abeli-Beti-Maaka, Yanowa, Kedesi ndi Hazori. Mfumu ya ku Asiriya inatenga Giliyadi ndi Galileya, kuphatikizanso madera onse a Nafutali ndipo anatumiza Aisraeli ku Asiriya.
30 Et Osée, fils d'Éla, fit une conspiration contre Pékach, fils de Rémalia, le frappa et le tua; et il devint roi à sa place, la vingtième année de Jotham, fils d'Ozias.
Kenaka Hoseya mwana wa Ela anachitira chiwembu Peka mwana wa Remaliya. Anamukantha ndi kumupha ndipo anakhala mfumu mʼmalo mwake mʼchaka makumi awiri cha Yotamu mwana wa Uziya.
31 Le reste des actions de Pékach, et tout ce qu'il fit, voici, cela est écrit au livre de Chroniques des rois d'Israël.
Ntchito zina za Peka ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
32 La seconde année de Pékach, fils de Rémalia, roi d'Israël, Jotham, fils d'Ozias, roi de Juda, commença à régner.
Mʼchaka chachiwiri cha Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli, Yotamu mwana wa Uziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
33 Il était âgé de vingt-cinq ans quand il commença à régner, et il régna seize ans à Jérusalem. Sa mère s'appelait Jérusha, fille de Tsadok.
Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Amayi ake anali Yerusa mwana wa Zadoki.
34 Il fit ce qui est droit aux yeux de l'Éternel, il fit tout comme avait fait Ozias, son père.
Iye anachita zabwino pamaso pa Yehova monga anachitira Uziya abambo ake.
35 Seulement les hauts lieux ne furent point ôtés. Le peuple sacrifiait encore et faisait des encensements dans les hauts lieux. Ce fut lui qui bâtit la porte Haute de la maison de l'Éternel.
Komabe malo opembedzera mafano sanawachotse ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
36 Le reste des actions de Jotham, et tout ce qu'il fit, n'est-il pas écrit au livre des Chroniques des rois de Juda?
Ntchito zina za Yotamu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
37 En ces jours-là, l'Éternel commença d'envoyer contre Juda Retsin, roi de Syrie, et Pékach, fils de Rémalia.
(Nthawi imeneyo, Yehova anayamba kumatuma Rezini mfumu ya Aaramu ndi Peka mwana wa Remaliya kudzamenyana ndi Yuda).
38 Et Jotham s'endormit avec ses pères, et fut enseveli avec ses pères dans la cité de David, son père. Et Achaz, son fils, régna à sa place.
Yotamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Ahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Rois 15 >