< Job 18 >

1 Et Bildad de Such répondit et dit:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Jusques à quand chasserez-vous aux mots? Prenez du sens, puis nous parlerons!
“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
3 Pourquoi nous tient-on pour des brutes, sommes-nous stupides à vos yeux?
Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
4 Toi, qui dans ta fureur te déchires toi-même, la terre à cause de toi sera-t-elle désertée, et le rocher transporté de sa place?
Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
5 Aussi bien la lumière des impies s'éteint, et la flamme de son feu cesse de briller;
“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
6 la lumière de sa tente s'éclipse, et sa lampe au-dessus de lui s'éteint;
Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
7 sa vigoureuse allure s'embarrasse, et il se perd par les mesures qu'il prend;
Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
8 car ses pieds mêmes le conduisent au piège, et il marche sur des lacs;
Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
9 le lacet le saisit au talon, et le filet se rend maître de lui;
Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
10 le sol pour lui recouvre des rêts, et la trappe l'attend sur le sentier.
Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
11 De toutes parts des terreurs l'épouvantent, et le pressent par derrière.
Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
12 Le malheur est avide de lui, et la misère s'apprête à le faire tomber.
Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
13 Il dévore les membres de son corps, il dévore ses membres, le Premier-né de la Mort.
Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
14 Il est arraché de sa tente, sa sécurité, et traîné vers le Roi de l'épouvante.
Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
15 D'autres que les siens viennent habiter sa tente, et le soufre tombe en pluie sur sa demeure;
Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
16 à ses pieds ses racines sèchent, à son sommet son rameau se flétrit,
Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
17 sa mémoire disparaît du pays, et il n'a plus un nom dans les campagnes;
Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
18 il est refoulé de la lumière dans la nuit, et banni de la terre;
Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
19 il n'a dans son peuple ni race, ni lignée, et pas un reste de lui dans ses demeures;
Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
20 son jour terrifie la postérité, et fait frissonner les contemporains.
Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
21 Ainsi seulement finissent les demeures du méchant, et ainsi le séjour de qui méconnaît Dieu.
Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”

< Job 18 >