< Josué 1 >

1 Et après la mort de Moïse, serviteur de l'Éternel, l'Éternel parla à Josué, fils de Nun, qui était au service de Moïse, en ces termes:
Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
2 Moïse, mon serviteur, est mort; lève-toi donc maintenant, passe ce Jourdain, toi et tout ce peuple, pour entrer dans le pays que je leur donne, aux enfants d'Israël.
“Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
3 Tous les lieux que touchera la plante de vos pieds, je vous les ai donnés, selon la promesse que j'ai faite à Moïse,
Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
4 depuis le Désert et le Liban que voilà, jusqu'au Grand Fleuve, l'Euphrate, tout le pays des Héthiens et jusqu'à la Grande Mer vers le soleil couchant, telle sera votre frontière.
Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
5 Personne ne tiendra devant toi, tant que tu vivras: je serai avec toi, de même que j'ai été avec Moïse; je ne te laisserai ni au dépourvu, ni dans l'abandon.
Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
6 Aie courage et fermeté, car c'est à toi de mettre ce peuple en possession du pays que j'ai juré à leurs pères de leur donner.
“Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
7 Aie seulement courage et grande fermeté, t'appliquant à agir en toutes choses d'après la Loi que t'a prescrite Moïse, mon serviteur; ne t'en écarte ni à droite ni à gauche, afin que tu réussisses dans toutes tes entreprises.
Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
8 Aie incessamment dans la bouche [les paroles du] livre de cette Loi, médite-le jour et nuit, pour avoir soin d'agir d'après tout ce qui y est consigné, car alors tu trouveras sur ta route réussite et succès.
Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
9 Ne t'ai-je pas donné cet ordre: Aie courage et fermeté? Ne prends ni alarme, ni épouvante, car tu as avec toi l'Éternel, ton Dieu, à tous les pas que tu feras.
Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
10 Alors Josué donna cet ordre aux Officiers du peuple:
Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
11 Parcourez le camp et transmettez au peuple cet ordre: Pourvoyez-vous de vivres, car dans trois jours vous serez près de passer ce Jourdain pour marcher à la conquête du pays que l'Éternel, votre Dieu, vous donne pour le conquérir.
“Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
12 Et aux Rubénites et aux Gadites et à la demi-Tribu de Manassé Josué parla en ces termes:
Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
13 Souvenez-vous de la condition que vous a prescrite Moïse, serviteur de l'Éternel, quand il disait: L'Éternel, votre Dieu, vous a donné votre lieu de repos, et concédé cette contrée-ci.
“Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
14 Vos femmes, vos enfants et vos troupeaux resteront dans la contrée que vous a donnée Moïse au delà du Jourdain; mais vous, vous marcherez équipés à la tête de vos frères, vous tous les braves guerriers, et vous les aiderez,
Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
15 jusqu'à ce que l'Éternel ait donné à vos frères leur lieu de repos comme à vous, et qu'eux aussi aient conquis le pays que l'Éternel, votre Dieu, leur donne. Alors vous regagnerez la contrée qui vous appartient, et vous occuperez ce lot que vous a donné Moïse, serviteur de l'Éternel, au delà du Jourdain, vers le soleil levant.
Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
16 Alors ils répondirent à Josué et dirent: Nous exécuterons tous tes ordres, et nous irons partout où tu nous enverras.
Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
17 En toutes choses nous t'obéirons comme nous avons obéi à Moïse. Puisse seulement l'Éternel, ton Dieu, être avec toi, de même qu'il fut avec Moïse!
Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
18 Tout homme qui résistera à tes ordres et n'obéira pas à tes paroles dans tout ce que tu lui commanderas, doit être mis à mort. Aie seulement courage et fermeté!
Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”

< Josué 1 >