< Josué 13 >

1 Cependant Josué était vieux, avancé en âge. Alors l'Éternel lui dit: Tu es vieux, avancé en âge, et il reste encore une très grande partie du pays à conquérir;
Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
2 cette partie du pays qui reste, c'est tous les cantons des Philistins, et la totalité du Gessuri,
“Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
3 depuis le Sihor (Nil) qui coule devant l'Egypte jusqu'à la limite de Ecron au nord doit être réputée Cananéenne; cinq princes des Philistins, celui de Gazal et celui d'Asdod, celui d'Ascalon, celui de Gath et celui de Ecron et les Avvites au midi;
kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
4 tout le pays des Cananéens et la caverne appartenant aux Sidoniens jusqu'à Aphek, jusqu'à la frontière des Amoréens;
Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
5 et le pays des Giblites et tout le Liban du côté du soleil levant depuis Baal-Gad au pied du mont Hermon jusqu'aux abords de Hamath.
Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
6 Tous les habitants des montagnes depuis le Liban aux Eaux qui brûlent, tous les Sidoniens, je les chasserai devant les enfants d'Israël; partage seulement ce pays par le sort à Israël comme patrimoine, ainsi que je te l'ai prescrit.
“Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
7 A présent donc répartis-le par lots aux neuf Tribus et à la demi-Tribu de Manassé.
Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
8 Les Rubénites et les Gadites ont reçu avec l'autre moitié [de Manassé] leurs lots que Moïse leur a donnés au delà du Jourdain à l'orient, comme Moïse, serviteur de l'Éternel, le leur a donné,
Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
9 savoir depuis Aroër au bord de la rivière de l'Arnon depuis la ville qui est au milieu du ravin de l'Arnon, et tout le pays plat de Medéba jusqu'à Dibon
Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
10 et toutes les villes de Sihon, Roi des Amoréens qui régnait à Hesbon, jusqu'à la frontière des fils d'Ammon,
Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
11 et Galaad et les Gessurites et les Maachatites et toute la montagne de l'Hermon, et tout Basan jusqu'à Salcha;
Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
12 tout le royaume de Og, Roi de Basan qui régnait à Astaroth et à Edreï (l'un des restes des Rephaïms); et Moïse les vainquit et les expulsa.
Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
13 Mais les enfants d'Israël n'expulsèrent point les Gessurites ni les Maachatites qui ont vécu au sein d'Israël jusqu'aujourd'hui.
Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
14 Il n'y eut que la Tribu de Lévi à laquelle il ne donna point de lot; les sacrifices ignés faits à l'Éternel, Dieu d'Israël, tel est son lot, comme Il le lui a dit.
Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
15 Et Moïse dota la Tribu des fils de Ruben en raison de ses familles.
Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
16 Et leur territoire, à partir d'Aroër au bord de la rivière de l'Arnon, de la ville située au centre du ravin, comprenait aussi tout le pays plat près de Medéba,
Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
17 Hesbon et toutes ses villes dans le pays plat, Dibon, et Bamoth-Baal et Beth Baal-Meon
Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
18 et Jahtsa et Kedémoth et Mephaath
Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
19 et Kiriathaïm et Sibma et Tséreth-Sahar dans la montagne de la vallée,
Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
20 et Beth-Pehor, et les versants du Pisga et Beth-Jesimoth,
Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
21 et toutes les villes du pays plat et tout le royaume de Sihon, Roi des Amoréens, qui régnait à Hesbon, que Moïse vainquit ainsi que les Princes de Madian, Evi et Rekem et Tsur et Hur et Reba, vassaux de Sihon qui habitaient dans le pays.
Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
22 Et les enfants d'Israël tuèrent avec l'épée Balaam, fils de Behor, le devin, qu'ils ajoutèrent aux morts.
Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
23 Et la frontière des fils de Ruben fut le Jourdain et le territoire adjacent. Tel est le lot des fils de Ruben selon leurs familles, les villes avec leurs villages.
Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
24 Et Moïse dota la Tribu de Gad, les fils de Gad, d'après leurs familles.
Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
25 Et leur territoire comprenait Jaëzer et toutes les villes de Galaad, et la moitié du pays des fils d'Ammon jusqu'à Aroër située devant Rabba,
Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
26 puis s'étendait depuis Hesbon jusqu'à Ramath-Mitspeh et Bethonim, et de Mahanaïm à la frontière de Debir;
ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
27 et dans la vallée ils eurent Beth-Haram et Beth-Nimra et Succoth et Tsaphon, reste du royaume de Sihon, Roi de Hesbon, le Jourdain et le territoire adjacent jusqu'à l'extrémité de la Mer Kinnéroth, au delà du Jourdain à l'orient.
Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
28 Tel fut le lot des fils de Gad selon leurs familles, les villes avec leurs villages.
Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
29 Et Moïse dota la demi-Tribu de Manassé, et la demi-Tribu des fils de Manassé fut pourvue en raison de ses familles.
Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
30 Et à partir de Mahanaïm leur territoire comprenait tout Basan, tout le royaume de Og, Roi de Basan, et tous les bourgs de Jaïr situés en Basan: soixante villes.
Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
31 Et la moitié de Galaad et Astaroth et Edreï, les villes du royaume de Og en Basan échurent aux fils de Machir, fils de Manassé, à la moitié des fils de Machir selon leurs familles.
Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
32 C'est là ce dont Moïse fit le partage dans les plaines de Moab au delà du Jourdain près de Jéricho, à l'orient.
Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
33 Quant à la Tribu de Lévi, Moïse ne lui donna pas de lot; l'Éternel, Dieu d'Israël, tel est son lot, comme Il le lui a dit.
Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.

< Josué 13 >