< Luc 23 >

1 Tous alors se levèrent en foule et le conduisirent à Pilate!
Kenaka gulu lonse la anthuwo linayimirira ndi kumutengera kwa Pilato.
2 Leur premier chef d'accusation fut: «Nous avons trouvé cet homme excitant notre peuple à la révolte, l'empêchant de payer le tribut à César, et se disant le Christ-roi.»
Ndipo iwo anayamba kumuneneza nati, “Ife tinapeza munthu uyu akusokoneza anthu a mtundu wathu ndipo amatsutsa zopereka msonkho kwa Kaisara komanso amati ndi Khristu, Mfumu.”
3 Pilate l'interrogea: «C'est toi qui es le roi des Juifs?» lui demanda-t-il. Jésus répondit ainsi: «Tu le dis.»
Pamenepo Pilato anamufunsa Yesu kuti, “Kodi Iwe ndiwe Mfumu ya Ayuda?” Yesu anayankha kuti, “Mwatero ndinu.”
4 Pilate, s'adressant aux chefs des prêtres et à la foule: «Chez cet homme je ne trouve rien de coupable», leur dit-il.
Kenaka Pilato anawawuza akulu a ansembe ndi gulu la anthu, “Ine sindikumupeza cholakwa munthuyu.”
5 Eux pourtant insistaient avec force, disant: «Il agitait le peuple, il parcourait toute la Judée, en enseignant; et c'est après avoir commencé par la Galilée qu'il est arrivé jusqu'ici.»
Koma iwo analimbikirabe kuti, “Iyeyu amasokoneza anthu ku Yudeya konse ndi chiphunzitso chake, Iyeyu anayambira ku Galileya ndipo wayenda mtunda wonse mpaka kuno.”
6 A ces paroles, Pilate demande si l'homme était Galiléen;
Pakumva zimenezi, Pilato anafunsa ngati munthuyo ndi Mgalileya.
7 et, apprenant qu'il, était sujet d'Hérode, il l'envoya à celui-ci, lequel se trouvait à Jérusalem ces jours-là.
Iye atamva kuti Yesu anali pansi pa ulamuliro wa Herode, anamutumiza kwa Herodeyo, amene pa nthawi imeneyo analinso mu Yerusalemu.
8 Pour Hérode, voir Jésus, fut une grande joie. Il y avait longtemps qu'il souhaitait de le connaître; il avait entendu parler de lui; et il espérait lui voir faire un miracle.
Herode ataona Yesu, anakondwa kwambiri, chifukwa kwa nthawi yayitali, ankafunitsitsa atamuona. Kuchokera pa zimene anamva za Iye, anayembekezera kuti achita zodabwitsa.
9 Aussi l'interrogea-t-il longuement; mais Jésus ne lui répondit rien. —
Iye anamufunsa mafunso ambiri, koma Yesu sanayankhe.
10 Quant aux chefs des prêtres et aux Scribes, ils étaient là debout l'accusant sans relâche. —
Akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, anayimirira pamenepo ndi kumuneneza kwambiri.
11 Alors Hérode ne fit plus aucun cas de Jésus; ses soldats et lui le raillèrent, et il le renvoya à Pilate après l'avoir affublé d'une robe blanche.
Pamenepo Herode ndi asilikali ake anamuseka ndi kumunyoza Iye. Atamuveka mkanjo wonyezimira, anamutumizanso kwa Pilato.
12 Hérode et Pilate, qui avaient vécu jusque-là en inimitié, devinrent amis, à dater de ce jour.
Tsiku limenelo, Herode ndi Pilato anakhala abwenzi. Zisanachitike izi anali adani.
13 Réunissant les chefs des prêtres, les magistrats et le peuple,
Pilato anasonkhanitsa akulu a ansembe, oweruza ndi anthu,
14 Pilate leur dit: «Vous m'avez présenté cet homme comme excitant le peuple à la révolte, et voilà qu'après enquête faite en votre présence, je ne l'ai trouvé en rien coupable de ce dont vous l'accusez.
ndipo anawawuza kuti, “Munabweretsa munthuyu kwa ine ngati ndiye amawuza anthu kuti awukire. Ine ndamufunsa pamaso panu ndipo sindinapeze chomuyimbira mlandu.
15 Hérode, non plus, car il nous l'a renvoyé. Ainsi il n'a rien fait qui mérite la mort.
Herodenso sanapeze chifukwa pakuti wamutumizanso kwa ife monga mmene mukuoneramu. Iyeyu sanachite chinthu chakuti aphedwe.
16 Je vais donc, après l'avoir fait frapper de verges, lui rendre la liberté.»
Nʼchifukwa chake, ine ndingomulanga, nʼkumumasula.”
17 (A chaque fête, il était obligé de leur relâcher un prisonnier).
(Pa nthawi yachikondwerero cha Paska iye ankayenera kumasula munthu mmodzi).
18 Alors tous, d'une seule voix, se mirent à crier «A mort celui-là! délivre-nous Bar-Abbas!»
Onse pamodzi anafuwula kuti, “Muchotseni munthuyu! Timasulireni Baraba!”
19 (C'était un homme qui avait été incarcéré pour avoir commis un meurtre à la suite d'une émeute qui avait eu lieu dans la ville.)
(Baraba anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe mu mzinda ndi kupha).
20 Pilate, qui désirait délivrer Jésus, leur parla de nouveau.
Pofuna kumumasula Yesu, Pilato anawadandaulira iwo.
21 Ils lui répondirent par des cris: «Crucifie-le! crucifie-le!»
Koma iwo anapitirirabe kufuwula kuti, “Mpachikeni! Mpachikeni!”
22 Pour la troisième fois, il leur demanda: «Mais quel mal a-t-il fait, cet homme? Je ne le trouve coupable de rien qui mérite la mort. Je vais donc, après l'avoir fait frapper de verges, lui rendre la liberté.»
Kachitatu anawafunsanso iwo kuti, “Chifukwa chiyani? Kodi munthu uyu wachita choyipa chanji? Ine sindinapeze cholakwa mwa Iye chakuti aphedwe choncho ndingomukwapula ndi kumumasula.”
23 Mais ils insistaient, ils demandaient à grands cris qu'on le crucifiât, et ce furent leurs cris qui l'emportèrent.
Koma ndi mawu ofuwulitsa, analimbikirabe kuti Iye apachikidwe, ndipo kufuwulako kunapitirira.
24 Pilate prononça une sentence conforme à leur demande.
Choncho Pilato anatsimikiza kuchita zofuna zawozo.
25 Il mit en liberté, à leur requête, celui qui avait été incarcéré pour émeute et pour meurtre, et il abandonna Jésus à leur volonté.
Iye anawamasulira munthu amene anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe ndi kupha, amene ankamufunayo, ndipo anawapatsa Yesu mwakufuna kwawo.
26 Comme ils l'emmenaient, ils rencontrèrent un certain Simon de Cyrène qui revenait des champs, et ils le chargèrent de porter la croix derrière Jésus.
Ndipo pamene ankapita naye, anagwira Simoni wa ku Kurene, amene ankachokera ku munda, namusenzetsa mtanda namuyendetsa pambuyo pa Yesu.
27 Une immense multitude de peuple le suivait, ainsi que des femmes qui se lamentaient et le pleuraient.
Gulu lalikulu la anthu linamutsata Iye, kuphatikiza amayi amene ankabuma ndi kumulirira.
28 Se tournant vers elles, Jésus dit: «Filles de Jérusalem, ne pleurez pas sur moi, mais pleurez sur vous et sur vos enfants;
Yesu anatembenuka nati kwa iwo, “Ana aakazi a Yerusalemu, musandilirire Ine; dzililireni nokha ndi ana anu.
29 voici, en effet, que viennent des jours où l'on dira: «Heureuses les stériles; heureuses les entrailles qui n'ont point enfanté, et les mamelles qui n'ont point allaité!»
Pakuti nthawi idzabwera imene inu mudzati, ‘Ndi odala amayi osabereka, mimba zimene sizinabereke ndi mawere amene sanayamwitse!’
30 On se mettra alors à dire aux montagnes: Tombez sur nous! Et aux collines: Recouvrez-nous!»
Kenaka, “adzawuza mapiri kuti tigwereni ife; zitunda kuti tiphimbeni ife.
31 Car si le bois vert est ainsi traité, qu'arrivera-t-il au bois sec?»
Chifukwa ngati anthu akuchita izi pa mtengo wauwisi, chidzachitike nʼchiyani ndi wowuma?”
32 On emmenait aussi deux autres hommes, des malfaiteurs, pour les mettre à mort avec lui.
Amuna ena awiri, onsewo achifwamba, anatengedwanso pamodzi ndi Yesu kukaphedwa.
33 Ils arrivèrent à l'endroit qui porte le nom de Crâne. Là on le crucifia, ainsi que les deux malfaiteurs, l'un à sa droite, l'autre à sa gauche.
Pamene anafika pamalo otchedwa Bade, anamupachika Iye pamodzi ndi achifwambawo, mmodzi kudzanja lake lamanja ndi winayo la ku lamazere.
34 Jésus disait: «Père! pardonne-leur, car ils ne savent ce qu'ils font!» Ses vêtements furent partagés après avoir été tirés au sort.
Yesu anati, “Atate, akhululukireni, pakuti sakudziwa chimene akuchita.” Ndipo anagawana malaya ake mochita maere.
35 Le peuple se tenait tout autour et regardait. Quant à ceux qui étaient les chefs de la nation, ils se moquaient, disant: «Il en a sauvé d'autres; qu'il se sauve lui-même s'il est le Christ, l'Élu de Dieu.»
Anthu anayimirira nʼkumaonerera, ngakhalenso akuluakulu ankamulalatira Iye. Iwo anati, “Iye anapulumutsa ena; adzipulumutse yekha ngati ndi Khristu wa Mulungu, Wosankhidwayo.”
36 Les soldats aussi le raillaient; ils, s'approchaient, ils lui offraient du vinaigre,
Asilikalinso anabwera ndi kumunyoza Iye. Iwo anamupatsa vinyo wosasa,
37 ils lui disaient: «Si tu es le Roi des Juifs, sauve-toi!»
ndipo anati, “Ngati ndiwe Mfumu ya Ayuda, dzipulumutse wekha.”
38 Au-dessus de lui, il y avait une inscription: CELUI-CI EST LE ROI DES JUIFS.
Ndipo panalembedwa chikwangwani pamwamba pake chimene chinati: uyu ndi mfumu ya ayuda.
39 Un des malfaiteurs suspendus en croix l'injuriait: «N'es-tu pas le Christ? Sauve-toi et nous avec toi!»
Mmodzi wa achifwambawo, amene anapachikidwa, anamunenera Iye zamwano nati, “Kodi sindiwe Khristu? Dzipulumutse wekha ndi ifenso!”
40 Mais l'autre éleva la voix pour le reprendre: «Est-ce que, toi non plus, tu ne crains pas Dieu, lui dit-il; toi qui subis le même supplice;
Koma wachifwamba winayo anamudzudzula iye nati, “Suopa Mulungu, iwenso ukulandira chilango chomwechi?
41 et pour nous ce n'est que justice; nous recevons ce qu'ont mérité nos actes; mais celui-ci n'a rien fait de mal.»
Ife tikulangidwa mwachilungamo, pakuti ife tikulandira monga mwa ntchito zathu. Koma munthu uyu sanachimwe kanthu.”
42 Et il disait: «Jésus, souviens-toi de moi quand tu viendras en ton Royaume!» —
Kenaka anati, “Yesu, mundikumbukire ine pamene mulowa mu ufumu wanu.”
43 «En vérité, je te le dis, lui répondit Jésus, aujourd'hui tu seras avec moi dans le Paradis.»
Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, ndikukuwuza kuti lero lino udzakhala ndi Ine mʼparadaiso.”
44 Il était déjà la sixième heure environ et, le soleil s'étant éclipsé, des ténèbres se firent sur tout le pays jusqu'à la neuvième heure.
Linali tsopano pafupi ora lachisanu ndi chimodzi, ndipo mdima unagwa pa dziko lonse mpaka ora lachisanu ndi chinayi,
45 Le rideau du Temple se déchira par le milieu;
pakuti dzuwa linaleka kuwala. Ndipo chinsalu cha mʼNyumba ya Mulungu chinangʼambika pakati.
46 et Jésus dit, en jetant un grand cri: «Père, Je remets mon esprit entre tes mains.» En disant cela, il expira.
Yesu anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Atate, ndikupereka mzimu wanga mʼmanja mwanu.” Atanena zimenezi, anamwalira.
47 Voyant ce qui se passait, le centurion glorifia Dieu, disant: «Certainement cet homme était juste!»
Kenturiyo, ataona zimene zinachitikazi, analemekeza Mulungu ndipo anati, “Zoonadi, uyu anali munthu wolungama.”
48 Et tous ceux qui avaient assisté en foule à ce spectacle et avaient été témoins de ce qui était arrivé, s'en retournaient en se frappant la poitrine.
Anthu onse amene anasonkhana kudzaonerera izi, ataona zinachitikazo, anadziguguda pachifuwa ndipo anachoka.
49 Quant à ceux qui l'avaient connu, ils se tenaient tous à distance, ainsi que des femmes qui l'avaient suivi depuis la Galilée, et ils regardaient.
Koma onse amene anamudziwa Iye, kuphatikiza amayi amene anamutsatira kuchokera ku Galileya, anayimirira akuona zinthu izi.
50 Survint un membre du Grand-Conseil appelé Joseph. C'était un homme juste et bon,
Ndipo taonani panali munthu wina wotchedwa Yosefe, mmodzi wa gulu loweruza, munthu wabwino ndi wolungama.
51 qui ne s'était associé ni aux projets ni aux actes des autres. (Il était d'Arimathée, ville des Juifs.) Lui aussi attendait le Royaume de Dieu.
Iye sanavomereze zimene anzake abwalo anagwirizana ndi kuchita. Iye ankachokera ku mudzi wa Arimateyu wa ku Yudeya ndipo ankayembekezera ufumu wa Mulungu.
52 Il alla trouver Pilate et demanda le corps de Jésus.
Atapita kwa Pilato, iye anakapempha mtembo wa Yesu.
53 Puis il le descendit de la croix, l'ensevelit dans un linceul, et le déposa dans un sépulcre taillé dans le roc, où personne encore n'avait été placé.
Ndipo anawutsitsa, nawukulunga nsalu yabafuta nawuyika mʼmanda wosemedwa mʼmwala, amene panalibe wina amene anayikidwamo.
54 C'était un jour de Préparation et un sabbat allait commencera.
Linali tsiku lokonzekera ndipo Sabata linatsala pangʼono kuyamba.
55 Des femmes, celles qui étaient venues avec Jésus de Galilée, ayant accompagné Joseph, virent le tombeau et comment y fut placé le corps;
Amayi amene anabwera ndi Yesu kuchokera ku Galileya, anatsata Yosefe ndipo anaona manda ndi momwe mtembo wake anawuyikira.
56 puis elles s'en retournèrent préparer des aromates et des parfums. Selon le commandement, elles se tinrent en repos le jour du, sabbat.
Kenaka anapita ku mudzi ndi kukakonza mafuta onunkhira. Koma anapuma pa tsiku la Sabata pomvera malamulo.

< Luc 23 >