< I Samuel 3 >

1 Nagserbi ti ubing a ni Samuel kenni Yahweh babaen iti panangidalan ni Eli. Manmano ti sao ni Yahweh kadagidiay nga al-aldaw; awan unay ti sirmata maipanggep iti masakbayan.
Samueli ankatumikira Yehova moyangʼaniridwa ndi Eli. Masiku amenewo mawu a Yehova sankamveka pafupipafupi. Kuona zinthu mʼmasomphenya sikunkachitikanso kawirikawiri.
2 Iti dayta a tiempo, idi ni Eli nga agkapsuten ti panagkitana a saan unayen a makakita, ket agid-idda iti bukodna a pagiddaan,
Tsiku lina Eli, amene maso anali ofowoka ndi kuti sankatha kuona bwino, anagona pa malo ake.
3 Saan pay idi a naiddep ti pagsilawan ti Dios, ket ni Samuel, matmaturog iti balay ni Yahweh nga ayan ti lakasa ti tulag ti Dios.
Nthawiyi nʼkuti nyale ya Mulungu isanazimitsidwe. Samueli anali gone mu Nyumba ya Yehova, kumene kunali Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
4 Inawagan ni Yahweh ni Samuel, a nagkuna, “Adtoyak.”
Yehova anayitana Samueli. Iye anayankha kuti, “Wawa.”
5 Timmaray ni Samuel iti ayan ni Eli, ket kinunana, “Immayak ta inayabannak.” Kinuna ni Eli, “Saanka nga inayaban; agsublika iti pagiddaam.” Isu a napan nagidda ni Samuel.
Ndipo iyeyo anathamangira kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera ndamva kuyitana.” Koma Eli anati, “Ine sindinakuyitane, bwerera kagone.” Ndipo iye anapita kukagona.
6 Immawag manen ni Yahweh, “Samuel.” Bimmangon manen ni Samuel ket napan kenni Eli ket kinunana, “Inayabannak isu nga adtoyak.” Simmungbat ni Eli, “Saanka nga inayaban, anakko; inka pay agidda.”
Yehova anayitananso, “Samueli!” Ndipo Samueli anadzuka ndi kupita kwa Eli nati, “Ndabwera popeza ndamva mukundiyitana.” Eli nati, “Mwana wanga, ine sindinakuyitane, bwerera kagone.”
7 Ita, awan pay ti kapadasan ni Samuel kenni Yahweh, wenno awan pay pulos ti aniaman a mensahe a naipakita kenkuana manipud kenni Yahweh.
Nthawiyi nʼkuti Samueli asanadziwe Yehova ndipo Mawu a Yehova nʼkuti asanawululidwe kwa iye.
8 Inawagan manen ni Yahweh ni Samuel iti maikatlo a gundaway. Bimmangon manen ni Samuel ket napan kenni Eli ket kinunana, “Immayak ta inayabannak.” Ket naamiris ni Eli nga inawagan ni Yahweh ti ubing.
Yehova anayitananso Samueli kachitatu ndipo Samueli anadzuka ndikupita kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera popeza mwandiyitana ndithu.” Apo Eli anazindikira kuti Yehova ndiye ankayitana mnyamatayo.
9 Ket kinuna ni Eli kenni Samuel, “Mapanka agidda manen; no awagannaka manen, nasken nga ibagam, 'Agsaoka, O Yahweh, ta dumdumngeg ti adipenmo.”' Isu a napan nagidda manen ni Samuel iti pagid-iddaanna.
Tsono Eli anamuwuza Samueli kuti, “Pita ukagone ndipo akakuyitananso ukanene kuti, ‘Yankhulani Yehova, pakuti mtumiki wanu ndikumvetsera.’” Choncho Samueli anapita ndi kukagona pamalo pake.
10 Immay ni Yahweh ket nagtakder; immawag a kas iti immuna, “Samuel, Samuel.” Ket kinuna ni Samuel, “Agsaoka, ta dumdumngeg ti adipenmo.”
Yehova anabwera ndi kuyima pomwepo, ndi kuyitana monga nthawi zina zija, “Samueli! Samueli!” Ndipo Samueli anayankha, “Yankhulani, pakuti mtumiki wanu akumvetsera.”
11 Kinuna ni Yahweh kenni Samuel, “Dumngegka, umadanin nga aramidek iti Israel ti banag nga uray la agkintayeg dagiti lapayag ti amin a makangngeg iti daytoy.
Ndipo Yehova anati kwa Samueli, “Taona, patsala pangʼono kuti ndichite chinthu china mu Israeli chimene chidzadabwitsa aliyense amene adzamve.
12 Iti dayta nga aldaw, ipatungpalkonto kenni Eli dagiti amin nga imbagak maipanggep iti balayna, manipud iti rugi agingga iti pagpatinggaan.
Tsiku limenelo ndidzachitadi zonse zimene ndinayankhula zokhudza banja la Eli kuyambira poyamba mpaka pomaliza.
13 Imbagak kenkuana a dandanin nga ukomek a mammaminsan ti balayna gapu iti amin a basol nga ammona, gapu ta nangiyeg iti lunod dagiti annakna kadagiti bagbagida ket saanna ida nga inatipa.
Pakuti ndinamudziwitsa kuti Ine ndikhoza kulanga banja lake kwamuyaya chifukwa cha zoyipa zimene ana ake ankadziyipitsa nazo. Iye ankadziwa zimenezi koma osawaletsa.
14 Gapu iti daytoy, insapatak iti balay ni Eli a saanto pulos a mapakawan dagiti basol ti balayna babaen iti daton wenno sagut.”
Nʼchifukwa chake ndinalumbira kuti, ‘Zoyipa zimene banja la Eli linandichita sizidzafafanizidwa mpaka muyaya ngakhale adzapereke nsembe kapena zopereka zina.’”
15 Nagidda ni Samuel agingga iti bigat; kalpasanna, linukatanna dagiti ruangan ti balay ni Yahweh. Ngem mabuteng ni Samuel a mangibaga kenni Eli iti maipanggep iti sirmata.
Samueli anagona mpaka mmawa. Atadzuka anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova. Iye anachita mantha kumuwuza Eli za masomphenya ake.
16 Ket inayaban ni Eli ni Samuel a kunana, “Samuel, anakko.” Kinuna ni Samuel, “Adtoyak.”
Koma Eli anamuyitana nati, “Samueli mwana wanga.” Samueli anayankha kuti, “Wawa.”
17 Kinuna ni Eli, “Ania ti imbagana kenka? Saanmo koma nga ilimed kaniak. Dusaennaka ti Dios, ken ad-adda pay koma no ilimedmo kaniak ti aniaman nga imbagana kenka.”
Tsono Eli anafunsa kuti, “Yehova wakuwuza chiyani? Usandibisire. Mulungu akulange ndithu ngati undibisira chilichonse cha zimene wakuwuza.”
18 Imbaga amin ni Samuel kenkuana; awan ti inlimedna kenkuana. Kinuna ni Eli, “Ni Yahweh daytoy. Aramidenna koma ti kasayaatan a maaramid.”
Choncho Samueli anamuwuza zonse, sanamubisire kalikonse. Ndipo Eli anati, “Iye ndi Yehova, mulekeni achite chimene chamukomera.”
19 Dimmakkel ni Samuel, ket adda kenkuana ni Yahweh ket awan ti pimmalso kadagiti padtona.
Yehova anali ndi Samueli pamene amakula, ndipo zonse zimene ankayankhula zinkachitikadi.
20 Ammo ti entero nga Israel manipud Dan agingga iti Beerseba a nadutokan ni Samuel nga agbalin a profeta ni Yahweh.
Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dera la Dani mpaka ku Beeriseba anazindikira kuti Yehova analozadi chala pa Samueli kuti akhale mneneri wake.
21 Nagparang manen ni Yahweh idiay Silo, ta nagparang isuna a mismo kenni Samuel idiay Silo babaen iti saona.
Yehova anapitiriza kuoneka ku Silo, ndipo kumeneko anadziwulula yekha kwa Samueli mwa mawu ake.

< I Samuel 3 >