< Un-unnoy 2 >

1 Naan-anay nga inabbongan ti Apo iti napuskol nga ulep ti anak a babai ti Sion gapu iti ungetna! Manipud langit agingga iti daga, intinnagna ti kinapintas ti Israel; saanna nga inkankano ti pagbatayan ti sakana iti aldaw ti ungetna.
Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni ndi mtambo wa mkwiyo wake! Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli kuchoka kumwamba. Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso popondapo mapazi ake.
2 Inalun-on ti Apo ken saan isuna a naasian kadagiti amin nga ili ni Jacob. Rinebbana dagiti nasarikedkedan a siudad ti anak a babai ti Juda gapu iti pungtotna; impababana ida iti daga ken imbabainna ti pagarian ken dagiti prinsipena.
Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo; mu mkwiyo wake anagwetsa malinga a mwana wamkazi wa Yuda. Anagwetsa pansi mochititsa manyazi maufumu ndi akalonga ake.
3 Pinutedna amin a bileg ti Israel babaen iti nakaro a pungtotna. Inawidna ti makannawan nga imana manipud iti sangoanan dagiti kabusor. Inuramna ni Jacob a kasla maysa a gumilgil-ayab nga apuy a mangikiskisap iti amin a banag nga adda iti aglawlawna.
Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola nyanga iliyonse ya Israeli. Anabweza dzanja lake lamanja pamene mdani anamuyandikira. Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.
4 Imbiatna ti baina kadakami a kasla maysa a kabusorna. Timmakder isuna a makigubat a kas maysa a kasupiat a nakasagana a mangdangran kadakami. Pinatayna dagiti amin a kapapatgan unay a tattao iti panagkitana. Iti uneg ti tolda ti anak a babai ti Sion, imbukbokna ti pungtotna a kasla apuy.
Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani; wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani, ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira. Ukali wake ukuyaka ngati moto pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.
5 Nagbalin ti Apo a kasla maysa a kabusor. Inalun-onna ti Israel. Inalun-onna dagiti amin a palasiona; dinadaelna dagiti sarikedked ti Israel. Pinakarona ti panagdungdung-aw ken panagun-unnoy iti anak a babai ti Juda.
Ambuye ali ngati mdani; wawonongeratu Israeli; wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu ndipo wawononga malinga ake. Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira kwa mwana wamkazi wa Yuda.
6 Rinautna ti tabernakulona a kasla maysa nga abung-abung ti minuyongan. Dinadaelna ti lugar a napasnek a paggigimongan. Inaramid ni Yahweh a malipatan ti napasnek a panaggigimong ken aldaw a Panaginana idiay Sion, ta linalaisna ti ari ken ti padi gapu iti ungetna.
Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda; wawononga malo ake a msonkhano. Yehova wayiwalitsa Ziyoni maphwando ake oyikika ndi masabata ake. Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza mfumu ndi wansembe.
7 Linaksid ti Apo ti altarna; ginurana ti santuariona. Inyawatna iti ima ti kabusor dagiti pader ti palasiona. Nagariwawada a sibaballigi iti balay ni Yahweh, a kas iti aldaw ti napasnek a panaggigimong.
Ambuye wakana guwa lake la nsembe ndipo wasiya malo ake opatulika. Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu kwa mdani wake; adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.
8 Sitatanang nga inkeddeng ni Yahweh a dadaelenna ti pader ti siudad ti anak a babai Sion. Imbinnatna ti pangrukod ket saanna nga imbabawi ti imana a mangdaddadael iti pader. Ken pinagdung-awna dagiti bakud ken pinarukopna dagiti pader.
Yehova anatsimikiza kugwetsa makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni. Anawayesa ndi chingwe ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa. Analiritsa malinga ndi makoma; onse anawonongeka pamodzi.
9 Limned iti daga dagiti ruanganna; tinukkolna dagiti balunet ti ruanganna. Ti ari ken dagiti prinsipena ket agtaud kadagiti Hentil, nga awanan iti linteg ni Moises. Uray dagiti profetana ket awan masarakanda a sirmata manipud kenni Yahweh.
Zipata za Yerusalemu zalowa pansi; wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake. Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, palibenso lamulo, ndipo aneneri ake sakupeza masomphenya kuchokera kwa Yehova.
10 Agtugtugaw iti daga ken siuulimek nga agladladingit dagiti panglakayen iti anak a babai ti Sion. Nangiwarakiwakda iti tapuk kadagiti uloda; nagkawesda iti nakirsang a lupot. Indumog dagiti birhen ti Jerusalem dagiti uloda iti daga.
Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni akhala chete pansi; awaza fumbi pa mitu yawo ndipo avala ziguduli. Anamwali a Yerusalemu aweramitsa mitu yawo pansi.
11 Naibusen ti luak; nalabagan dagiti matak; marirriribukan ti pusok. Agladladingit ti entero a kaunggak gapu iti pannakarumek iti anak a babai dagiti tattaok, gapu ta agkakapsut dagiti ubbing a babassit ken dagiti agsussuso a maladaga kadagiti kalsada dagiti bario.
Maso anga atopa ndi kulira, ndazunzika mʼmoyo mwanga, mtima wanga wadzaza ndi chisoni chifukwa anthu anga akuwonongeka, chifukwa ana ndi makanda akukomoka mʼmisewu ya mu mzinda.
12 Kunaenda kadagiti innada, “Sadino ti ayan ti bukbukel ken arak?” mataltalimudaw a kasla nadangran a tattao kadagiti kalsada ti siudad, nga in-inutda a matay iti sidong dagiti innada.
Anawo akufunsa amayi awo kuti, “Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?” pamene akukomoka ngati anthu olasidwa mʼmisewu ya mʼmizinda, pamene miyoyo yawo ikufowoka mʼmanja mwa amayi awo.
13 Ania ti makunak kenka anak a babai ti Jerusalem? Ania ti pangiyaspingak kenka tapno maliwliwaka, birhen nga anak a babai ti Sion? Ti pannakatalimudawmo ket nakabutbuteng a kas iti kadakkel ti baybay. Siasino ti makapaimbag kenka?
Ndinganene chiyani za iwe? Ndingakufanizire ndi chiyani, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu? Kodi ndingakufanizire ndi yani kuti ndikutonthoze, iwe namwali wa Ziyoni? Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja, kodi ndani angakuchiritse?
14 Nakakita dagiti profetam kadagiti makaallilaw ken minamaag a sirmata a para kenka. Saanda nga impakaammo ti basolmo tapno maisubli ti gasatmo, ngem nakakitada kadagiti makaallilaw a mammadles ken sulisog a para kenka.
Masomphenya a aneneri ako anali abodza ndi achabechabe. Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo poyika poyera mphulupulu zako. Mauthenga amene anakupatsa anali achabechabe ndi osocheretsa.
15 Palakpakandaka dagiti amin a lumabas kadagiti daldalan. Agsakuntip ken iwingiwingda dagiti uloda iti anak a babai ti Jerusalem ket kunaenda, “Daytoy kadi ti siudad nga aw-awaganda iti 'Kinapintas nga Awan Pagkuranganna,' 'Ti Rag-o ti Amin a Daga?'”
Onse oyenda mʼnjira yako akukuwombera mʼmanja; akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu: “Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa wokongola kotheratu, chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”
16 Inganga dagiti amin a kabusormo dagiti ngiwatda ket laisendaka. Agsagawisiw ken pagngaretngetenda dagiti ngipenda; kunaenda, “Inalun-onmi isuna! Awan duadua a daytoy ti aldaw nga inur-uraymi! Nasarakanmin! Nakitamin!”
Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza; iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo, ndipo akuti, “Tamumeza. Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera; tili ndi moyo kuti tilione.”
17 Inaramid ni Yahweh ti inkeddengna. Tinungpalna ti saona nga impakaammona iti nabayagen a tiempo. Rinebbana; saan isuna a naasian, ta intulokna nga agrag-o ti kabusor gapu kenka; pinapigsana dagiti kabusormo.
Yehova wachita chimene anakonzeratu; wakwaniritsa mawu ake, amene anatsimikiza kale lomwe. Wakuwononga mopanda chifundo, walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako, wakweza mphamvu za adani ako.
18 Ipukpukkaw dagiti pusoda iti Apo, “Padpader iti anak a babai ti Sion, pagayusenyo dagiti lua a kasla karayan iti aldaw ken rabii. Saanka nga agin-inana. Saanmo nga isardeng ti panagayusna kadagiti matam.
Mitima ya anthu ikufuwulira Ambuye. Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni, misozi yako itsike ngati mtsinje usana ndi usiku; usadzipatse wekha mpumulo, maso ako asaleke kukhetsa misozi.
19 Agtakder ken agpukkawka iti rabii; manipud iti rugi ti panagbabantay, ibukbokmo ti pusom a kasla danum iti sangoanan ti Apo. Itag-aymo kenkuana dagiti imam nga agpaay iti biag dagiti annakmo nga agkakapuy a nakaidda a mabisbisinan iti nagsasabatan ti tunggal kalsada.”
Dzuka, fuwula usiku, pamene alonda ayamba kulondera; khuthula mtima wako ngati madzi pamaso pa Ambuye. Kweza manja ako kwa Iye chifukwa cha miyoyo ya ana ako, amene akukomoka ndi njala mʼmisewu yonse ya mu mzinda.
20 Kumitaka, O Yahweh, ket panunotem koma dagidiay nangaramidam iti kastoy. Rumbeng kadi a kanen dagiti babbai ti bukodda a bunga, dagiti annak nga ay-aywananda? Rumbeng kadi a mapapatay dagiti padi ken profeta iti santuario ti Apo?
Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani: kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi? Kodi amayi adye ana awo, amene amawasamalira? Kodi ansembe ndi aneneri awaphere mʼmalo opatulika a Ambuye?
21 Naiwalang iti daga kadagiti kalsada dagiti ubbing ken lallakay. Napasag dagiti birhenko ken dagiti tattaok a mamaingel babaen iti kampilan. Pinapataymo ida iti aldaw ti pungtotmo; naulpit ti panangpapataymo ken saanka a naasian kadakuada.
Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda; anyamata anga ndi anamwali anga aphedwa ndi lupanga. Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu; mwawapha mopanda chifundo.
22 Inayabam dagiti pagbutbutngak manipud iti amin nga aglawlaw a kas iti aldaw ti napasnek a panaggigimong; awan ti nakalibas, ken awan ti nakalasat iti aldaw ti pungtot ni Yahweh. Dagiti inay-aywanak ken pinadakkelko, pinapatay ti kabusorko.
Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando, chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse. Pa tsiku limene Yehova wakwiya palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo; mdani wanga wawononga onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.

< Un-unnoy 2 >