< Dagiti Salmo 47 >

1 Dakayo amin a tattao, ipalakpakyo dagiti imayo; ipukkawyo iti Dios ti timek ti balligi.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
2 Ta ni Yahweh a Kangangatoan ket nakaam-mak; naindaklan isuna nga Ari iti entero a daga.
Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
3 Parukmaenna dagiti tattao iti babaentayo ken dagiti nasion iti sirok ti sakatayo.
Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
4 Pinilina ti tawidentayo, ti dayaw ni Jacob nga inayatna. (Selah)
Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
5 Nagpangato ti Dios a nabuyogan iti pukkaw, nagpangato ni Yahweh a napakuyogan iti uni ti trumpeta.
Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
6 Agkantatayo kadagiti pammadayaw para iti Dios, kantaentayo dagiti pammadayaw, kantaentayo dagiti pammadayaw para iti Aritayo. Kantaentayo dagiti pammadayaw.
Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
7 Ta ti Dios ti Ari iti entero a daga; kantaentayo dagiti pammadayaw nga addaan pannakaawat.
Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
8 Agari ti Dios kadagiti nasion; agtugtugaw iti nasantoan a tronona.
Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
9 Dagiti prinsipe iti amin a tattao ket naummongda a kadua dagiti tattao ti Dios ni Abraham; ta ti salaknib ti lubong ket kukua ti Dios; maitan-ok isuna iti kasta unay.
Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.

< Dagiti Salmo 47 >