< Luka 2 >

1 Matungo na mahiku nanso ukaisari Agusto au pumilye Ilago akaila holi ua ligwa waantu Ihi ni Ikie mihiyi.
Mʼmasiku amenewo Kaisara Augusto anapereka lamulo kuti kalembera achitike mʼdziko lonse la Aroma.
2 Ili aialyo lagwandiyo alitumilye matungo krenio amukulu wang'wa siria.
(Uyu ndi kalembera woyamba amene anachitika pamene Kureniyo anali bwanamkubwa wa Siriya).
3 Kila muntu akalongola kukisali kao. Kenda kuhola ialo.
Ndipo aliyense anapita ku mzinda wa kwawo kukalembetsa.
4 Nung'wenso uyusufu akahega mukisali ka Nazareti ku Galilay nu kulongola ku Yudea mukisali ka Bethlehemu. nu manyikile anga kisali kang'wa Daudi. kunsoko au pumie muileli wang'wa Daudi.
Choncho Yosefe anachoka ku Nazareti ku Galileya kupita ku Yudeya, ku Betelehemu ku mudzi wa Davide, chifukwa anali wa banja ndi fuko la Davide.
5 Au ulongae kung'wanso kenda kuhola ialo palung'wi nu Mariamu amuligilye nukumulindilya ung'wana.
Iye anapita kumeneko kukalembetsa pamodzi ndi Mariya, amene anapalana naye ubwenzi kuti akwatirane ndipo anali woyembekezera.
6 Naiakole kung'wanso imatungo nanso aialindie ung'wana alelywe.
Ali kumeneko, nthawi inakwana yakuti mwana abadwe,
7 Akaleta ng'wana mugoha. Uleli wakwe wang'wandyo akamuimba inguo muili wihi kugilya impepo ung'wana. Akamuika muntua nakuliselya imitugo kunsoko aikutile ilyoma munyumba ya kila nzila.
ndipo anabereka mwana wake woyamba, wamwamuna. Iye anamukulunga mʼnsalu ndi kumuyika modyera ngʼombe, chifukwa kunalibe malo mʼnyumba ya alendo.
8 Ihi ni anso aiakole iadimi naikie mumbuga akazelindila ikolo yao utiku.
Ndipo kunali abusa amene amakhala ku dera lomwelo, kuyangʼanira ziweto zawo usiku.
9 Itungo malaika wa mukulu akapumila utemi wa mukulu ukelya nukupilimilya akatula nu oa.
Mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iwo ndipo ulemerero wa Ambuye unawala mowazungulira. Iwo anachita mantha.
10 Kululo umalaika akaaila, ''leki kogopi numuletee lukani luza, nulukuleta ilumbi ku antu ihi.
Koma mngeloyo anawawuza kuti, “Musachite mantha. Ine ndakubweretserani Uthenga Wabwino wachimwemwe chachikulu umene udzakhala wa anthu onse.
11 Iie liyi, muguni uleilwe kunsoko anyu, mukisale kang'wa Daudi nuanso yuyo kristo mkulu!
Lero mʼmudzi wa Davide wakubwadwirani Mpulumutsi; Iye ndi Khristu Ambuye.
12 Ike inge kilingasilyo mkupegwa, mukumu hanga ung'wana utungilye nguo uloe muntua akulisilya imetungo.
Ichi chidzakhala chizindikiro kwa inu: mukapeza mwana wakhanda wokutidwa ndi nsalu atagona modyera ngʼombe.”
13 Itungo itumi akilunde ikaza idu ikatula palung'wi ikamusongelya Itunda, Ikalunga.
Mwadzidzidzi gulu lalikulu la angelo linaonekera pamodzi ndi mngeloyo, kuyamika Mulungu ndi kumati,
14 Ukulu wang'wi itunda mua migulya nu upolowa mihi nualoilye.
“Ulemerero kwa Mulungu mmwambamwamba, ndi mtendere kwa anthu pa dziko lapansi amene Iye akondwera nawo.”
15 Kuite inge ia malaika ai atuile kulongola kenda kilunde, iadimi akitambuile enso kua enso, Inge kweni ku Bethelehemu, kende kuone iku nikigee nu mukulu ukulagie.
Angelowo atabwerera kumwamba, abusawo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni ku Betelehemu tikaone zinthu zomwe zachitika, zimene Ambuye atiwuza ife.”
16 Akakaya kung'wanso, akamuhanga mariamu nu Yusufu, ikamuona ug'wana ulae muntua nikilyesilya imetugo.
Ndipo iwo anafulumira nyamuka nakapeza Mariya ndi Yosefe ndi mwana wakhanda, amene anagona modyera ngʼombe.
17 Na iane uu akaaila iantu naiaiwe aya na ng'wana.
Pamene anamuona Iye, iwo anafotokoza zomwe anawuzidwa za mwanayo,
18 Ihi naigule alukani ulu ikakuilwa iko na ikitambuwe nu mudimi.
ndipo onse amene anamva zimene abusawa ananena anadabwa.
19 Inge u mariamu akalongoleka, kusega kunsoko ihi nae wigule, akamaika munkola akwe.
Koma Mariya anasunga zonsezi mu mtima mwake ndi kumazilingalira.
20 I a dime ikasuka ikamukulya nukumulumbelya Itunda kitu naeigule nukuona, anga nae itambuwe, kung'wanso.
Abusa anabwerera, akulemekeza ndi kuyamika Mulungu chifukwa cha zonse anazimva ndi kuziona, zomwe zinali monga anawuzidwira ndi angelo aja.
21 Naelipikile ulu hiku la munana ikatula matungo, akumutala kukedamu ung'wana, ikamitanga elina lakwe Yesu, elina naupewe nu malaika Inda naikilengila munda.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, tsiku loti amuchite mdulidwe anamutcha Yesu, dzina limene mngelo anamupatsa asanabadwe.
22 Naelipikile imahiku akuzepilingwa kitalao anga nai uzepeigwe malagelyo ang'wa musa, Yusuma na Mariamu akamutala mitekelo ku yerusalemu kumuika kuntongela ing'wi Tunda.
Nthawi yoyeretsedwa kwawo itatha, monga mwa lamulo la Mose, Yosefe ndi Mariya anapita naye ku Yerusalemu kukamupereka kwa Ambuye.
23 Anga naeiandekilye mumalago ang'wi Tunda, kila mugoha nulugue Inda ukitangwa naupumigwe wakfu wang'wi Tunda.
(Monga mmene zinalembedwera mu lamulo la Ambuye kuti, “Muzikapereka kwa Ambuye mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa”),
24 Ne anso aiazile kupumwa isongelyo anga naelitambuwe milago la ng'wi Tunda.
ndi kupereka nsembe posunga zimene zinanenedwa mulamulo la Ambuye: “Njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri.”
25 Goza aukoli muntu ku yerusalemu zilina lakwe aukitangwa Simeoni. Umuntu nuanso aewatai nukumukulya Itunda. nuanso aizulindie muaili wa Israeli, nu ng'wang'welu aiukole migulya lakwe.
Ndipo taonani, mu Yerusalemu munali munthu wotchedwa Simeoni, amene anali wolungama ndi wodzipereka. Iye ankadikira chitonthozo cha Israeli, ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.
26 Aituile kuhila kukiela kung'wa ng'welu kuiti nuanso sanga auzesha iza kuli kumuona U - kristo wang'wi itunda.
Mzimu Woyera anamuwululira kuti sadzafa asanaone Khristu wa Ambuye.
27 Luhuki lung'wi auzile mukate mitekeelo akazutongewe nung'wang'welu, Ateli ai amuletile ung'wana, yesu, kumtendela anga ilago.
Motsogozedwa ndi Mzimu Woyera, iye anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Makolo ake a Yesu atabwera naye kuti achite naye mwambo malingana ndi malamulo,
28 Simeoni akamsingilya mumikono akwe, kumukulya Itunda akalunga.
Simeoni anamunyamula mʼmanja mwake nayamika Mulungu, nati:
29 Mulekele umitumi wako alongote kuhuili wa mukulu, kutula nulukani lako.
“Ambuye waulamuliro, monga munalonjeza, tsopano lolani kuti mtumiki wanu apite mu mtendere.
30 Kunsoko imiho ane auona uza wako.
Pakuti maso anga aona chipulumutso chanu,
31 Nuingee kumiho aantu ihi.
chimene Inu munakonza pamaso pa anthu onse,
32 Nuanso ng'welu kunsoko akukunukulya ukumbigulu nu ukulu wa antu Israeli.
kuwala kowunikira anthu a mitundu ina ndi kwa ulemerero kwa anthu anu Aisraeli.”
33 Ihe nu nyinga nia ng'wana ai akuiwe Inkani nai itambuwe kunsoko akwe.
Abambo ndi amayi a Mwanayo anadabwa chifukwa cha zimene zinanenedwa za Iye.
34 Smeoni akasongelya akalunga Mariamu, akwe ntegeelye kisa ung'wana uyu ite ukutula kunsoko kulimila kuguna iantu Idu ku Israeli inge kulingasilyo ku antu idu nia kuhita.
Kenaka Simeoni anawadalitsa ndipo anati kwa Mariya amayi ake: “Mwana uyu wakonzedwa kukhala kugwa ndi kudzuka kwa ambiri mu Israeli, ndi kukhala chizindikiro chimene adzayankhula motsutsana nacho,
35 Ingi upanga ukusonsa ikolo ako ue, maswgo amukolo igelekee!
kotero kuti malingaliro a mitima ya ambiri adzawululidwa. Ndipo lupanga lidzabaya moyo wakonso.”
36 Munyakidagu musungu nai witangwa Ana hangi au koli mitekelo, nuanso ai munanso wang'wa Fanueli kupuma ulelwa wa ng'wa asheli, Aukite mahiku idu, nung'wenso ai ikie nu mugoha myaka mapungate nai ihoile.
Panalinso mneneri wamkazi, dzina lake Ana, mwana wa Fanuelo, wa fuko la Aseri. Anali wokalamba kwambiri; anakhala ndi mwamuna wake zaka zisanu ndi ziwiri atakwatiwa,
37 Akatula muhimbe kumanyaka munana na unne Nuanso shanga aiwihega mitekelo akendelea kumukulya Itunda palung'wi nukupunga nukulopa, utiko nu mung'wi.
ndipo kenaka anakhala wamasiye mpaka pamene anali ndi zaka 84. Iye sanachoke mʼNyumba ya Mulungu koma ankapembedza usiku ndi usana, kusala kudya ndi kupemphera.
38 Matungo nanso akaza pang'wanso na iakoli akamusongelya Itunda akaligitya kunsoko ang'wa na kumuntu na mulindie ku Yerusalemu.
Pa nthawiyo pamene ankapita kwa iwo, iye anayamika Mulungu ndi kuyankhula za Mwanayo kwa onse amene ankayembekezera chipulumutso cha Yerusalemu.
39 Naiamalile kila ekintu naealoilye kituma ilango la mukulu ikasuka ku Galilaya, kukesali, kao, Nazareti.
Yosefe ndi Mariya atachita zonse zimene zinkafunikira ndi lamulo la Ambuye, anabwerera ku Galileya ku mudzi wa Nazareti.
40 Ung'wana akakula akatula ukete inguru akaongeleka mulikalo, Uza wang'witunda ukatula mingulya.
Ndipo Mwanayo anakula nakhala wamphamvu; Iye anadzazidwa ndi nzeru, ndipo chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.
41 Ialeli akwe kila ung'waka enda ku Yerusalemu kunsoko amilundo wa Pasaka.
Chaka chilichonse makolo ake ankapita ku Yerusalemu ku phwando la Paska.
42 Nautuele myaka ikumi na ibili akalongoka hange naeipipile miko kunsoko amilundo.
Iye ali ndi zaka khumi ndi ziwiri, anapita ku phwando, monga mwa mwambo.
43 Naisigile matungo ehi kunsoko amilundo ikanza kusuka kito. Inge Umuhumba u-Yesu auasiga kunyuma mumo mu-Yerusalemu ialeli akwe shanga ikalinga ili.
Phwando litatha, pamene makolo ake ankabwerera kwawo, mnyamata Yesu anatsalira ku Yerusalemu, koma iwo sanadziwe zimenezi.
44 Aialiye ukoi palung'wi neinso naiakugenda aiagendile luhiku. Kululo akanza kumuduma Mwanya ndugu ao.
Poganiza kuti anali nawo mʼgulu lawo, anayenda tsiku limodzi. Kenaka anayamba kumufunafuna pakati pa abale awo ndi anzawo.
45 Naialemilye kumulija akasuka ku-Yerusalemu ikatula kumuduma kuko.
Atalephera kumupeza, anabwerera ku Yerusalemu kukamufuna.
46 Ikatula mahiku atatu ikamuhanga mutekelo akazimikie pakate pamanyisigwa akizu ategeye nuku akolya inkani.
Patatha masiku atatu anamupeza ali mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, atakhala pakati pa aphunzitsi, akumvetsera ndi kuwafunsa mafunso.
47 Ihi naiamigule akakuilwa umanyi wakwe nu usukeli.
Aliyense amene anamumva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake ndi mayankho ake.
48 Nai amuine Ikakuilwa unyinya akamuila ng'waane, neke nukutenda nanso? Utata ako nu nene aikekuduma kuoa nuukulu.
Makolo ake atamuona, anadabwa. Amayi ake anati kwa Iye, “Mwanawe, watichitira zimenezi chifukwa chiyani? Abambo ako ndi ine takhala tili ndi nkhawa kukufunafuna Iwe.”
49 Kunene, ''naimukunduma? sanga aimulingile kina kutula koli munyumba ang'wa tata ane?
Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumandifunafuna? Kodi simukudziwa kuti ndikuyenera kukhala mʼnyumba ya Atate anga?”
50 Singa alinga azu kuligitya nkanike izi.
Koma iwo sanazindikire chomwe Iye amatanthauza.
51 Sunga akalongala palung'wi ku nazareti kitalao hangi au gombile kitalao, Unyinya auikile inkani yihi munkolo akwe.
Kenaka anapita nawo ku Nazareti ndipo anawamvera iwo. Koma amayi ake anasunga zinthu zonsezi mu mtima mwawo.
52 Sunga u Yesu akalongeleka kukula kimahala ni kimwili, niantu ang'wi Tunda ikamulowa.
Ndipo Yesu anakula mu nzeru, msinkhu ndi chisomo cha Mulungu ndi anthu.

< Luka 2 >