< Salmi 22 >

1 Salmo di Davide, [dato] al Capo de' Musici, sopra Aielet-hassahar DIO mio, Dio mio, perchè mi hai lasciato? [Perchè stai] lontano dalla mia salute, [e dalle] parole del mio ruggire?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
2 O Dio mio, io grido di giorno, e tu non rispondi; Di notte ancora, e non ho posa alcuna.
Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
3 E pur tu [sei] il Santo, Il Permanente, le lodi d'Israele.
Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
4 I nostri padri si son confidati in te; Si son confidati [in te], e tu li hai liberati.
Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
5 Gridarono a te, e furon liberati; In te si confidarono, e non furon confusi.
Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
6 Ma io [sono] un verme, e non un uomo; Il vituperio degli uomini, e lo sprezzato fra il popolo.
Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
7 Chiunque mi vede, si beffa di me, [Mi] stende il labbro, [e] scuote il capo;
Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
8 [Dicendo: ] Egli si rimette nel Signore; liberilo dunque; Riscuotalo, poichè egli lo gradisce.
“Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
9 Certo, tu [sei quel] che mi hai tratto fuor del seno; Tu mi hai affidato [da che io era] alle mammelle di mia madre.
Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
10 Io fui gettato sopra te dalla matrice; Tu [sei] il mio Dio fin dal seno di mia madre.
Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
11 Non allontanarti da me; perciocchè l'angoscia [è] vicina, E non [vi è] alcuno che [mi] aiuti.
Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
12 Grandi tori mi hanno circondato; Possenti tori di Basan mi hanno intorniato;
Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
13 Hanno aperta la lor gola contro a me, [Come] un leone rapace e ruggente.
Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
14 Io mi scolo come acqua, E tutte le mie ossa si scommettono; Il mio cuore è come cera, [E] si strugge nel mezzo delle mie interiora.
Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
15 Il mio vigore è asciutto come un testo, E la mia lingua è attaccata alla mia gola; Tu mi hai posto nella polvere della morte.
Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
16 Perciocchè cani mi hanno circondato; Uno stuolo di maligni mi ha intorniato; Essi mi hanno forate le mani ed i piedi.
Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
17 Io posso contar tutte le mie ossa; Essi mi riguardano, [e] mi considerano.
Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
18 Si spartiscono fra loro i miei vestimenti, E tranno la sorte sopra la mia vesta.
Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
19 Tu dunque, Signore, non allontanarti; [Tu che sei la] mia forza, affrettati a soccorrermi.
Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
20 Riscuoti l'anima mia dalla spada, L'unica mia dalla branca del cane.
Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
21 Salvami dalla gola del leone, Ed esaudiscimi, [liberandomi] dalle corna de' liocorni.
Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
22 Io racconterò il tuo Nome a' miei fratelli; Io ti loderò in mezzo della raunanza.
Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
23 [Voi] che temete il Signore, lodatelo; Glorificatelo [voi], tutta la progenie di Giacobbe; E [voi] tutta la generazione d'Israele, abbiate timor di lui.
Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
24 Perciocchè egli non ha sprezzata, nè disdegnata l'afflizione dell'afflitto; E non ha nascosta la sua faccia da lui; E quando ha gridato a lui, l'ha esaudito.
Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
25 Da te [io ho] l'argomento della mia lode in grande raunanza; Io adempirò i miei voti in presenza di quelli che ti temono.
Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
26 I mansueti mangeranno, e saranno saziati; Que' che cercano il Signore lo loderanno; Il vostro cuore viverà in perpetuo.
Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
27 Tutte le estremità della terra ne avranno memoria, E si convertiranno al Signore; E tutte le nazioni delle genti adoreranno nel suo cospetto.
Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
28 Perciocchè al Signore [appartiene] il regno; Ed [egli è quel] che signoreggia sopra le genti.
pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
29 Tutti i grassi della terra mangeranno ed adoreranno; [Parimente] tutti quelli che scendono nella polvere, E che non possono mantenersi in vita, s'inchineranno davanti a lui.
Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
30 La [lor] posterità gli servirà; Ella sarà annoverata per generazione al Signore.
Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
31 Essi verranno, ed annunzieranno la sua giustizia; [Ed] alla gente che ha da nascere ciò ch'egli avrà operato.
Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.

< Salmi 22 >