< Salmi 34 >

1 Di Davide, quando si finse insensato davanti ad Abimelec e, cacciato da lui, se ne andò. Io benedirò l’Eterno in ogni tempo; la sua lode sarà del continuo nella mia bocca.
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2 L’anima mia si glorierà nell’Eterno; gli umili l’udranno e si rallegreranno.
Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3 Magnificate meco l’Eterno, ed esaltiamo il suo nome tutti insieme.
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4 Io ho cercato l’Eterno, ed egli m’ha risposto e m’ha liberato da tutti i miei spaventi.
Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
5 Quelli che riguardano a lui sono illuminati, e le loro facce non sono svergognate.
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6 Quest’afflitto ha gridato, e l’Eterno l’ha esaudito e l’ha salvato da tutte le sue distrette.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7 L’Angelo dell’Eterno s’accampa intorno a quelli che lo temono, e li libera.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
8 Gustate e vedete quanto l’Eterno è buono! Beato l’uomo che confida in lui.
Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9 Temete l’Eterno, voi suoi santi, poiché nulla manca a quelli che lo temono.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 I leoncelli soffron penuria e fame, ma quelli che cercano l’Eterno non mancano d’alcun bene.
Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11 Venite, figliuoli, ascoltatemi; io v’insegnerò il timor dell’Eterno.
Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 Qual è l’uomo che prenda piacere nella vita, ed ami lunghezza di giorni per goder del bene?
Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 Guarda la tua lingua dal male a le tue labbra dal parlar con frode.
asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Dipartiti dal male e fa’ il bene; cerca la pace, e procacciala.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15 Gli occhi dell’Eterno sono sui giusti e le sue orecchie sono attente al loro grido.
Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 La faccia dell’Eterno è contro quelli che fanno il male per sterminare di sulla terra la loro memoria.
nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17 I giusti gridano e l’Eterno li esaudisce e li libera da tutte le loro distrette.
Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 L’Eterno e vicino a quelli che hanno il cuor rotto, e salva quelli che hanno lo spirito contrito.
Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19 Molte sono le afflizioni del giusto; ma l’Eterno lo libera da tutte.
Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 Egli preserva tutte le ossa di lui, non uno ne è rotto.
Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21 La malvagità farà perire il malvagio, e quelli che odiano il giusto saranno condannati.
Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 L’Eterno riscatta l’anima de’ suoi servitori, e nessun di quelli che confidano in lui sarà condannato.
Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.

< Salmi 34 >