< 詩篇 38 >

1 記念のためにうたったダビデの歌 主よ、あなたの憤りをもってわたしを責めず、激しい怒りをもってわたしを懲らさないでください。
Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
2 あなたの矢がわたしに突き刺さり、あなたの手がわたしの上にくだりました。
Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
3 あなたの怒りによって、わたしの肉には全きところなく、わたしの罪によって、わたしの骨には健やかなところはありません。
Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
4 わたしの不義はわたしの頭を越え、重荷のように重くて負うことができません。
Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
5 わたしの愚かによって、わたしの傷は悪臭を放ち、腐れただれました。
Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
6 わたしは折れかがんで、いたくうなだれ、ひねもす悲しんで歩くのです。
Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
7 わたしの腰はことごとく焼け、わたしの肉には全きところがありません。
Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
8 わたしは衰えはて、いたく打ちひしがれ、わたしの心の激しい騒ぎによってうめき叫びます。
Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
9 主よ、わたしのすべての願いはあなたに知られ、わたしの嘆きはあなたに隠れることはありません。
Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
10 わたしの胸は激しく打ち、わたしの力は衰え、わたしの目の光もまた、わたしを離れ去りました。
Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
11 わが友、わがともがらはわたしの災を見て離れて立ち、わが親族もまた遠く離れて立っています。
Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
12 わたしのいのちを求める者はわなを設け、わたしをそこなおうとする者は滅ぼすことを語り、ひねもす欺くことをはかるのです。
Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
13 しかしわたしは耳しいのように聞かず、おしのように口を開きません。
Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
14 まことに、わたしは聞かない人のごとく、議論を口にしない人のようです。
Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
15 しかし、主よ、わたしはあなたを待ち望みます。わが神、主よ、あなたこそわたしに答えられるのです。
Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
16 わたしは祈ります、「わが足のすべるとき、わたしにむかって高ぶる彼らにわたしのことによって喜ぶことをゆるさないでください」と。
Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
17 わたしは倒れるばかりになり、わたしの苦しみは常にわたしと共にあります。
Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
18 わたしは、みずから不義を言いあらわし、わが罪のために悲しみます。
Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
19 ゆえなく、わたしに敵する者は強く、偽ってわたしを憎む者は多いのです。
Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
20 悪をもって善に報いる者は、わたしがよい事に従うがゆえに、わがあだとなります。
Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
21 主よ、わたしを捨てないでください。わが神よ、わたしに遠ざからないでください。
Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
22 主、わが救よ、すみやかにわたしをお助けください。
Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.

< 詩篇 38 >