< UHezekheli 32 >

1 Kwasekusithi ngomnyaka wetshumi lambili, ngenyanga yetshumi lambili, ngolokuqala lwenyanga, ilizwi leNkosi lafika kimi lisithi:
Pa tsiku loyamba la mwezi wa khumi ndi chiwiri, chaka chakhumi ndi chiwiri, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Ndodana yomuntu, phakamisa isililo ngoFaro inkosi yeGibhithe, uthi kuye: Ufanana lebhongo lesilwane lezizwe, futhi wena ufanana lomgobho phakathi kwezinlwandle, waphutsha emifuleni yakho, wadunga amanzi ngenyawo zakho, wangcolisa imifula yazo.
“Iwe mwana wa munthu imba nyimbo ya maliro a Farao mfumu ya Igupto ndipo uyiwuze kuti, “Iwe umadziyesa ngati mkango pakati pa mitundu ya anthu. Koma iwe uli ngati ngʼona mʼnyanja. Umakhuvula mʼmitsinje yako, kuvundula madzi ndi mapazi ako ndi kudetsa madzi mʼmitsinje.
3 Itsho njalo iNkosi uJehova: Ngakho ngizakwendlala imbule lami phezu kwakho ngexuku labantu abanengi, bakukhuphule ngembule lami.
“Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Pogwiritsa ntchito gulu la anthu a mitundu yambiri, ndidzakuponyera khoka langa ndi kukugwira mu ukonde wanga.
4 Besengikutshiya emhlabathini, ngikujikijele egcekeni, ngenze zonke inyoni zamazulu zihlale phezu kwakho, ngisuthise izilo zawo wonke umhlaba ngawe.
Ndidzakuponya ku mtunda ndi kukutayira pansi. Ndidzabweretsa mbalame zamumlengalenga kuti zidzatere pa iwe, ndipo zirombo zonse za dziko lapansi zidzakudya.
5 Ngizabeka inyama yakho phezu kwezintaba, ngigcwalise izihotsha ngobude bakho.
Ndidzayanika mnofu wako pa mapiri ndipo zigwa zidzadzaza ndi zotsalira zako.
6 Ngizathelela ilizwe ngokuntshaza kwegazi lakho kuze kube sezintabeni; lezifula zizagcwala ngawe.
Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi ako, mpaka kumapiri komwe, ndipo mitsinje idzadzaza ndi mnofu wako.
7 Lalapho ngikucitsha ngizasibekela amazulu, ngenze inkanyezi zawo zibe mnyama; ngizasibekela ilanga ngeyezi, lenyanga kayiyikukhanyisa ngokukhanya kwayo.
Ndikadzakuwononga, ndidzaphimba miyamba ndikudetsa nyenyezi zake. Ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo, ndipo mwezi sudzawala.
8 Zonke izibane ezikhanyisayo emazulwini ngizazenza zibe mnyama phezu kwakho, ngibeke ubumnyama phezu kwelizwe lakho, itsho iNkosi uJehova.
Zowala zonse zamumlengalenga ndidzazizimitsa; ndidzachititsa mdima pa dziko lako, akutero Ambuye Yehova.
9 Njalo ngizakhathaza inhliziyo zabantu abanengi, nxa ngizaletha incithakalo yakho phakathi kwezizwe emazweni ongawaziyo.
Ndidzasautsa mitima ya anthu a mitundu yambiri pamene ndidzakupititsa ku ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, ku mayiko amene iwe sunawadziwe.
10 Yebo, ngizakwenza abantu abanengi bamangale kakhulu ngawe, lamakhosi abo azahlasimuka umzimba kakhulu ngawe, lapho ngiphazimisa inkemba yami phambi kwabo; njalo bazathuthumela isikhathi sonke, ngulowo lalowo ngempilo yakhe, ngosuku lokuwa kwakho.
Ine ndidzachititsa kuti anthu a mitundu yambiri adabwe nawe, ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha aakulu chifukwa cha iwe pamene ndidzaonetsa lupanga langa pamaso pawo. Pa nthawi ya kugwa kwako, aliyense wa iwo adzanjenjemera moyo wake wonse.
11 Ngoba itsho njalo iNkosi uJehova: Inkemba yenkosi yeBhabhiloni izakwehlela.
“‘Pakuti ndikunena Ine Ambuye Yehova kuti, “‘Lupanga la mfumu ya ku Babuloni lidzabwera kudzalimbana nawe.
12 Ngezinkemba zamaqhawe ngizakwenza ixuku lakho liwe, abesabekayo bezizwe, bonke; njalo azachitha ukuziphakamisa kweGibhithe, lexuku layo lonke lizabhujiswa.
Ndidzachititsa gulu lako lankhondo kuti ligwe ndi lupanga la anthu amphamvu, anthu ankhanza kwambiri pakati pa mitundu yonse ya anthu. Adzathetsa kunyada kwa Igupto, ndipo gulu lake lonse la nkhondo lidzagonjetsedwa.
13 Njalo ngizabhubhisa zonke izinyamazana zayo ngasemanzini amanengi; lonyawo lomuntu kalusayikuwadunga, lamasondo ezinyamazana kawayikuwadunga.
Ndidzawononga ziweto zake zonse zokhala mʼmbali mwa madzi ambiri. Ku madziko sikudzaonekanso phazi la munthu kapena kudetsedwa ndi phazi la ziweto.
14 Besengisenza amanzi abo atshone, ngenze imifula yabo igeleze njengamafutha, itsho iNkosi uJehova.
Pambuyo pake ndidzayeretsa madzi ake ndipo mitsinje yake idzayenda mokometsera ngati mafuta, akutero Ambuye Yehova.
15 Mhla ngizakwenza ilizwe leGibhithe libe yincithakalo, lelizwe liphundlwe ukugcwala kwalo, lapho ngitshaya bonke abahlala kilo, khona bazakwazi ukuthi ngiyiNkosi.
Ndikadzasandutsa dziko la Igupto kukhala bwinja; ndikadzawononga dziko lonse ndi kukantha onse okhala kumeneko, adzadziwa kuti ndine Yehova.’
16 Lesi yisililiselo abazasililisela; amadodakazi ezizwe azasililisela; bazasililisela, ngeGibhithe, langexuku layo lonke, itsho iNkosi uJehova.
“Mawu angawa adzakhala nyimbo ya maliro. Ana a akazi amitundu ya anthu adzayimba, kuyimbira Igupto ndi gulu lake lonse la nkhondo, akutero Ambuye Yehova.”
17 Kwasekusithi ngomnyaka wetshumi lambili, ngolwetshumi lanhlanu lwenyanga, ilizwi leNkosi lafika kimi lisithi:
Pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, chaka cha khumi ndi chiwiri, Yehova anayankhula kuti:
18 Ndodana yomuntu, khala ngenxa yexuku leGibhithe, ubehlisele, yona lamadodakazi ezizwe ezidumileyo, ezindaweni ezingaphansi zomhlaba, kanye labo abehlela emgodini.
“Iwe mwana wa munthu, lirira gulu lankhondo la Igupto ndipo uwalowetse pamodzi ndi anthu ena amphamvu a mayiko ena ku dziko la anthu akufa.
19 Wedlula bani ngokuthandeka? Yehla, ulaliswe labangasokanga.
Ufunse kuti, ‘Ndani amene akukuposa kukongola? Tsikirani ku manda ndi kukhala pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe.’
20 Bazawela phakathi kwababulewe ngenkemba. Inikelwe enkembeni; ihuduleni kanye lamaxuku ayo wonke.
Aigupto adzagwa pakati pa amene akuphedwa ndi lupanga. Lupanga ndi losololedwa kale. Iye adzaphedwa pamodzi ndi gulu lake lankhondo.
21 Abalamandla bamaqhawe bazakhuluma laye bephakathi kwesihogo, kanye labayisizayo; behlele phansi, balele abangasokanga, babulewe ngenkemba. (Sheol h7585)
Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’ (Sheol h7585)
22 IAsiriya ilapho lexuku layo lonke; amangcwaba ayo asenhlangothini zayo zonke, bonke bebulewe, bewile ngenkemba.
“Asiriya ali komweko ndipo ankhondo ake onse ali mʼmanda omuzungulira. Onsewo anaphedwa pa nkhondo.
23 Omangcwaba ayo enziwe emaceleni egodi, lexuku layo lihanqe ingcwaba layo, bonke bebulewe, bewile ngenkemba, ababenika isesabiso elizweni labaphilayo.
Manda awo ali kumalo ozama a dzenje, ndipo ankhondo ake azungulira manda ake. Onse amene anaopseza dziko la anthu amoyo aphedwa, agwa ndi lupanga.
24 Ikhona lapho iElamu lexuku layo lonke inhlangothi zonke zengcwaba layo, bonke bebulewe, abawileyo ngenkemba, abehle bengasokanga baya ezindaweni ezingaphansi zomhlaba, abanika isethuso sabo elizweni labaphilayo; kanti bethwele ihlazo labo kanye labo abehlela egodini.
“Elamu ali komweko ndipo ankhondo ake ali mʼmanda omuzungulira. Onsewa anaphedwa pa nkhondo, natsikira ku manda ali osachita mdulidwe. Iwowa kale ankaopseza anthu pa dziko lapansi. Tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda.
25 Bayenzele umbheda phakathi kwababuleweyo kanye lexuku layo lonke; amangcwaba ayo ayihanqile; bonke bengasokanga, bebulewe ngenkemba; ngoba isethuso sabo sanikelwa elizweni labaphilayo, kanti bathwala ihlazo labo kanye labo abehlela egodini; ibekwa phakathi kwababuleweyo.
Amukonzera pogona pakati pa anthu ophedwa, pamodzi ndi gulu lake lonse la nkhondo litazungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe ophedwa ndi lupanga. Paja anthuwa ankaopsa mʼdziko la anthu a moyo. Koma tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. Iwo ayikidwa pakati pa anthu ophedwa.
26 Kukhona lapho iMesheki leThubhali, kanye lexuku layo lonke; amangcwaba ayo ayihanqile; bonke bengasokanga, bebulewe ngenkemba; ngoba banikile isethuso sabo elizweni labaphilayo.
“Mesaki ndi Tubala ali komweko, pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo litazungulira manda awo. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe, ophedwa ndi lupanga. Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo.
27 Kodwa kabayikulala lamaqhawe awileyo angawabangasokanga, ehlela esihogweni lezikhali zawo zempi, abeka inkemba zawo ngaphansi kwamakhanda awo; kodwa ububi bawo buzakuba phezu kwamathambo awo; ngoba isethuso samaqhawe sasiselizweni labaphilayo. (Sheol h7585)
Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo. (Sheol h7585)
28 Wena-ke uzakwephulwa phakathi kwabangasokanga, ulale lababulewe ngenkemba.
“Iwenso Farao, udzaphwanyidwa ndi kuyikidwa pakati pa anthu osachita mdulidwe, amene anaphedwa ndi lupanga.
29 Kukhona lapho iEdoma, amakhosi ayo lazo zonke iziphathamandla zayo, abalaliswe lababulewe ngenkemba, kanye lamandla abo; bona bazalala labangasokanga, labehlela egodini.
“Edomu ali kumeneko pamodzi ndi mafumu ake ndi akalonga ake onse. Ngakhale anali amphamvu, koma anayikidwa. Ayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje.
30 Kukhona lapho iziphathamandla zenyakatho, zonke zazo, lawo wonke amaSidoni, asehle lababuleweyo; kusesabiso sabo balenhloni ngenxa yobuqhawe bawo; njalo balele bengasokanga kanye lababuleweyo ngenkemba, bethwele ihlazo labo kanye labo abehlela egodini.
“Akalonga onse akumpoto pamodzi ndi anthu onse a ku Sidoni ali kumeneko. Anatsikira ku dziko la anthu akufa mwamanyazi ngakhale anali owopsa ndi mphamvu zawo. Iwo akugona osachita mdulidwe pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga ndipo akuchita manyazi pamodzi ndi iwo amene anatsikira kale ku manda.
31 UFaro uzababona, aduduzeke ngenxa yexuku lakhe lonke, uFaro lebutho lakhe lonke, ababulewe ngenkemba, itsho iNkosi uJehova.
“Farao ndi gulu lake lankhondo akadzawaona iwowa adzathunza mtima pokumbukira kuchuluka kwa gulu lake lankhondo limene linaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
32 Ngoba ngibekile isethuso sami elizweni labaphilayo; ngakho uzalaliswa phakathi kwabangasokanga kanye lababulewe ngenkemba, uFaro lexuku lakhe lonke, itsho iNkosi uJehova.
Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. Koma Faraoyo pamodzi ndi ankhondo ake onse adzayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi amene anaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< UHezekheli 32 >