< Akolosai 2 >

1 Kwa mana nipala muitange jinsi ambayo nibile na taabu zanyansima kwa ajili yinu, kwa bote babile Laodikia na kwa bote ambao babona kwaa minyo yango mu'yega.
Ndikufuna mudziwe kuti ndikukuvutikirani kwambiri, inuyo pamodzi ndi anzanu a ku Laodikaya, ndi ena onse amene sitinaonane maso ndi maso.
2 Napanga kazi ili kuwa mu'mioyo yabe iweze kufarijiwa kwa kuletwa pamope mu'lipendo ni mu'utajiri woti wanansima wa uhakika kamili wa maarifa, mu'kuitanga siri ya kweli ya Nnongo, lwabile ni Kristo.
Cholinga changa nʼchakuti alimbikitsidwe ndi kuyanjana pamodzi mʼchikondi, akhale odzaza ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndi kuti azindikire chinsinsi cha Mulungu, chimene ndi Khristu.
3 Mu'hazina yoti ya hekima ni maarifa ziyowanika kwaa.
Mwa Iyeyu muli chuma chonse chobisidwa cha nzeru ndi chidziwitso.
4 Nilongela nyoo ili kwamba mundu yeyoti kana aise kuwapangia hila kwa hotuba yabile ni ushawishi.
Ndikukuwuzani zimenezi kuti wina aliyense asakunamizeni ndi kukukopani ndi mawu ake.
5 Na ingawa nibile kwaa pamope ni nenga mu'yega, lakini nabile ni mwenga mu'roho. Napuraika kuubona utaratibu winu unoite ni ngupu ya imani yinu mu'Kristo.
Pakuti ngakhale sindili pakati panu mʼthupi, ndili nanu pamodzi mu mzimu, ndipo ndikukondwa kuona kuti mukulongosola bwino zonse ndiponso kuti chikhulupiriro chanu mwa Khristu ndi chokhazikika ndithu.
6 Kati mwampokii Kristo Ngwana, mutyange mu'ywembe.
Tsono popeza munavomereza Khristu Yesu kukhala Ambuye anu, mupitirire kukhala mwa Iyeyo.
7 Muiimarishe mu'ywembe, muchengwe nkati ya ywembe, muimarishwe nkati ya imani kati mwamupundishilwe, kutabilwa mu'shukrani yanyansima.
Mukhale ozikika mizu mwa Iye, ndipo moyo wanu umangike pa Iye. Mulimbike mʼchikhulupiriro monga momwe munaphunzirira, ndipo kuyamika kwanu kusefukire.
8 Mulole ya kuwa mundu yeyote kana abanase kwa falsafa ni maneno matupu ga ubocho lingana na mapokeo ga bandu, lingana na kanuni ya kidunia, na lingana kwaa na Kristo.
Musalole kuti wina aliyense akutengeni ukapolo ndi mʼnzeru zachinyengo zolongosola zinthu zozama, zomwe zimachokera ku miyambo ya anthu ndi ku maganizo awo okhudza za dziko lapansi osati kwa Khristu.
9 Kwa kuwa mu'ywembe ukamilifu woti wa Nnongo utamile mu'yega.
Pakuti mʼthupi la Khristu mumakhala umulungu wonse wathunthu.
10 Mwenga mwatijazwa mu'ywembe. Ywembe nga ntwe wa kila uweza ni mamlaka.
Ndipo inunso ndinu athunthu mwa Khristu. Iye ndiye mtsogoleri wa pamwamba pa maufumu onse ndi maulamuliro wonse.
11 Mu'ywembe kae mwatitahiriwa kwa tohara ipangilwa kwaa na bandu mu'kuboyelwa yega wa nyama, lakini nga mu'tohara ya Kristo.
Mwa Iye inunso munachita mdulidwe mʼthupi lanu, osati mdulidwe ochitidwa ndi manja a anthu ayi, koma ochitidwa ndi Khristu pamene anavula khalidwe lanu lauchimo lija.
12 Mwatisikwa pamope ni ywembe mu'ubatizo. Na kwa ndela ya imani ywembe mwatifufuliwa kwa uweza wa Nnongo, ywabile atikutufufua boka mu'kiwo.
Mu ubatizo, munayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Khristu ndi kuukitsidwa naye pamodzi, pokhulupirira mphamvu za Mulungu amene anamuukitsa kwa akufa.
13 Na mwabile mwatiwaa mu'makosa yinu na kutahiriwa kwaa kwa yega yinu, awapangite ukoto pamope ni ywembe ni kuasamehe makosa yitu yote.
Pamene munali akufa chifukwa cha machimo anu ndi osachita mdulidwe mʼmitima mwanu, Mulungu anakupatsani moyo mwa Khristu. Iye anatikhululukira machimo athu onse.
14 Atikuifuta kumbukumbu ya madeni yaiandikilwe, ni taratibu yaibile kunchogo na twenga. Aiboite yote na kuigongomea msalabani.
Anafafaniza kalata ya ngongole yathu, pomwe panali milandu yotitsutsa ife. Iye anayichotsa, nayikhomera pa mtanda.
15 Atikuiboywa ngupu ni mamlaka. Atikugabeka wazi na kugapanga kuwa sherehe ya ushaidi kwa ndela ya msalaba wake.
Ndipo atalanda zida maufumu ndi maulamuliro, Iye anawachititsa manyazi powayendetsa pamaso pa anthu onse atawagonjetsa ndi mtanda.
16 Kwa nyo, mundu kana abamuhukumu mwenga mu'kulya au mu'kunywa, au kuhusu lisoba lya sikukuu au mwezi waayambe, au lisoba lya Sabato.
Nʼchifukwa chake musalole wina aliyense kukuzengani mlandu chifukwa cha zimene mumadya kapena kumwa, kapena za masiku achikondwerero cha chipembedzo, za chikondwerero cha mwezi watsopano, kapena za tsiku la Sabata.
17 Ayee nga ivuli ya makowe gaisa, lakini kiini nga Kristo.
Zimenezi ndi chithunzithunzi chabe cha zinthu zimene zikubwera, koma choonadi chenicheni chikupezeka mwa Khristu.
18 Mundu yeyote kana anyang'anywe tuzo yake kwa tamaniya unyenyekevu ni kwa kuabudu mamlaka. Mundu wa jinsi yee ujingya mu'makowe yaayabonikiye ni kushawishiwa ni mawazo yake kwa yega.
Musalole kuti wina aliyense amene amakonda kudzichepetsa mwachiphamaso ndi kumapembedza angelo akulepheretseni kukalandira mphotho. Munthu woteroyu amayankhulanso mwatsatanetsatane zinthu zimene akuti anaziona mʼmasomphenya. Anthuwa ndi odzitukumula ndi fundo zopanda pake zochokera mʼmaganizo mwawo amene si auzimu.
19 Ywembe aukamwa kwaa ntwe kuwa yega woti pitya viungo vyake ni mifupa uungwa na kushikamanikiwa kwa mpamo; ni hukua kwa ukuaji ubokana no Nnongo.
Iwo sakulumikizananso ndi mutu, kumene kumachokera thupi lonse, logwirizidwa ndi kumangiriridwa pamodzi ndi mʼmitsempha yake ndi mnofu, limene limakula monga mmene Mulungu afunira kuti likulire.
20 Mana itei mwati waa pamope ni Kristo kwa tabia za dunia, mbona mwatama kati mwatiwajibika kwa dunia:
Popeza munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nayo miyambo ya dziko lapansi lino, nʼchifukwa chiyani mukukhalanso ngati a dziko lapansi lino? Bwanji mukumvera malamulo monga awa:
21 “Kana muikamwe, wala kuionja, wala kuigusa?”
“Usagwire chakuti,” “Usalawe chakuti,” “Usakhudze chakuti?”
22 Aga goti yatiamuliwa kwa ajili ya uharibifu woisa ni matumizi, bokana na maelekezo ni mapundisho ga bandu.
Malamulo amenewa amakhudza zinthu zimene zimatha zikamagwiritsidwa ntchito, ndipo malamulo ndi zophunzitsa za anthu chabe.
23 Saliya zino zabile ni hekima ya dini zabile zatitengwa kwa ubinafsi ni unyeyekevu ni mateso ga yega. Lakini zabile kwaa ni thamani dhidi ya tamaa ya yega.
Ndithu malamulo oterewa amaoneka ngati anzeru, pakuti amalamulira anthu ambiri pa zachipembedzo ndi pa zakudzichepetsa kwa chiphamaso, ndi pa zakuzunza thupi lawo, koma alibe mphamvu zoletsa kuchita zofuna za thupilo.

< Akolosai 2 >