< Salmenes 20 >

1 Til sangmesteren; en salme av David. Herren bønnhøre dig på nødens dag, Jakobs Guds navn berge dig!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
2 Han sende dig hjelp fra helligdommen og støtte dig fra Sion!
Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
3 Han komme alle dine matoffer i hu og finne ditt brennoffer godt! (Sela)
Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
4 Han gi dig efter ditt hjerte og fullbyrde alt ditt råd!
Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
5 Måtte vi kunne juble over din frelse og løfte seiersmerket i vår Guds navn! Herren opfylle alle dine bønner!
Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
6 Nu vet jeg at Herren frelser sin salvede; han svarer ham fra sin hellige himmel med frelsende storverk av sin høire hånd.
Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
7 Hine priser vogner, hine hester, men vi priser Herrens, vår Guds navn.
Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
8 De synker og faller, men vi står og holder oss oppe.
Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
9 Herre, frels! Kongen bønnhøre oss på den dag vi roper!
Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!

< Salmenes 20 >