< Salomos Høisang 5 >

1 Jeg er kommet til min have, min søster, min brud! Jeg har plukket min myrra og min balsam, jeg har ett min honningkake og min honning, jeg har drukket min vin og min melk. Et, venner, og drikk! Drikk eder lystige, mine elskede!
Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga; ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga. Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe; ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga. Abwenzi Idyani abwenzi anga, imwani; Inu okondana, imwani kwambiri.
2 Jeg sover, men mitt hjerte våker; da lyder min elskedes røst - han banker på: Lukk op for mig, min søster, min venninne, min due, du rene! For mitt hode er fullt av dugg, mine lokker av nattens dråper.
Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso. Tamverani, bwenzi langa akugogoda: “Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa, nkhunda yanga, wangwiro wanga. Mutu wanga wanyowa ndi mame, tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”
3 Jeg sa: Jeg har tatt av mig min kjortel, skulde jeg da ta den på igjen? Jeg har tvettet mine føtter, skulde jeg da skitne dem til?
Ndavula kale zovala zanga, kodi ndizivalenso? Ndasamba kale mapazi anga kodi ndiwadetsenso?
4 Min elskede rakte sin hånd inn gjennem luken; da blev mitt hjerte rørt for hans skyld.
Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko; mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.
5 Jeg stod op for å lukke op for min elskede, og mine hender dryppet av myrra, mine fingrer av flytende myrra, som vætte låsens håndtak.
Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo, ndipo manja anga anali noninoni ndi mure, zala zanga zinali mure chuchuchu, pa zogwirira za chotsekera.
6 Jeg lukket op for min elskede, men min elskede hadde vendt om og gått bort; min sjel var ute av sig selv over hans ord; jeg lette efter ham, men fant ham ikke; jeg ropte på ham, men han svarte mig ikke.
Ndinamutsekulira wachikondi wanga, koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita. Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake. Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze. Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.
7 Vekterne, som går omkring i byen, møtte mig, de slo mig, de såret mig; de tok mitt slør fra mig, vekterne på murene.
Alonda anandipeza pamene ankayendera mzindawo. Anandimenya ndipo anandipweteka; iwo anandilanda mwinjiro wanga, alonda a pa khoma aja!
8 Jeg ber eder inderlig, I Jerusalems døtre! Om I finner min elskede, hvad skal I si ham? - At jeg er syk av kjærlighet.
Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani, mukapeza wokondedwa wangayo, kodi mudzamuwuza chiyani? Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.
9 Hvad er din elskede fremfor andre elskede, du fagreste blandt kvinner, hvad er din elskede fremfor andre elskede, siden du ber oss så inderlig?
Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji? Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani kuti uzichita kutipempha motere?
10 Min elskede er hvit og rød, utmerket fremfor ti tusen.
Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi pakati pa anthu 1,000.
11 Hans hode er som det fineste gull; hans lokker er kruset, sorte som ravnen.
Mutu wake ndi golide woyengeka bwino; tsitsi lake ndi lopotanapotana, ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.
12 Hans øine er som duer ved rinnende bekker; de bader sig i melk, de hviler i sin ramme.
Maso ake ali ngati nkhunda mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, ngati nkhunda zitasamba mu mkaka, zitayima ngati miyala yamtengowapatali.
13 Hans kinner er som velluktende blomstersenger, som det vokser krydderurter i; hans leber er som liljer, de drypper av flytende myrra.
Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya zopatsa fungo lokoma. Milomo yake ili ngati maluwa okongola amene akuchucha mure.
14 Hans hender er gullringer med innlagte krysolitter, hans midje er et kunstverk av elfenben, dekket med safirer.
Manja ake ali ngati ndodo zagolide zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali. Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu woyikamo miyala ya safiro.
15 Hans ben er marmorstøtter, som står på fotstykker av fineste gull; hans skikkelse er som Libanon, herlig som sedrene.
Miyendo yake ili ngati mizati yamwala, yokhazikika pa maziko a golide. Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni, abwino kwambiri ngati mkungudza.
16 Hans gane er sødme, og alt ved ham er liflighet. Slik er min elskede, slik er min venn, I Jerusalems døtre!
Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri; munthuyo ndi wokongola kwambiri! Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa, inu akazi a ku Yerusalemu.

< Salomos Høisang 5 >