< حَجّای 2 >

در روز بیست و یکم ماه هفتم، کلام خداوند بواسطه حجی نبی نازل شده، گفت: ۱ 1
Pa tsiku la 21 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Yehova anayankhula kudzera mwa mneneri Hagai kuti:
زربابل بن شالتیئیل والی یهودا و یهوشع بن یهوصادق رئیس کهنه، و بقیه قوم را خطاب کرده، بگو: ۲ 2
“Yankhula kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, kwa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi kwa anthu onse otsala. Afunse kuti,
کیست در میان شما که باقی‌مانده واین خانه را در جلال نخستینش دیده باشد؟ پس الان در نظر شما چگونه می‌نماید؟ آیا در نظر شماناچیز نمی نماید؟ ۳ 3
‘Kodi alipo amene watsala pakati panu amene anaona ulemerero wakale wa Nyumba iyi? Nanga tsopano ikuoneka motani kwa inu? Kodi sikuoneka ngati yopanda pake kwa inu?
اما الان خداوند می‌گوید: ای زربابل قوی‌دل باش و‌ای یهوشع بن یهوصادق رئیس کهنه قوی‌دل باش و‌ای تمامی قوم زمین قوی‌دل باشید و خداوند می‌فرماید که مشغول بشوید زیرا که من با شما هستم. قول یهوه صبایوت این است. ۴ 4
Iwe Zerubabeli, limba mtima tsopano,’ akutero Yehova. ‘Limba mtima, iwe Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe. Limbani mtima, anthu nonse a mʼdziko,’ akutero Yehova, ‘ndipo gwirani ntchito. Pakuti ine ndili nanu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
برحسب کلام آن عهدی که در حین بیرون آوردن شما از مصر با شما بستم وچونکه روح من در میان شما قایم می‌باشد، ترسان مباشید. ۵ 5
‘Izi ndi zimene ndinapangana nanu pamene munkatuluka ku Igupto. Ndipo Mzimu wanga uli pakati panu. Musachite mantha.’
زیرا که یهوه صبایوت چنین می‌گوید: یک دفعه دیگر و آن نیز بعد از اندک زمانی، آسمانها و زمین و دریا و خشکی را متزلزل خواهم ساخت. ۶ 6
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakapita nthawi pangʼono ndidzagwedezanso thambo ndi dziko lapansi, nyanja ndi mtunda.
و تمامی امت‌ها را متزلزل خواهم ساخت و فضیلت جمیع امت‌ها خواهندآمد و یهوه صبایوت می‌گوید که این خانه را ازجلال پر خواهم ساخت. ۷ 7
Ndidzagwedeza mitundu yonse ya anthu, ndipo chimene mitundu yonse ya anthu imachifuna chidzabwera, ndipo ndidzaza Nyumba ino ndi ulemerero,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
یهوه صبایوت می‌گوید: نقره از آن من و طلا از آن من است. ۸ 8
‘Siliva yense ndi wanga, golide yense ndi wanganso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
یهوه صبایوت می‌گوید: جلال آخر این خانه ازجلال نخستینش عظیم تر خواهد بود و در این مکان، سلامتی را خواهم بخشید. قول یهوه صبایوت این است. ۹ 9
‘Ulemerero wa nyumba iyi udzaposa ulemerero wa nyumba yoyamba ija,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo pamalo pano ndidzakhazikitsapo mtendere,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
در روز بیست و چهارم ماه نهم از سال دوم داریوش، کلام خداوند بواسطه حجی نبی نازل شده، گفت: ۱۰ 10
Chaka chachiwiri cha Dariyo, pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti:
یهوه صبایوت چنین می‌گوید: ازکاهنان درباره شریعت سوال کن و بپرس. ۱۱ 11
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Funsa ansembe za zimene lamulo likunena:
اگرکسی گوشت مقدس را در دامن جامه خود برداردو دامنش به نان یا آش یا شراب یا روغن یا به هرقسم خوراک دیگر برخورد، آیا آن مقدس خواهد شد؟ و کاهنان جواب دادند که نی. ۱۲ 12
Ngati munthu wakulunga nyama yopatulika mu mkanjo wake, ndipo mkanjowo nʼkukhudza buledi kapena msuzi, kapena vinyo, mafuta kapena chakudya cha mtundu wina uliwonse, kodi zimenezo zimasanduka zopatulika?’” Ansembe anayankha kuti, “Ayi.”
پس حجی پرسید: اگر کسی‌که از میتی نجس شده باشد یکی از اینها را لمس نماید آیا آن نجس خواهد شد؟ و کاهنان در جواب گفتند که نجس خواهد شد. ۱۳ 13
Pamenepo Hagai anati, “Ngati munthu amene anayipitsidwa pokhudza mtembo akhudza chimodzi cha zinthu zimenezi, kodi chinthucho chimayipitsidwa?” Ansembe anayankha kuti, “Inde, chimayipitsidwa.”
پس حجی تکلم نموده، گفت: خداوند می‌فرماید این قوم همچنین هستند و این امت به نظر من همچنین می‌باشند و همه اعمال دستهای ایشان چنین است و هر هدیه‌ای که درآنجا می‌برند نجس می‌باشد. ۱۴ 14
Pamenepo Hagai anati, “‘Ndi mmene zilili ndi anthu awa ndi dziko ili pamaso panga,’ akutero Yehova. ‘Chilichonse amachita ndiponso chilichonse chimene amapereka nʼchodetsedwa.
و الان دل خود رامشغول سازید از این‌روز و قبل از این، پیش ازآنکه سنگی برسنگی در هیکل خداوند گذاشته شود. ۱۵ 15
“‘Tsopano muganizire zimenezi kuyambira lero mpaka mʼtsogolo. Ganizirani momwe zinthu zinalili asanayambe kumanga nyumba ya Yehova.
در تمامی این ایام چون کسی به توده بیست (من ) می‌آمد فقط ده (من ) بود و چون کسی به میخانه می‌آمد تا پنجاه رطل از آن بکشد، فقطبیست رطل بود. ۱۶ 16
Pamene munthu ankayembekezera miyeso ya tirigu makumi awiri ankangopeza khumi yokha. Munthu akapita kuti akatunge miyeso makumi asanu ya vinyo mu mtsuko, ankangopeza miyeso makumi awiri yokha.
و شما را و تمامی اعمال دستهای شما را به باد سموم و یرقان و تگرگ زدم. لیکن خداوند می‌گوید بسوی من بازگشت ننمودید. ۱۷ 17
Ndinawononga ntchito yonse ya manja anu ndi chinsikwi, chiwawu ndi matalala, komabe inu simunatembenukire kwa Ine,’ akutero Yehova
الان دل خود را مشغول سازید از این‌روز به بعد، یعنی از روز بیست و چهارم ماه نهم، از روزی که بنیاد هیکل خداوند نهاده شد، دل خود را مشغول سازید. ۱۸ 18
‘Kuyambira lero tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi mpaka mʼtsogolo, chonde ganizirani bwino tsiku limene munayika maziko a nyumba ya Yehova. Ganizirani bwino.
آیا تخم هنوز در انباراست و مو و انجیر و انار و درخت زیتون هنوزمیوه خود را نیاورده‌اند؟ از این‌روز برکت خواهم داد. ۱۹ 19
Kodi mʼnkhokwe mwatsala mbewu? Mpaka lero, mpesa ndi mtengo wa mkuyu, makangadza ndi mtengo wa olivi sizinabereke zipatso. “‘Kuyambira lero mpaka mʼtsogolo ndidzakudalitsani.’”
و کلام خداوند بار دوم در بیست و چهارم ماه بر حجی نازل شده، گفت: ۲۰ 20
Yehova anayankhula ndi Hagai kachiwiri, pa tsiku la 24 la mwezi kuti:
زربابل والی یهودا را خطاب کرده، بگو: من آسمانها و زمین رامتزلزل خواهم ساخت. ۲۱ 21
“Uza Zerubabeli, bwanamkubwa wa Yuda, kuti ndidzagwedeza thambo ndi dziko lapansi.
و کرسی ممالک را واژگون خواهم نمود و قوت ممالک امت‌ها راهلاک خواهم ساخت و ارابه‌ها و سواران آنها راسرنگون خواهم کرد و اسبها و سواران آنها به شمشیر یکدیگر خواهند افتاد. ۲۲ 22
Ndidzagwetsa mipando yaufumu ndi kuwononga mphamvu za maufumu achilendo. Ndidzagubuduza magaleta ndi okwerapo ake; akavalo ndi okwerapo ake adzagwa, aliyense adzaphedwa ndi lupanga la mʼbale wake.
یهوه صبایوت می گوید: در آن روز‌ای بنده من زربابل بن شالتیئیل، تو را خواهم گرفت و خداوند می‌گویدکه تو را مثل نگین خاتم خواهم ساخت زیرا که من تو را برگزیده‌ام. قول یهوه صبایوت این است. می گوید: در آن روز‌ای بنده من زربابل بن شالتیئیل، تو را خواهم گرفت و خداوند می‌گویدکه تو را مثل نگین خاتم خواهم ساخت زیرا که من تو را برگزیده‌ام. قول یهوه صبایوت این است. ۲۳ 23
“‘Tsiku limenelo,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse, ‘ndidzakutenga, iwe mtumiki wanga Zerubabeli mwana wa Sealatieli,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakusandutsa kukhala mphete yanga yolamulira, pakuti ndasankha iwe,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

< حَجّای 2 >