< اشعیا 26 >

در آن روز این سرود در زمین یهوداسراییده خواهد شد؛ ما را شهری قوی است که دیوارها و حصار آن نجات است. ۱ 1
Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi. Tili ndi mzinda wolimba. Mulungu amawuteteza ndi zipupa ndi malinga.
دروازه‌ها را بگشایید تا امت عادل که امانت رانگاه می‌دارند داخل شوند. ۲ 2
Tsekulani zipata za mzinda kuti mtundu wolungama ndi wokhulupirika ulowemo.
دل ثابت را درسلامتی کامل نگاه خواهی داشت، زیرا که بر توتوکل دارد. ۳ 3
Inu mudzamupatsa munthu wa mtima wokhazikika mtendere weniweni.
بر خداوند تا به ابد توکل نمایید، چونکه در یاه یهوه صخره جاودانی است. ۴ 4
Mudalireni Yehova mpaka muyaya, chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.
زیراآنانی را که بر بلندیها ساکنند فرود می‌آورد. وشهر رفیع را به زیر می‌اندازد. آن را به زمین انداخته، با خاک یکسان می‌سازد. ۵ 5
Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba, iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula, amagumula makoma ake ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.
پایها آن راپایمال خواهد کرد. یعنی پایهای فقیران وقدمهای مسکینان. ۶ 6
Mapazi a anthu akuwupondereza, mapazi a anthu oponderezedwa, mapazi anthu osauka.
طریق عادلان استقامت است. ای تو که مستقیم هستی طریق عادلان را هموار خواهی ساخت. ۷ 7
Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza, Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.
پس‌ای خداوند در طریق داوریهای توانتظار تو را کشیده‌ایم. و جان ما به اسم تو و ذکر تو مشتاق است. ۸ 8
Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama, ife timayembekezera Inu; mitima yathu imakhumba kukumbukira ndi kulemekeza dzina lanu.
شبانگاه به‌جان خود مشتاق توهستم. و بامدادان به روح خود در اندرونم تو رامی طلبم. زیرا هنگامی که داوریهای تو بر زمین آید سکنه ربع مسکون عدالت را خواهندآموخت. ۹ 9
Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse; nthawi yammawa ndimafunafuna Inu. Pamene muweruza dziko lapansi anthu amaphunzira kuchita chilungamo.
هرچند بر شریر ترحم شود عدالت را نخواهد آموخت. در زمین راستان شرارت می‌ورزد و جلال خداوند را مشاهده نمی نماید. ۱۰ 10
Ngakhale mukomere mtima anthu oyipa, saphunzira chilungamo. Amachita zoyipa mʼdziko la chilungamo, ndipo sazindikira ululu wa Yehova.
‌ای خداوند دست تو برافراشته شده است امانمی بینند. لیکن چون غیرت تو را برای قوم ملاحظه کنند خجل خواهند شد. و آتش نیزدشمنانت را فرو خواهد برد. ۱۱ 11
Inu Yehova, mwatukula dzanja lanu kuti muwalange, koma iwo sakuliona dzanjalo. Aloleni anthu aone ndi kuchita manyazi poona mmene mukondera anthu anu; ndipo moto umene mwasonkhera adani anu uwapsereze.
‌ای خداوند سلامتی را برای ما تعیین خواهی نمود. زیرا که تمام کارهای ما را نیز برای ما به عمل آورده‌ای. ۱۲ 12
Yehova, mumatipatsa mtendere; ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.
‌ای یهوه خدای ما آقایان غیر از تو بر ما استیلا داشتند. اما به تو فقط اسم تورا ذکر خواهیم کرد. ۱۳ 13
Inu Yehova Mulungu wathu, ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena mʼmalo mwanu, koma ife timalemekeza dzina lanu lokha.
ایشان مردند و زنده نخواهند شد. خیالها گردیدند و نخواهندبرخاست. بنابراین ایشان را سزا داده، هلاک ساختی و تمام ذکر ایشان را محو نمودی. ۱۴ 14
Iwo tsopano sadzadzukanso; mizimu yawo sidzabwera kudzativutitsa pakuti mwawalanga ndipo mwawawononga; palibenso amene amawakumbukira.
قوم را افزودی‌ای خداوند قوم را مزید ساخته، خویشتن را جلال دادی. و تمامی حدود زمین راوسیع گردانیدی. ۱۵ 15
Inu Yehova, mwaukulitsa mtundu wathu; mwauchulukitsa ndithu ndipo mwalandirapo ulemu; mwaukuza mbali zonse za dziko.
‌ای خداوند ایشان در حین تنگی، تو راخواهند طلبید. و چون ایشان را تادیب نمایی دعاهای خفیه خواهند ریخت. ۱۶ 16
Yehova, anthu anu anabwera kwa Inu pamene anali mʼmasautso; pamene munawalanga, iwo anapemphera kwa Inu.
مثل زن حامله‌ای که نزدیک زاییدن باشد و درد او راگرفته، از آلام خود فریاد بکند همچنین ما نیز‌ای خداوند در حضور تو هستیم. ۱۷ 17
Monga mayi woyembekezera pamene nthawi yake yobereka yayandikira amamva kupweteka ndipo amalira ndi ululu, ifenso tinali chimodzimodzi pamaso panu, Inu Yehova.
حامله شده، دردزه ما را گرفت و باد را زاییدیم. و در زمین هیچ نجات به ظهور نیاوردیم. و ساکنان ربع مسکون نیفتادند. ۱۸ 18
Ife chimodzimodzi tinamva ululu, ngati mayi pa nthawi yobala mwana, koma sitinapindulepo kanthu, kapena kupulumutsa dziko lapansi; sitinabadwitse anthu atsopano pa dziko pano.
مردگان تو زنده خواهند شد و جسدهای من خواهند برخاست. ای شما که در خاک ساکنیدبیدار شده، ترنم نمایید! زیرا که شبنم تو شبنم نباتات است. و زمین مردگان خود را بیرون خواهدافکند. ۱۹ 19
Koma anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo; matupi awo adzadzuka. Iwo amene ali ku fumbi tsopano adzadzuka ndi kuyimba mosangalala. Monga mame amafewetsa pansi kutsitsimutsa zomera, momwenso Yehova adzaukitsa anthu amene anafa kale.
‌ای قوم من بیایید به حجره های خویش داخل شوید و درهای خود را در عقب خویش ببندید. خویشتن را اندک لحظه‌ای پنهان کنید تاغضب بگذرد. ۲۰ 20
Abale anga, pitani mukalowe mʼnyumba zanu ndipo mukadzitsekere; mukabisale kwa kanthawi kochepa mpaka ukali wake utatha.
زیرا اینک خداوند از مکان خود بیرون می‌آید تا سزای گناهان ساکنان زمین را به ایشان برساند. پس زمین خونهای خود رامکشوف خواهد ساخت و کشتگان خویش رادیگر پنهان نخواهد نمود. ۲۱ 21
Taonani, Yehova akubwera kuchokera kumene amakhala; akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo awo. Dziko lapansi lidzawulula magazi amene anakhetsedwa pa dzikolo; dziko lapansi silidzabisanso mitembo ya anthu ophedwa.

< اشعیا 26 >