< ارمیا 43 >

و چون ارمیا فارغ شد از گفتن به تمامی قوم، تمامی کلام یهوه خدای ایشان راکه یهوه خدای ایشان آن را به واسطه او نزد ایشان فرستاده بود یعنی جمیع این سخنان را، ۱ 1
Yeremiya atatsiriza kuwawuza anthuwo mawu onse a Yehova Mulungu wawo, amene Yehova anamutuma kuti akawawuze,
آنگاه عزریا ابن هوشعیا و یوحانان بن قاریح و جمیع مردان متکبر، ارمیا را خطاب کرده، گفتند: «تودروغ می‌گویی، یهوه خدای ما تو را نفرستاده است تا بگویی به مصر مروید و در آنجا سکونت منمایید. ۲ 2
Azariya mwana wa Hosayia ndi Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi anthu onse odzikuza anawuza Yeremiya kuti, “Ukunama iwe! Yehova Mulungu wathu sanakutume kuti unene kuti, ‘Musapite ku Igupto kukakhala kumeneko.’
بلکه باروک بن نیریا تو را بر مابرانگیخته است تا ما را به‌دست کلدانیان تسلیم نموده، ایشان ما را بکشند و به بابل به اسیری ببرند.» ۳ 3
Koma ndi Baruki mwana wa Neriya amene akukulimbikitsa kuti utiletse zopita ku Igupto ndi kuti mʼmalo mwake tidzipereke mʼmanja mwa Ababuloni, kuti iwo atiphe kapena kutitenga ukapolo ku Babuloni.”
و یوحانان بن قاریح و همه سرداران لشکر وتمامی قوم فرمان خداوند را که در زمین یهودابمانند، اطاعت ننمودند. ۴ 4
Motero Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi anthu onse sanamvere lamulo la Yehova loti akhale mʼdziko la Yuda.
بلکه یوحانان بن قاریح و همه سرداران لشکر، بقیه یهودا را که از میان تمامی امت هایی که در میان آنها پراکنده شده بودند برگشته، در زمین یهودا ساکن شده بودندگرفتند. ۵ 5
Mʼmalo mwake, Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo anatenga anthu onse otsala a ku Yuda amene anabwera kudzakhala mʼdziko la Yuda kuchokera ku mayiko onse kumene anabalakirako.
یعنی مردان و زنان و اطفال و دختران پادشاه و همه کسانی را که نبوزردان رئیس جلادان، به جدلیا ابن اخیقام بن شافان سپرده بود وارمیای نبی و باروک بن نیریا را. ۶ 6
Mʼgulu la anthu otengedwalo munali amuna onse, akazi ndi ana, ana aakazi a mfumu, ndiponso anthu amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anawasiya kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani pamodzinso ndi mneneri Yeremiya ndi Baruki mwana wa Neriya.
و به زمین مصررفتند زیرا که قول خداوند را گوش نگرفتند و به تحفنحیس آمدند. ۷ 7
Kotero anthuwo analowa mʼdziko la Igupto chifukwa anakana kumvera Yehova, nakafika ku Tapanesi.
پس کلام خداوند در تحفنحیس بر ارمیانازل شده، گفت: ۸ 8
Ndipo Yehova anayankhula ndi Yeremiya ku Tapanesi kuti,
«سنگهای بزرگ به‌دست خودبگیر و آنها را در نظر مردان یهودا در سعه‌ای که نزد دروازه خانه فرعون در تحفنحیس است با گچ بپوشان. ۹ 9
“Tenga miyala inayi yayikulu ndipo uyikwirire mʼdothi pa chiwundo cha polowera ku nyumba yaufumu ya Farao ku Tapanesi. Uchite zimenezi Ayuda onse akuona.
و به ایشان بگو که یهوه صبایوت خدای اسرائیل چنین می‌گوید: اینک من فرستاده، بنده خود نبوکدرصر پادشاه بابل را خواهم گرفت و کرسی او را بر این سنگهایی که پوشانیدم خواهم نهاد و او سایبان خود را بر آنها خواهدبرافراشت. ۱۰ 10
Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayitana mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzakhazika mpando wake waufumu pa miyala imene ndayikwirira apayi. Iye adzafunyulula tenti yake yaufumu pa miyala imeneyi.
و آمده، زمین مصر را خواهد زد وآنانی را که مستوجب موت‌اند به موت و آنانی راکه مستوجب اسیری‌اند به اسیری و آنانی را که مستوجب شمشیرند به شمشیر (خواهد سپرد). ۱۱ 11
Iye adzabwera kudzathira nkhondo Igupto. Iwo oyenera kufa ndi mliri adzafa ndi mliri, iwo oyenera kutengedwa ukapolo adzatengedwa ukapolo, ndipo iwo oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
و آتشی در خانه های خدایان مصر خواهم افروخت و آنها را خواهد سوزانید و به اسیری خواهد برد و خویشتن را به زمین مصر ملبس خواهد ساخت مثل شبانی که خویشتن را به‌جامه خود ملبس سازد و از آنجا به سلامتی بیرون خواهد رفت. ۱۲ 12
Adzayatsa moto mʼnyumba zopembedzera milungu ya Igupto. Adzayeretsa dziko la Igupto monga momwe mʼbusa amayeretsera chovala chake pochotsamo nsabwe. Pambuyo pake adzachoka mʼdziko la Igupto mwa mtendere.
و تمثالهای بیت شمس را که درزمین مصر است خواهد شکست و خانه های خدایان مصر را به آتش خواهد سوزانید.» ۱۳ 13
Ku Iguptoko adzagwetsa zipilala zachipembedzo za ku nyumba yopembedzera mulungu wa dzuwa. Adzatentha ndi moto nyumba za milungu ya ku Igupto.’”

< ارمیا 43 >