< ارمیا 6 >

ای بنی بنیامین از اورشلیم فرار کنید و کرنارا در تقوع بنوازید و علامتی بر بیت هکاریم برافرازید زیرا که بلایی از طرف شمال وشکست عظیمی رو خواهد داد. ۱ 1
“Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
و من آن دخترجمیل و لطیف یعنی دختر صهیون را منقطع خواهم ساخت. ۲ 2
Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
و شبانان با گله های خویش نزدوی خواهند آمد و خیمه های خود را گرداگرد اوبرپا نموده، هر یک در جای خود خواهند چرانید. ۳ 3
Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
با او جنگ را مهیا سازید و برخاسته، در وقت ظهر برآییم. وای بر ما زیرا که روز رو به زوال نهاده است و سایه های عصر دراز می‌شود. ۴ 4
Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
برخیزید! و در شب برآییم تا قصرهایش رامنهدم سازیم. ۵ 5
Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
زیرا که یهوه صبایوت چنین می فرماید: «درختان را قطع نموده، مقابل اورشلیم سنگر برپا نمایید. زیرا این است شهری که سزاوار عقوبت است چونکه اندرونش تمام ظلم است. ۶ 6
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
مثل چشمه‌ای که آب خود رامی جوشاند همچنان او شرارت خویش رامی جوشاند. ظلم و تاراج در اندرونش شنیده می‌شود و بیماریها و جراحات دایم در نظر من است. ۷ 7
Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
‌ای اورشلیم، تادیب را بپذیر مبادا جان من از تو بیزار شود و تو را ویران و زمین غیرمسکون گردانم.» ۸ 8
Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
یهوه صبایوت چنین می‌گوید که «بقیه اسرائیل را مثل مو خوشه چینی خواهند کرد پس مثل کسی‌که انگور می‌چینددست خود را بر شاخه هایش برگردان.» ۹ 9
Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
کیستند که به ایشان تکلم نموده، شهادت دهم تا بشنوند. هان گوش ایشان نامختون است که نتوانند شنید. اینک کلام خداوند برای ایشان عارگردیده است و در آن رغبت ندارند. ۱۰ 10
Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
و من ازحدت خشم خداوند پر شده‌ام و از خودداری خسته گردیده‌ام پس آن را در کوچه‌ها بر اطفال وبر مجلس جوانان با هم بریز. زیرا که شوهر و زن هر دو گرفتار خواهند شد و شیخ با دیرینه روز. ۱۱ 11
Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
و خانه‌ها و مزرعه‌ها و زنان ایشان با هم از آن دیگران خواهند شد زیرا خداوند می‌گوید که «دست خود را به ضد ساکنان این زمین درازخواهم کرد. ۱۲ 12
Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
چونکه جمیع ایشان چه خرد وچه بزرگ، پر از طمع شده‌اند و همگی ایشان چه نبی و چه کاهن، فریب را بعمل می‌آورند. ۱۳ 13
“Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
وجراحت قوم مرا اندک شفایی دادند، چونکه می‌گویند سلامتی است، سلامتی است با آنکه سلامتی نیست.» ۱۴ 14
Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
آیا چون مرتکب رجاسات شدند خجل گردیدند؟ نی ابد خجل نشدند بلکه حیا را احساس ننمودند. بنابراین خداوندمی گوید که «در میان افتادگان خواهند افتاد وحینی که من به ایشان عقوبت رسانم خواهندلغزید.» ۱۵ 15
Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
خداوند چنین می‌گوید: «بر طریق هابایستید و ملاحظه نمایید و درباره طریق های قدیم سوآل نمایید که طریق نیکو کدام است تا درآن سلوک نموده، برای جان خود راحت بیابید، لیکن ایشان جواب دادند که در آن سلوک نخواهیم کرد. ۱۶ 16
Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
و من پاسبانان بر شما گماشتم (که می‌گفتند): به آواز کرنا گوش دهید، اما ایشان گفتند گوش نخواهیم داد. ۱۷ 17
Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
پس‌ای امت هابشنوید و‌ای جماعت آنچه را که در میان ایشان است بدانید! ۱۸ 18
Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
‌ای زمین بشنو اینک من بلایی براین قوم می‌آورم که ثمره خیالات ایشان خواهدبود زیرا که به کلام من گوش ندادند و شریعت مرانیز ترک نمودند. ۱۹ 19
Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
چه فایده دارد که بخور از سباو قصب الذریره از زمین بعید برای من آورده می‌شود. قربانی های سوختنی شما مقبول نیست و ذبایح شما پسندیده من نی.» ۲۰ 20
Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
بنابراین خداوند چنین می‌گوید: «اینک من پیش روی این قوم سنگهای لغزش دهنده خواهم نهاد و پدران وپسران با هم از آنها لغزش خواهند خورد و ساکن زمین با همسایه‌اش هلاک خواهند شد.» ۲۱ 21
Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
خداوند چنین می‌گوید: «اینک قومی اززمین شمال می‌آورم و امتی عظیم از اقصای زمین خواهند برخاست. ۲۲ 22
Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
و کمان و نیزه خواهندگرفت. ایشان مردان ستمکیش می‌باشند که ترحم ندارند. به آواز خود مثل دریا شورش خواهندنمود و بر اسبان سوار شده، مثل مردان جنگی به ضد تو‌ای دختر صهیون صف آرایی خواهندکرد.» ۲۳ 23
Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
آوازه این را شنیدیم و دستهای ما سست گردید. تنگی و درد مثل زنی که می‌زاید ما را درگرفته است. ۲۴ 24
A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
به صحرا بیرون مشوید و به راه مروید زیرا که شمشیر دشمنان و خوف از هرطرف است. ۲۵ 25
Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
‌ای دختر قوم من پلاس بپوش وخویشتن را در خاکستر بغلطان. ماتم پسر یگانه ونوحه گری تلخ برای خود بکن زیرا که تاراج کننده ناگهان بر ما می‌آید. ۲۶ 26
Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
تو را در میان قوم خودامتحان کننده و قلعه قرار دادم تا راههای ایشان رابفهمی و امتحان کنی. ۲۷ 27
“Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
همه ایشان سخت متمرد شده‌اند و برای نمامی کردن گردش می‌کنند. برنج و آهن می‌باشند و جمیع ایشان فساد کننده‌اند. ۲۸ 28
Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
دم پر زور می‌دمد و سرب درآتش فانی می‌گردد و قالگر عبث قال می‌گذاردزیرا که شریران جدا نمی شوند. ۲۹ 29
Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
نقره ترک شده نامیده می‌شوند زیرا خداوند ایشان را ترک کرده است. ۳۰ 30
Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”

< ارمیا 6 >