< یوحنا 10 >

«آمین آمین به شما می‌گویم هر‌که از دربه آغل گوسفند داخل نشود، بلکه از راه دیگر بالا رود، او دزد و راهزن است. ۱ 1
“Zoonadi, Ine ndikukuwuzani inu Afarisi, kuti munthu amene salowera pa khomo mʼkhola la nkhosa, koma amalowera pena pake ndi wakuba ndi wachifwamba.
و اما آنکه از در داخل شود، شبان گوسفندان است. ۲ 2
Munthu amene amalowera pa khomo ndi mʼbusa wankhosazo.
دربان بجهت او می‌گشاید و گوسفندان آواز او رامی شنوند و گوسفندان خود را نام بنام می‌خواند وایشان را بیرون می‌برد. ۳ 3
Mlonda amamutsekulira khomo, ndipo nkhosa zimamvera mawu ake. Iye amaziyitana mayina nkhosa zakezo, nazitulutsa.
و وقتی که گوسفندان خود را بیرون برد، پیش روی ایشان می‌خرامد وگوسفندان از عقب او می‌روند، زیرا که آواز او رامی شناسند. ۴ 4
Akazitulutsa nkhosa zake zonse, iye amazitsogolera, ndipo nkhosa zakezo zimamutsata chifukwa zimadziwa mawu ake.
لیکن غریب را متابعت نمی کنند، بلکه از او می‌گریزند زیرا که آواز غریبان رانمی شناسند.» ۵ 5
Koma nkhosazo sizidzatsatira mlendo. Izo zidzamuthawa chifukwa sizizindikira mawu a mlendo.”
و این مثل را عیسی برای ایشان آورد، اماایشان نفهمیدند که چه چیز بدیشان می‌گوید. ۶ 6
Yesu ananena mawu ophiphiritsawa, koma Afarisi sanazindikire zimene ankawawuza.
آنگاه عیسی بدیشان باز‌گفت: «آمین آمین به شما می‌گویم که من در گوسفندان هستم. ۷ 7
Choncho Yesu anatinso, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti Ine ndine khomo la nkhosa.
جمیع کسانی که پیش از من آمدند، دزد و راهزن هستند، لیکن گوسفندان سخن ایشان را نشنیدند. ۸ 8
Onse amene anadza ndisanabwere Ine ndi akuba ndi achifwamba, ndipo nkhosa sizinawamvere.
من درهستم هر‌که از من داخل گردد نجات یابد و بیرون و درون خرامد و علوفه یابد. ۹ 9
Ine ndine khomo, aliyense amene alowa kudzera mwa Ine adzapulumuka. Iye adzalowa ndi kutuluka ndi kupeza msipu.
دزد نمی آید مگرآنکه بدزدد و بکشد و هلاک کند. من آمدم تاایشان حیات یابند و آن را زیادتر حاصل کنند. ۱۰ 10
Mbala sibwera chabe koma kuti idzabe, kupha ndi kuwononga. Ine ndabwera kuti iwo akhale ndi moyo, ndi kukhala nawo wochuluka.
«من شبان نیکو هستم. شبان نیکو جان خودرا در راه گوسفندان می‌نهد. ۱۱ 11
“Ine ndine Mʼbusa wabwino. Mʼbusa wabwino amataya moyo wake chifukwa cha nkhosa zake.
اما مزدوری که شبان نیست و گوسفندان از آن او نمی باشند، چون بیند که گرگ می‌آید، گوسفندان را گذاشته، فرار می‌کند و گرگ گوسفندان را می‌گیرد وپراکنده می‌سازد. ۱۲ 12
Wantchito ndi mʼbusa amene nkhosazo si zake. Choncho, pamene aona mmbulu ukubwera, iye amazisiya nkhosazo ndi kuthawa. Ndipo mmbulu umagwira nkhosazo ndikuzibalalitsa.
مزدور می‌گریزد چونکه مزدور است و به فکر گوسفندان نیست. ۱۳ 13
Munthuyo amathawa chifukwa ndi wantchito ndipo sasamalira chilichonse cha nkhosazo.
من شبان نیکو هستم و خاصان خود را می‌شناسم وخاصان من مرا می‌شناسند. ۱۴ 14
“Ine ndine mʼbusa wabwino. Ine ndimazidziwa nkhosa zanga ndipo nkhosa zangazo zimandidziwa,
چنانکه پدر مرامی شناسد و من پدر را می‌شناسم و جان خود رادر راه گوسفندان می‌نهم. ۱۵ 15
monga momwe Atate amandidziwa Ine, ndiponso Ine kudziwira Atatewo. Ndimapereka moyo wanga chifukwa cha nkhosa.
و مرا گوسفندان دیگر هست که از این آغل نیستند. باید آنها را نیزبیاورم و آواز مرا خواهند شنید و یک گله و یک شبان خواهند شد. ۱۶ 16
Ine ndili ndi nkhosa zina zimene sizili za gulu ili. Ine ndiyenera kuzibweretsanso. Izonso zidzamvera mawu anga, ndipo zidzakhala gulu limodzi ndi mʼbusa mmodzi.
و از این سبب پدر مرادوست می‌دارد که من جان خود را می‌نهم تا آن راباز گیرم. ۱۷ 17
Nʼchifukwa chake Atate anga amandikonda, popeza Ine ndikupereka moyo wanga kuti ndiwutengenso.
کسی آن را از من نمی گیرد، بلکه من خود آن را می‌نهم. قدرت دارم که آن را بنهم وقدرت دارم آن را باز گیرم. این حکم را از پدرخود یافتم.» ۱۸ 18
Palibe amene angawuchotse mwa Ine, koma ndikuwupereka mwakufuna kwanga. Ine ndili ndi ulamuliro wa kuwupereka ndi ulamuliro wakuwutenganso. Lamulo ili ndinalandira kwa Atate anga.”
باز به‌سبب این کلام، در میان یهودیان اختلاف افتاد. ۱۹ 19
Pa mawu awa Ayuda anagawikananso.
بسیاری از ایشان گفتند که «دیودارد و دیوانه است. برای چه بدو گوش می‌دهید؟» ۲۰ 20
Ambiri a iwo anati, “Iye ndi wogwidwa ndi ziwanda ndi wamisala. Chifukwa chiyani mukumvera Iye?”
دیگران گفتند که «این سخنان دیوانه نیست. آیا دیو می‌تواند چشم کوران را بازکند؟» ۲۱ 21
Koma ena anati, “Awa si mawu a munthu wogwidwa ndi ziwanda. Kodi ziwanda zingathe bwanji kutsekula maso a wosaona?”
پس در اورشلیم، عید تجدید شد و زمستان بود. ۲۲ 22
Ku Yerusalemu kunali chikondwerero chokumbukira kupatulidwa kwa Nyumba ya Mulungu. Inali nthawi yozizira,
و عیسی در هیکل، در رواق سلیمان می‌خرامید. ۲۳ 23
ndipo Yesu ankayenda mʼbwalo la Nyumbayo ku malo a Solomoni.
پس یهودیان دور او را گرفته، بدوگفتند: «تا کی ما را متردد داری؟ اگر تو مسیح هستی، آشکارا به ما بگو. ۲۴ 24
Ayuda anamuzungulira Iye akunena kuti, “Kodi iwe udzazunguza malingaliro athu mpaka liti? Ngati iwe ndi Khristu, tiwuze momveka.”
عیسی بدیشان جواب داد: «من به شما گفتم و ایمان نیاوردید. اعمالی را که به اسم پدر خود به‌جا می‌آورم، آنهابرای من شهادت می‌دهد. ۲۵ 25
Yesu anayankha kuti, “Ine ndimakuwuzani, koma inu simukhulupirira. Ntchito zimene ndikuchita mʼdzina la Atate anga zikundichitira umboni,
لیکن شما ایمان نمی آورید زیرا از گوسفندان من نیستید، چنانکه به شما گفتم. ۲۶ 26
koma inu simukhulupirira chifukwa simuli a gulu lankhosa zanga.
گوسفندان من آواز مرا می‌شنوندو من آنها را می‌شناسم و مرا متابعت می‌کنند. ۲۷ 27
Nkhosa zanga zimamva mawu anga, Ine ndimazidziwa, ndipo zimanditsata Ine.
ومن به آنها حیات جاودانی می‌دهم و تا به ابد هلاک نخواهند شد و هیچ‌کس آنها را از دست من نخواهد گرفت. (aiōn g165, aiōnios g166) ۲۸ 28
Ine ndimazipatsa moyo wosatha ndipo sizidzawonongeka. Palibe amene adzazikwatula mʼdzanja langa. (aiōn g165, aiōnios g166)
پدری که به من داد از همه بزرگتر است و کسی نمی تواند از دست پدر من بگیرد. ۲۹ 29
Atate anga, amene anandipatsa Ine, ndi akulu kuposa onse. Palibe amene angazikwatule mʼdzanja la Atate anga.
من و پدر یک هستیم.» ۳۰ 30
Ine ndi Atate ndife amodzi.”
آنگاه یهودیان باز سنگها برداشتند تا او راسنگسار کنند. ۳۱ 31
Ayuda anatolanso miyala kuti amugende Iye,
عیسی بدیشان جواب داد: «ازجانب پدر خود بسیار کارهای نیک به شما نمودم. به‌سبب کدام‌یک از آنها مرا سنگسار می‌کنید؟» ۳۲ 32
koma Yesu anawawuza kuti, “Ine ndakuonetsani zinthu zambiri zabwino zodabwitsa kuchokera kwa Atate. Nʼchifukwa chiti mwa izi chimene mukundigendera?”
یهودیان در جواب گفتند: «به‌سبب عمل نیک، تو را سنگسار نمی کنیم، بلکه به‌سبب کفر، زیرا توانسان هستی و خود را خدا می‌خوانی.» ۳۳ 33
Ayuda anayankha kuti, “Ife sitikukugenda chifukwa cha izi, koma popeza ukunyoza Mulungu, chifukwa iwe, munthu wamba, ukuti ndiwe Mulungu.”
عیسی در جواب ایشان گفت: «آیا در تورات شما نوشته نشده است که من گفتم شما خدایان هستید؟ ۳۴ 34
Yesu anawayankha kuti, “Kodi sizinalembedwa mʼmalamulo anu kuti, ‘Ine ndanena kuti ndinu milungu?’
پس اگر آنانی را که کلام خدا بدیشان نازل شد، خدایان خواند و ممکن نیست که کتاب محو گردد، ۳۵ 35
Ngati anawatcha milungu anthu amene analandira mawu a Mulungu, pajatu Malemba sangasweke,
آیا کسی را که پدر تقدیس کرده، به جهان فرستاد، بدو می‌گویید کفر می‌گویی، از آن سبب که گفتم پسر خدا هستم؟ ۳۶ 36
nanga bwanji uyu amene Atate anamuyika padera monga wake weniweni ndi kumutuma ku dziko lapansi? Nanga ndi chifukwa chiyani mukundinena Ine kuti ndikuchita chipongwe? Kodi nʼchifukwa choti ndanena kuti, ‘Ine ndine Mwana wa Mulungu?’
اگر اعمال پدرخود را به‌جا نمی آورم، به من ایمان میاورید. ۳۷ 37
Musandikhulupirire Ine ngati sindichita ntchito za Atate anga.
ولکن چنانچه به‌جا می‌آورم، هرگاه به من ایمان نمی آورید، به اعمال ایمان آورید تا بدانید و یقین کنید که پدر در من است و من در او.» ۳۸ 38
Koma ngati Ine ndikuchita zimenezi, ngakhale kuti simundikhulupirira, khulupirirani ntchito zodabwitsazo, ndipo mudziwe ndi kuzindikira kuti Atate ali mwa Ine, ndiponso Ine ndili mwa Atate.”
پس دیگرباره خواستند او را بگیرند، اما از دستهای ایشان بیرون رفت. ۳۹ 39
Iwo anafuna kumugwiranso koma anawapulumuka mʼmanja mwawo.
و باز به آن طرف اردن، جایی که اول یحیی تعمید می‌داد، رفت و در آنجا توقف نمود. ۴۰ 40
Kenaka Yesu anabwereranso kutsidya la mtsinje wa Yorodani kumalo kumene Yohane ankabatiza mʼmasiku akale. Iye anakhala kumeneko
وبسیاری نزد او آمده، گفتند که یحیی هیچ معجزه ننمود و لکن هر‌چه یحیی درباره این شخص گفت راست است. ۴۱ 41
ndipo anthu ambiri anabwera kwa Iye. Iwo anati, “Ngakhale kuti Yohane sanachite chizindikiro chodabwitsa, zonse zimene Yohane ananena za munthu uyu zinali zoona.”
پس بسیاری در آنجا به او ایمان آوردند. ۴۲ 42
Ndipo pamalo amenewo ambiri anakhulupirira Yesu.

< یوحنا 10 >