< یونس 1 >

و کلام خداوند بر یونس بن امتای نازل شده، گفت: ۱ 1
Yehova anayankhula ndi Yona mwana wa Amitai kuti,
«برخیز و به نینوا شهر بزرگ برو و بر آن ندا کن زیرا که شرارت ایشان به حضورمن برآمده است.» ۲ 2
“Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire motsutsana nawo, chifukwa zoyipa zawo zafika pamaso panga.”
اما یونس برخاست تا از حضور خداوند به ترشیش فرار کند و به یافا فرود آمده، کشتی‌ای یافت که عازم ترشیش بود. پس کرایه‌اش را داده، سوار شد تا همراه ایشان از حضور خداوند به ترشیش برود. ۳ 3
Koma Yona anathawa Yehova ndi kulowera ku Tarisisi. Anapita ku Yopa, kumene anapeza sitima yapamadzi yopita ku Tarisisi. Atagula chiphaso, anakwera sitimayo kupita ku Tarisisi kuthawa Yehova.
و خداوند باد شدیدی بر دریاوزانید که تلاطم عظیمی در دریا پدید آمدچنانکه نزدیک بود که کشتی شکسته شود. ۴ 4
Koma Yehova anatumiza chimphepo champhamvu pa nyanja, ndipo panauka namondwe wamphamvu amene anafuna kuphwanya sitimayo.
وملاحان ترسان شده، هر کدام نزد خدای خوداستغاثه نمودند و اسباب را که در کشتی بود به دریا ریختند تا آن را برای خود سبک سازند. امایونس در اندرون کشتی فرود شده، دراز شد وخواب سنگینی او را در ربود. ۵ 5
Onse oyendetsa sitimayo anachita mantha ndipo aliyense anayamba kupemphera kwa mulungu wake. Ndipo anaponya katundu mʼnyanja kuti sitimayo ipepuke. Koma Yona pa nthawiyi nʼkuti atatsikira mʼkatikati mwa sitimayo kumene anagona tulo tofa nato.
و ناخدای کشتی نزد او آمده، وی را گفت: «ای که خفته‌ای تو را چه شده است؟ برخیز وخدای خود را بخوان شاید که خدا ما را بخاطرآورد تا هلاک نشویم.» ۶ 6
Mkulu wa oyendetsa sitimayo anapita kwa iye ndipo anati, “Kodi iwe, nʼchifukwa chiyani ukugona? Dzuka pemphera kwa mulungu wako! Mwina adzatithandiza, ndipo sitidzawonongeka.”
و به یکدیگر گفتند: «بیایید قرعه بیندازیم تا بدانیم که این بلا به‌سبب چه کس بر ما وارد شده است؟» پس چون قرعه انداختند، قرعه به نام یونس درآمد. ۷ 7
Ndipo oyendetsa sitimayo anayamba kuwuzana kuti, “Bwerani, tichite maere kuti tipeze amene wabweretsa tsoka limeneli.” Iwo anachita maerewo ndipo anagwera Yona.
پس او راگفتند: «ما را اطلاع ده که این بلا به‌سبب چه کس بر ما عارض شده؟ شغل تو چیست و از کجا آمده‌ای و وطنت کدام است و از چه قوم هستی؟» ۸ 8
Tsono anamufunsa kuti, “Tatiwuze, tsoka limeneli latigwera chifukwa chiyani? Umagwira ntchito yanji? Ukuchokera kuti? Kwanu nʼkuti? Ndiwe mtundu wanji wa anthu?”
او ایشان را جواب داد که: «من عبرانی هستم و ازیهوه خدای آسمان که دریا و خشکی را آفریده است ترسان می‌باشم.» ۹ 9
Iye anayankha kuti, “Ndine Mhebri, ndipo ndimapembedza Yehova, Mulungu Wakumwamba, amene analenga nyanja ndi mtunda.”
پس آن مردمان سخت‌ترسان شدند و او را گفتند: «چه کرده‌ای؟» زیرا که ایشان می‌دانستند که از حضور خداوند فرار کرده است چونکه ایشان را اطلاع داده بود. ۱۰ 10
Izi zinawachititsa mantha kwambiri ndipo anafunsa kuti, “Kodi wachita chiyani?” (Iwo ankadziwa kuti iyeyo amathawa Yehova, chifukwa nʼkuti atawawuza kale).
و او راگفتند: «با تو چه کنیم تا دریا برای ما ساکن شود؟» زیرا دریا در تلاطم همی افزود. ۱۱ 11
Namondwe ananka nakulirakulirabe pa nyanjapo. Tsono anamufunsa iye kuti, “Kodi tikuchite chiyani kuti nyanjayi ikhale bata?”
او به ایشان گفت: «مرا برداشته، به دریا بیندازید ودریا برای شما ساکن خواهد شد، زیرا می‌دانم این تلاطم عظیم به‌سبب من بر شما وارد آمده است. ۱۲ 12
Iye anayankha kuti, “Nyamuleni ndi kundiponya mʼnyanjamu ndipo nyanjayi ikhala bata. Ndikudziwa kuti wolakwa ndine nʼchifukwa chake chimphepo champhamvuchi chabwera pa inu.”
اما آن مردمان سعی نمودند تا کشتی را به خشکی برسانند اما نتوانستند زیرا که دریا به ضدایشان زیاده و زیاده تلاطم می‌نمود. ۱۳ 13
Komabe oyendetsa sitimayo anayesetsa kupalasa kwambiri kuti abwerere ku mtunda koma analephera ndithu poti nyanja inawinduka kwambiri kuposa poyamba paja
پس نزدیهوه دعا کرده، گفتند: «آه‌ای خداوند به‌خاطرجان این شخص هلاک نشویم و خون بی‌گناه را برما مگذار زیرا تو‌ای خداوند هر‌چه می‌خواهی می‌کنی.» ۱۴ 14
Pamenepo iwo anafuwulira kwa Yehova nati, “Inu Yehova, musalole kuti ife tife chifukwa cha moyo wa munthu uyu. Musatizenge mlandu wa kupha munthu wosalakwa, pakuti ife tachita monga mwakufuna kwanu, Inu Yehova.”
پس یونس را برداشته، در دریاانداختند و دریا از تلاطمش آرام شد. ۱۵ 15
Ndipo anatenga Yona namuponya mʼnyanja, ndipo nyanja yowindukayo inakhala bata.
و آن مردمان از خداوند سخت‌ترسان شدند و برای خداوند قربانی‌ها گذرانیدند و نذرها نمودند. ۱۶ 16
Anthuwo ataona zimenezi anachita mantha akulu ndi Yehova, ndipo anapereka nsembe kwa Yehova nalumbira kuti adzatumikira Yehovayo.
واما خداوند ماهی بزرگی پیدا کرد که یونس را فروبرد و یونس سه روز و سه شب در شکم ماهی ماند. ۱۷ 17
Koma Yehova anatuma nsomba yayikulu kuti imeze Yona. Motero Yona anakhala mʼmimba mwa nsombayo masiku atatu, usana ndi usiku.

< یونس 1 >