< یوشع 3 >

بامدادان یوشع بزودی برخاسته، او و تمامی بنی‌اسرائیل از شطیم روانه شده، به اردن آمدند، و قبل از عبور کردن در آنجا منزل گرفتند. ۱ 1
Yoswa ndi Aisraeli onse anadzuka mmamawa nanyamuka ku Sitimu kupita ku Yorodani. Iwo anagona kumeneko asanawoloke mtsinje wa Yorodaniwo.
و بعد از سه روز روسای ایشان از میان لشکرگاه گذشتند. ۲ 2
Patatha masiku atatu, atsogoleri anayendera misasa yonse,
و قوم را امر کرده، گفتند: «چون تابوت عهد یهوه، خدای خود را ببینید که لاویان کهنه آن را می‌برند، آنگاه شما از جای خود روانه شده، در عقب آن بروید. ۳ 3
kulangiza anthu kuti, “Mukaona ansembe a Chilevi atanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu, inu munyamuke pa malo ano ndi kumalitsatira.
و در میان شما و آن، به مقدار دوهزار ذراع مسافت باشد، ونزدیک آن میایید تا راهی که باید رفت بدانید، زیراکه از این راه قبل از این عبور نکرده‌اید.» ۴ 4
Potero mudzadziwa njira yoti mudzere, popeza simunayendepo njira ino nʼkale lomwe. Koma musaliyandikire. Pakati pa inu ndi bokosilo pakhale mtunda pafupifupi kilomita imodzi.”
و یوشع به قوم گفت: «خود را تقدیس نمایید زیرا فرداخداوند در میان شما کارهای عجیب خواهدکرد.» ۵ 5
Yoswa anawuza anthu kuti, “Dzipatuleni tsono pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati panu.”
و یوشع کاهنان را خطاب کرده، گفت: «تابوت عهد را برداشته، پیش روی قوم بروید.» پس تابوت عهد را برداشته، پیش روی قوم روانه شدند. ۶ 6
Mmawa mwake Yoswa ananena kwa ansembe kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano muwoloke ndipo mukhale patsogolo pa anthu.” Motero iwo analinyamula ndi kupita patsogolo pawo.
و خداوند یوشع را گفت: «امروز به بزرگ ساختن تو در نظر تمام اسرائیل شروع می‌کنم تابدانند که چنانکه با موسی بودم با تو نیز خواهم بود. ۷ 7
Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Lero Ine ndidzayamba kukukweza pamaso pa Aisraeli onse kuti adziwe kuti ndili nawe monga ndinalili ndi Mose.
پس تو کاهنان را که تابوت عهد رابرمی دارند امر فرموده، بگو: چون شما به کنار آب اردن برسید در اردن بایستید.» ۸ 8
Ansembe amene akunyamula Bokosi la Chipangano uwalamule kuti, ‘Mukafika ku mtsinje wa Yorodani mulowe mu mtsinjemo ndi kuyima mʼmphepete.’”
و یوشع بنی‌اسرائیل را گفت: «اینجا نزدیک آمده، سخنان یهوه خدای خود را بشنوید.» ۹ 9
Yoswa anati kwa Aisraeli, “Bwerani pano mudzamve mawu a Yehova Mulungu wanu.
و یوشع گفت: «به این خواهید دانست که خدای زنده در میان شماست، و او کنعانیان و حتیان و حویان و فرزیان و جرجاشیان و اموریان و یبوسیان را از پیش روی شما البته بیرون خواهد کرد. ۱۰ 10
Umu ndi mmene mudzadziwira kuti Mulungu wamoyo ali pakati panu. Inu mukamadzapita patsogolo Iye adzathamangitsa Akanaani, Ahiti, Ahivi, Aperezi, Agirigasi, Aamori ndi Ayebusi.
اینک تابوت عهد خداوند تمامی زمین، پیش روی شما به اردن عبور می‌کند. ۱۱ 11
Pamenepo, Bokosi la Chipangano la Mbuye wa dziko lonse lapansi lidzawoloka mu Yorodani patsogolo panu.
پس الان دوازده نفر از اسباطاسرائیل، یعنی از هر سبط یک نفر را انتخاب کنید. ۱۲ 12
Musankhe amuna khumi ndi awiri kuchokera ku fuko lililonse la Israeli.
و واقع خواهد شد چون کف پایهای کاهنانی که تابوت یهوه، خداوند تمامی زمین رابرمی دارند در آبهای اردن قرار گیرد که آبهای اردن، یعنی آبهایی که از بالا می‌آید شکافته شده مثل توده بر روی هم خواهد ایستاد.» ۱۳ 13
Mapazi a ansembe onyamula Bokosi la Yehova, Mbuye wa dziko lapansi, akadzangoponda mu Yorodani, madzi ake onse ochokera ku mtunda adzaleka kuyenda ndipo adzayima ngati chipupa.”
و چون قوم از خیمه های خود روانه شدند تا از اردن عبور کنند و کاهنان تابوت عهد را پیش روی قوم می‌بردند. ۱۴ 14
Tsono Aisraeli anachoka ku misasa yawo kukawoloka mtsinje wa Yorodani. Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano ndiwo anatsogolera anthuwo.
و بردارندگان تابوت به اردن رسیدند، و پایهای کاهنانی که تابوت رابرداشته بودند، به کنار آب فرو رفت (و اردن، تمام موسم حصاد، بر همه کناره هایش سیلاب می‌شود). ۱۵ 15
Nyengo imeneyi inali yokolola ndipo mtsinje wa Yorodani umakhala wodzaza. Komabe, ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anafika ku Yorodani, ndipo atangoponda mʼmadzimo,
واقع شد که آبهایی که از بالامی آمد، بایستاد و به مسافتی بسیار دور تا شهرآدم که به‌جانب صرتان است، بلند شد، و آبی که به سوی دریای عربه، یعنی بحرالملح می‌رفت تمام قطع شد، و قوم در مقابل اریحا عبور کردند. ۱۶ 16
madzi ochokera ku mtunda anasiya kuyenda. Madzi a Yorodani ochokera ku mtunda anawunjikana pamodzi ngati khoma lalitali pa mtunda wautali ndithu ndi mzinda wa Adama chapafupi ndi mzinda wa Zaretani. Madzi othamangira ku nyanja ya Araba, ngakhalenso amene amachokera kuti Nyanja ya Mchere amathera pamenepo. Choncho anthu anawoloka tsidya lina moyangʼanana ndi Yeriko.
و کاهنانی که تابوت عهد خداوند رابرمی داشتند در میان اردن بر خشکی قایم ایستادند، و جمیع اسرائیل به خشکی عبورکردند تا تمامی قوم از اردن، بالکلیه گذشتند. ۱۷ 17
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anali chiyimire powuma, pakati pa Yorodani pamene Aisraeli amawoloka mpaka gulu lonse linamaliza kuwoloka powuma.

< یوشع 3 >