< اعداد 12 >

و مریم و هارون درباره زن حبشی که موسی گرفته بود، بر او شکایت آوردند، زیرا زن حبشی گرفته بود. ۱ 1
Miriamu ndi Aaroni anayamba kuyankhula motsutsana ndi Mose chifukwa cha mkazi wa ku Kusi, popeza Moseyo anakwatira Mkusi.
و گفتند: «آیا خداوندبا موسی به تنهایی تکلم نموده است، مگر به ما نیزتکلم ننموده؟» و خداوند این را شنید. ۲ 2
Iwowo anafunsa kuti, “Kodi Yehova anayankhula kudzera mwa Mose yekha? Kodi sanayankhule kudzeranso mwa ife?” Ndipo Yehova anamva zimenezi.
و موسی مرد بسیار حلیم بود، بیشتر از جمیع مردمانی که در روی زمینند. ۳ 3
(Koma Mose anali munthu wodzichepetsa kwambiri kuposa munthu aliyense pa dziko lapansi).
در ساعت خداوند به موسی و هارون و مریم گفت: «شما هر سه نزد خیمه اجتماع بیرون آیید.» و هر سه بیرون آمدند. ۴ 4
Nthawi yomweyo Yehova anati kwa Mose, Aaroni ndi Miriamu, “Bwerani ku tenti ya msonkhano nonse atatu.” Ndipo atatuwo anapitadi kumeneko.
و خداوند در ستون ابرنازل شده، به در خیمه ایستاد، و هارون و مریم راخوانده، ایشان هر دو بیرون آمدند. ۵ 5
Tsono Yehova anatsika mu mtambo, nayima pa khomo la chihema. Kenaka anayitana Aaroni ndi Miriamu. Ndipo onse awiri atapita patsogolo,
و او گفت: «الان سخنان مرا بشنوید: اگر در میان شما نبی‌ای باشد، من که یهوه هستم، خود را در رویا بر اوظاهر می‌کنم و در خواب به او سخن می‌گویم. ۶ 6
Mulungu anati, “Mverani mawu anga: “Pakakhala mneneri wa Yehova pakati panu, ndimadzionetsera kwa iyeyo mʼmasomphenya, ndimayankhula naye mʼmaloto.
اما بنده من موسی چنین نیست. او در تمامی خانه من امین است. ۷ 7
Koma sinditero ndi Mose mtumiki wanga; Iyeyu ndi wokhulupirika mʼnyumba yanga yonse.
با وی روبرو و آشکارا و نه در رمزها سخن می‌گویم، و شبیه خداوند رامعاینه می‌بیند، پس چرا نترسیدید که بر بنده من موسی شکایت آوردید؟» ۸ 8
Ndimayankhula naye maso ndi maso, momveka bwino osati mophiphiritsa; ndipo amaona maonekedwe a Yehova. Nʼchifukwa chiyani simunaope kuyankhula motsutsana ndi Mose mtumiki wanga?”
و غضب خداوند برایشان افروخته شده، برفت. ۹ 9
Ndipo Yehova anawakwiyira, nachoka.
و چون ابر از روی خیمه برخاست، اینک مریم مثل برف مبروص بود، و هارون بر مریم نگاه کرد و اینک مبروص بود. ۱۰ 10
Pamene mtambo unachoka pamwamba pa Chihema, taonani, Miriamu anagwidwa ndi khate. Aaroni atachewuka anaona Miriamu ali ndi khate;
و هارون به موسی گفت: «وای‌ای آقایم بار این گناه را بر ما مگذار زیرا که حماقت کرده، گناه ورزیده‌ایم. ۱۱ 11
ndipo Aaroni anawuza Mose kuti, “Pepani mbuye wanga, musatilange chifukwa cha tchimo limene tachita mopusa.
و او مثل میته‌ای نباشد که چون از رحم مادرش بیرون آید، نصف بدنش پوسیده باشد.» ۱۲ 12
Musalole kuti Miriamu akhale ngati mwana wobadwa wakufa kuchoka mʼmimba mwa amayi ake, thupi lake litawonongeka.”
پس موسی نزد خداوند استغاثه کرده، گفت: «ای خدا او را شفا بده!» ۱۳ 13
Tsono Mose anafuwulira Yehova kuti, “Chonde Inu Mulungu, muchiritseni!”
خداوند به موسی گفت: «اگر پدرش به روی وی فقط آب دهان می‌انداخت، آیا هفت روز خجل نمی شد؟ پس هفت روز بیرون لشکرگاه محبوس بشود، وبعد از آن داخل شود.» ۱۴ 14
Yehova anayankha Mose kuti, “Abambo ake akanamulavulira malovu mʼmaso, kodi sakanakhala wonyozeka masiku asanu ndi awiri? Mutsekereni kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri, kenaka mumulowetsenso.”
پس مریم هفت روزبیرون لشکرگاه محبوس ماند، و تا داخل شدن مریم، قوم کوچ نکردند. ۱۵ 15
Choncho anamutsekera Miriamu kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri ndipo anthu sanayende ulendo wawo mpaka Miriamu atamulowetsanso.
و بعد از آن، قوم از حضیروت کوچ کرده، در صحرای فاران اردو زدند. ۱۶ 16
Pambuyo pake anthu ananyamuka ku Heziroti ndi kukamanga mʼchipululu cha Parani.

< اعداد 12 >