< مزامیر 49 >

برای سالار مغنیان. مزمور بنی قورح ای تمامی قوم‌ها این را بشنوید! ای جمیع سکنه ربع مسکون این را گوش گیرید! ۱ 1
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
‌ای عوام و خواص! ای دولتمندان وفقیران جمیع! ۲ 2
anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
زبانم به حکمت سخن می‌راند وتفکر دل من فطانت است. ۳ 3
Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
گوش خود را به مثلی فرا می‌گیرم. معمای خویش را بر بربط می‌گشایم. ۴ 4
Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
چرا در روزهای بلا ترسان باشم، چون گناه پاشنه هایم مرا احاطه می‌کند؛ ۵ 5
Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
آنانی که بر دولت خود اعتماد دارند و بر کثرت توانگری خویش فخر می‌نمایند. ۶ 6
Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
هیچ‌کس هرگز برای برادر خودفدیه نخواهد داد و کفاره او را به خدا نخواهد بخشید. ۷ 7
Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
زیرا فدیه جان ایشان گران بهاست و ابد بدان نمی توان رسید ۸ 8
Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
تا زنده بماند تا ابدالاباد وفساد را نبیند. ۹ 9
kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
زیرا می‌بیند که حکیمان می‌میرند. و جاهلان و ابلهان با هم هلاک می‌گردند و دولت خود را برای دیگران ترک می‌کنند. ۱۰ 10
Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
فکر دل ایشان این است که خانه های ایشان دائمی باشد و مسکنهای ایشان دوربه دور؛ و نامهای خود را بر زمینهای خود می‌نهند. ۱۱ 11
Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
لیکن انسان در حرمت باقی نمی ماند، بلکه مثل بهایم است که هلاک می‌شود. ۱۲ 12
Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
این طریقه ایشان، جهالت ایشان است و اعقاب ایشان سخن ایشان را می‌پسندند، سلاه. ۱۳ 13
Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
مثل گوسفندان درهاویه رانده می‌شوند و موت ایشان را شبانی می‌کند و صبحگاهان راستان بر ایشان حکومت خواهند کرد و جمال ایشان در هاویه پوسیده خواهد شد تا مسکنی برای آن نباشد. (Sheol h7585) ۱۴ 14
Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
لیکن خدا جان مرا از دست هاویه نجات خواهد دادزیرا که مرا خواهد گرفت، سلاه. (Sheol h7585) ۱۵ 15
Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
پس ترسان مباش، چون کسی دولتمندگردد و جلال خانه او افزوده شود! ۱۶ 16
Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
زیرا چون بمیرد چیزی از آن نخواهد برد و جلالش در عقب او فرو نخواهد رفت. ۱۷ 17
Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
زیرا در حیات خود، خویشتن را مبارک می‌خواند. و چون بر خوداحسان می‌کنی، مردم ترا می‌ستایند. ۱۸ 18
Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
لیکن به طبقه پدران خود خواهد پیوست که نور را تا به ابدنخواهند دید. ۱۹ 19
iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
انسانی که در حرمت است وفهم ندارد، مثل بهایم است که هلاک می‌شود. ۲۰ 20
Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.

< مزامیر 49 >