< Wyjścia 1 >

1 Teć są imiona synów Izraelskich, którzy weszli do Egiptu z Jakóbem; każdy z domem swym weszli:
Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
2 Ruben, Symeon, Lewi, i Judas.
Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
3 Isaszar, Zabulon, i Benjamin.
Isakara, Zebuloni, Benjamini;
4 Dan, i Neftali, Gad, i Aser.
Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
5 A było wszystkich dusz, które wyszły z biódr Jakóbowych, siedmdziesiąt dusz; a Józef był przedtem w Egipcie.
Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
6 I umarł Józef, i wszyscy bracia jego, i wszystek on rodzaj.
Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
7 A synowie Izraelscy rozrodzili się, i rozpłodzili się, i rozmnożyli się, i zmocnili się bardzo wielce, a napełniona jest ziemia nimi.
Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
8 Między tem powstał król nowy nad Egiptem, który nie znał Józefa;
Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
9 I rzekł do ludu swego: Oto lud synów Izraelskich wielki, i możniejszy nad nas.
Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
10 Przetoż mądrze sobie pocznijmy z nimi, by się snać nie rozmnożył, a jeźliby przypadła wojna, aby się nie przyłączył i on do nieprzyjaciół naszych, i nie walczył przeciwko nam, i nie uszedł z ziemi.
Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
11 A tak ustawili nad nimi poborcę, aby go dręczyli ciężarami swemi; i zbudował lud Izraelski miasta składu Faraonowi: Pytom i Rameses.
Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
12 Ale im więcej go trapili, tem więcej się rozmnażał, i tem więcej rósł, tak, iż ściśnieni byli dla synów Izraelskich.
Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
13 I podbili Egipczanie syny Izraelskie w niewolą ciężką.
ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
14 I przykrzyli im żywot ich robotą ciężką około gliny, i około cegieł, i około każdej roboty na polu, mimo wszelaką robotę swą, do której ich używali bez litości.
Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
15 I rozkazał król Egipski babom Hebrejskim, z których imię jednej Zefora, a imię drugiej Fua;
Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
16 A rzekł: Gdy będziecie babić niewiastom Hebrejskim, a ujrzycie że rodzą, byłliby syn, zabijcież go, a jeźli córka, niech żywa zostanie.
“Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
17 Ale baby one bały się Boga, i nie czyniły, jako im rozkazał król Egipski, ale żywo zachowywały chłopiątka.
Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
18 Zaczem wezwawszy król Egipski onych bab, mówił do nich: Czemuście to uczyniły, żeście żywo zachowały chłopiątka?
Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
19 I odpowiedziały baby Faraonowi: Iż nie są jako niewiasty Egipskie, niewiasty Hebrejskie; bo są duże, pierwej niż przyjdzie do nich baba, rodzą.
Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
20 I czynił dobrze Bóg onym babom; i krzewił się lud, i zmocnili się bardzo.
Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
21 I stało się, przeto że się bały one baby Boga, pobudował im domy.
Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
22 Tedy rozkazał Farao wszystkiemu ludowi swemu, mówiąc: Każdego syna, który się urodzi, w rzekę go wrzućcie, a każdą córkę żywo zachowajcie.
Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”

< Wyjścia 1 >