< Rodzaju 43 >

1 A głód wielki był w onej ziemi.
Njala inakula kwambiri mʼdzikomo.
2 I stało się, gdy strawili onę żywność, którą byli przynieśli z Egiptu, że rzekł do nich ojciec ich: Idźcie znowu, a kupcie nam cokolwiek żywności.
Tsono atatha kudya tirigu yense amene anakatenga ku Igupto, Yakobo anati kwa ana ake aja, “Pitani kuti mukatigulire chakudya china pangʼono.”
3 I rzekł do niego Judas, mówiąc: Oświadczając oświadczył się przeciwko nam ten mąż mówiąc: Nie ujrzycie oblicza mojego, jeźli nie będzie brat wasz z wami:
Koma Yuda anati kwa iye, “Munthu uja anatichenjeza monenetsa kuti, ‘Simudzandionanso ine pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanu.’
4 Jeźli tedy poślesz brata naszego z nami, pojedziemy i nakupiemyć żywności;
Mukalola kuti mngʼono wathuyu apite nafe, ndiye ife tidzapita kukakugulirani chakudya.
5 Ale jeźli nie poślesz, nie pojedziemy; bo on mąż mówił do nas: Nie ujrzycie twarzy mojej, jeźli nie będzie brata waszego z wami.
Koma mukapanda kumulola, ife sitipita, chifukwa munthuyo anatiwuza kuti, ‘Simudzandionanso pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanuyo.’”
6 Tedy rzekł Izrael: Przeczżeście mi tak źle uczynili, powiedziawszy temu mężowi, że jeszcze macie brata?
Tsono Israeli anafunsa kuti, “Bwanji inu munandiputira mavuto oterewa pomuwuza munthuyo kuti muli ndi mʼbale wanu wina?”
7 I rzekli: Pilnie się pytał on mąż o nas, i o rodzinie naszej, mówiąc: Żywże jeszcze ojciec wasz? macieli jeszcze którego brata? I odpowiedzieliśmy mu według pytania jego; cóżeśmy wiedzieli, że miał mówić: Przywiedźcie mi tu brata waszego?
Iwo anayankha, “Munthuyo ankangofunsafunsa za ife ndi za banja lathu. Iye anatifunsa kuti, ‘Kodi abambo anu akanali ndi moyo? Kodi muli ndi mʼbale wanu wina?’ Ife tinkangoyankha mafunso ake. Ife tikanadziwa bwanji kuti adzanena kuti, ‘Mubwere naye kuno mʼbale wanu’?”
8 I rzekł Judas do Izraela, ojca swego: Poślij tego młodzieńca ze mną, a wstawszy pojedziemy, abyśmy żyli a nie pomarli głodem, tak my, jako i ty, i dziateczki nasze.
Ndipo Yuda anati kwa Israeli abambo ake, “Muloleni mnyamatayo apite ndi ine, ndipo tinyamuka nthawi yomweyo, kuti ife ndi inu pamodzi ndi ana athu tikhale ndi moyo.
9 Ja przyrzekam zań, z ręki mojej szukaj go; jeźli go nie przywiodę do ciebie, a nie stawię go przed tobą, będęć winien grzechu po wszystkie dni;
Ine ndidzipereka kuti ndikhale chikole cha moyo wa mnyamatayu. Ine ndidzamuteteza. Ngati sindibwera naye ndi kumupereka kwa inu, ndidzakhala wolakwa pamaso panu moyo wanga wonse.
10 Bo gdybyśmy byli nie omieszkali, już byśmy się byli dwa kroć wrócili.
Mmene zililimu, tikanapanda kuchedwa, bwenzi titapita ndi kubwerako kawiri.”
11 Tedy rzekł do nich Izrael, ojciec ich: Jeźliże tak być musi, uczyńcież to; nabierzcie najlepszych pożytków ziemi w naczynia wasze, a zanieście mężowi onemu w upominku: trochę balsamu, i trochę miodu, i rzeczy wonnych, i myrry, orzechów terebintowych, i migdałów.
Tsono abambo awo Israeli anawawuza kuti, “Ngati pafunika kutero, ndiye muchite izi: Ikanimo zipatso zabwino kwambiri za dziko lino mʼmatumba mwanu ndi kumutengera munthuyo ngati mphatso. Mumutengere mafuta wopaka pangʼono, uchi pangʼono, mafuta wonunkhiritsa chakudya, mule, mtedza ndi alimoni.
12 Pieniądze też dwoje weźmijcie do rąk waszych, a pieniądze przywrócone na wierzchu worów waszych odnieście w ręce swoje; snać się to omyłką stało.
Mutenge ndalama zokwanira. Ndalama zina nʼzokamubwezera zija anakuyikirani mʼmatumba anu zija. Mwina anangolakwitsa.
13 Ale i brata waszego weźmijcie, a wstawszy jedźcie znowu do męża onego;
Mutengeninso mngʼono wanuyu ndi kubwerera kwa munthuyo msanga.
14 A Bóg Wszechmogący niech wam da miłosierdzie przed obliczem tego męża, aby wam wypuścił brata waszego drugiego i Benjamina; a ja jako osierociały bez dziatek będę.
Ndipo Mulungu Wamphamvuzonse akuchitireni chifundo pamaso pa munthuyo kuti akamulole mʼbale wanu wina uja ndi Benjamini kuti abwerere ndi inu. Kukakhala kulira, ndine wolira basi.”
15 Tedy wziąwszy oni mężowie on podarek, i dwoje pieniądze wziąwszy w ręce swe, i Benjamina, wstali, i jechali do Egiptu, i stanęli przed Józefem.
Choncho abale aja anatenga mphatso, ndalama zokwanira ndi Benjamininso. Iwo anafulumira kupita ku Igupto ndipo anakaonekera kwa Yosefe.
16 A ujrzawszy Józef z nimi Benjamina, rzekł do tego, który był sprawcą domu jego: Wprowadź te męże w dom, a zabij bydlę i nagotuj; bo ze mną jeść będą mężowie ci w południe.
Yosefe ataona Benjamini ali pamodzi ndi abale ake, anati kwa wantchito wa mʼnyumba mwake, “Atengereni anthu awa ku nyumba kwanga, ndipo uphe nyama ndi kukonza bwino chakudya popeza amenewa adya ndi ine masana ano.”
17 I uczynił on mąż, jako mu rozkazał Józef, a wprowadził on mąż one ludzie w dom Józefów.
Wantchitoyo anachita monga momwe Yosefe ananenera, ndipo anawatengera abale aja ku nyumba kwa Yosefe.
18 Bali się tedy mężowie oni, gdy byli wprowadzeni w dom Józefów, i mówili: Dla onychci to pieniędzy, które pierwej włożono było do worów naszych, wprowadzeni tu jesteśmy, aby potwarz na nas zwaliwszy targnął się na nas, a pobrał w niewolą nas i osły nasze.
Tsono anthu aja anachita mantha ataona kuti akuwatengera ku nyumba kwa Yosefe. Mʼmaganizo awo ankanena kuti, “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zija zinabwezeredwa mʼmatumba athu poyamba paja. Ameneyu akufuna kuti atipanikize ndi kutigwira ukapolo natilanda abulu athu.”
19 A przystąpiwszy do męża tego, który był sprawcą domu Józefowego, mówili do niego we drzwiach domu.
Choncho atafika pa khomo la nyumba ya Yosefe anamuyandikira wantchito wa Yosefe nayankhula naye kuti,
20 I rzekli: Słuchaj mię, panie mój! przyjechaliśmy byli pierwej kupować żywność.
“Pepani mbuye wathu, ife tinabweranso ulendo woyamba kudzagula chakudya
21 I stało się, gdyśmy przyjechali do gospody, i rozwiązaliśmy wory nasze, oto, pieniądze każdego były na wierzchu woru jego, pieniądze nasze, według wagi ich, któreśmy zaś przynieśli w rękach naszych.
koma titafika pa malo ena kuti tigone, tinatsekula matumba athu ndipo aliyense wa ife anapeza ndalama zake momwe zinalili zili pakamwa pa thumba lake. Ndiye tabwerera nazo.
22 Pieniądze też drugie przynieśliśmy w rękach naszych, abyśmy nakupili żywności, a nie wiemy, kto włożył te pieniądze nasze do worów naszych.
Tabweretsanso ndalama zina kuti tigule chakudya. Sitikudziwa kuti kaya ndani anayika ndalamazo mʼmatumba athu.”
23 A on rzekł: Pokój wam, nie bójcie się; Bóg wasz, i Bóg ojca waszego dał wam skarb do worów waszych; pieniądze wasze doszły mię. I wywiódł do nich Symeona.
Koma iye anati, “Mitima yanu ikhale pansi ndipo musachite mantha. Mulungu wanu, Mulungu wa abambo anu, anakuyikirani chumacho mʼmatumba anu. Ine ndinalandira ndalama zanu.” Ndipo anakawatulutsira Simeoni.
24 A przywiódłszy on mąż one ludzie w dom Józefów, dał im wody, i umyli nogi swe; dał też obrok osłom ich.
Wantchito uja anawalowetsa anthuwo mʼnyumba ya Yosefe, nawapatsa madzi kuti asambe mapazi awo. Anadyetsanso abulu awo.
25 Zatem nagotowali podarek, niż przyszedł Józef w południe; słyszeli bowiem, iż tam mieli jeść chleb.
Abale aja anakonzeratu mphatso zawo zija kuti adzapereke kwa Yosefe, popeza anamva kuti Yosefe adzadya komweko masana.
26 A gdy wszedł Józef w dom, przynieśli mu podarek, który mieli w rękach swych w domu onym, i kłaniali mu się aż do ziemi.
Yosefe atafika ku nyumbako, iwo anapereka mphatso zija namuweramira pansi.
27 I pytał ich, jakoby się mieli, i rzekł: Zdrówże jest ojciec wasz stary, o którymeście mi powiadali? Żywże jeszcze?
Yosefe anawafunsa za moyo wawo kenaka anati, “Kodi abambo anu wokalamba amene munkandiwuza aja ali bwanji? Ali ndi moyobe?”
28 A oni odpowiedzieli: Zdrówci sługa twój, ojciec nasz, jeszczeć żyw. A schyliwszy się, pokłonili mu się.
Iwo anayankha kuti, “Mtumiki wanu abambo athu akanali ndi moyo ndipo ali bwino.” Ndipo anamugwadira namuweramira pansi.
29 Tedy podniósłszy oczy swe, ujrzał Benjamina, brata swego, syna matki swej, i rzekł: Tenże jest brat wasz młodszy, o którymeście mi powiadali? I rzekł mu: Bóg niech ci będzie miłościw, miły synu.
Pomwazamwaza maso Yosefe anaona Benjamini, mʼbale wake weniweni wa bere limodzi, ndipo anafunsa, “Kodi uyu ndiye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri amene munkandiwuza uja?” Kenaka anati, “Ambuye akukomere mtima mwana wanga.”
30 I pokwapił się Józef wynijść, bo się były wzruszyły wnętrzności jego ku bratu swemu, i szukał miejsca, gdzie by płakał, i wszedłszy do komory, płakał tam.
Kenaka Yosefe anafulumira kutuluka chifukwa mtima wake unadzaza ndi chifundo cha mngʼono wake ndipo anafuna kulira. Tsono anakalowa mʼchipinda chakechake nakalira kumeneko.
31 Potem umywszy twarz swoję, wyszedł zasię, i wstrzymał się, i rzekł: Kładźcie chleb.
Atatha kupukuta misozi mʼmaso mwake anatuluka, ndipo modzilimbitsa analamula kuti chakudya chibwere.
32 I położono jemu osobno, i onym osobno, Egipczanom też, którzy jedli z nim, osobno; bo nie mogą jeść Egipczanie z Hebrejczykami chleba, gdyż to jest obrzydliwością Egipczanom.
Anamupatsira Yosefe chakudya payekha, abale ake aja pawokha, ndiponso Aigupto amene ankadya pamodzi ndi iye nawonso pawokha. Izi zinali choncho chifukwa Aigupto ankanyansidwa kudya pamodzi ndi Ahebri.
33 I usiedli przed obliczem jego, pierworodny według pierworodztwa swego, a młodszy według młodości swej; i dziwowali się mężowie oni patrząc jeden na drugiego.
Abale aja anawakhazika patsogolo pa Yosefe. Iwo anawakhazika monga mwa mabadwidwe awo kuyambira woyamba kubadwa mpaka wotsirizira; ndipo ankangoyangʼanitsitsana modabwa.
34 I biorąc potrawy przed sobą dawał im; a dostała się pięć kroć większa część Benjaminowi nad inne części onych wszystkich; i pili, a podpili sobie z nim.
Tsono ankawagawira chakudya kuchokera pa tebulo la Yosefe. Koma chakudya cha Benjamini chinkaposa cha ena onsewa kasanu. Motero anadya ndi kumwa mpaka kukhuta, ndipo anasangalala pamodzi ndi Yosefe.

< Rodzaju 43 >