< Psalmów 105 >

1 Wysławiajcie Pana; ogłaszajcie imię jego; opowiadajcie między narodami sprawy jego.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 Śpiewajcie mu, śpiewajcie mu psalmy, rozmawiajcie o wszystkich cudach jego.
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Chlubcie się imieniem świętem jego; niech się weseli serce szukających Pana.
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Szukajcież Pana i mocy jego; szukajcie oblicza jego zawsze.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Przypominajcie sobie dziwy jego, które czynił, cuda jego i sądy ust jego.
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 Wy nasienie Abrahama, sługi jego! Wy synowie Jakóbowi, wybrani jego!
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 Onci jest Pan, Bóg nasz, po wszystkiej ziemi sądy jego.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 Pamięta wiecznie na przymierze swoje: na słowo, które przykazał aż do tysiącznego pokolenia;
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 Które postanowił z Abrahamem, i na przysięgę swą uczynioną Izaakowi.
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 Bo je postanowił Jakóbowi za ustawę, a Izraelowi za umowę wieczną.
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 Mówiąc: Tobie dam ziemię Chananejską za sznur dziedzictwa waszego;
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 Kiedy ich był mały poczet, prawie mały poczet, a jeszcze w niej byli przychodniami.
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 Przechodzili zaiste od narodu do narodu, a z królestwa innego ludu;
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 Nie dopuszczał nikomu, aby im miał krzywdę czynić; nawet karał dla nich i królów, mówiąc:
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 Nie tykajcie pomazańców moich, a prorokom moim nie czyńcie nic złego.
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 Gdy przywoławszy głód na ziemię, wszystkę podporę chleba pokruszył.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 Posłał przed nimi męża, który był za niewolnika sprzedany, to jest Józefa;
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 Którego nogi pętami trapili, a żelazo ścisnęło ciało jego,
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 Aż do onego czasu, gdy się o nim wzmianka stała; mowa Pańska doświadczała go.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 Posławszy król kazał go puścić; ten, który panował nad narodami, wolnym go uczynił.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 Postanowił go panem domu swego, i książęciem nad wszystką dzierżawą swoją,
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 Aby władał i książętami jego według zdania duszy swojej, i starców jego mądrości nauczał.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Potem wszedł Izrael do Egiptu, a Jakób był gościem w ziemi Chamowej;
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 Gdzie rozmnożył Bóg lud swój bardzo, i uczynił go możniejszym nad nieprzyjaciół jego.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 Odmienił serce ich, iż mieli w nienawiści lud jego, a zmyślali zdrady przeciw sługom jego.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 Posłał Mojżesza, sługę swego i Aarona, którego obrał;
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 Którzy im przedłożyli słowa znaków jego, i cuda w ziemi Chamowej.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 Posłał ciemności, i zaćmiło się, a nie byli odpornymi słowu jego.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 Obrócił wody ich w krew, a pomorzył ryby w nich.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Wydała ziemia ich mnóstwo żab, i były w pałacach królów ich.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 Rzekł, a przyszła rozmaita mucha, i mszyce we wszystkich granicach ich.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 Dał grad miasto deszczu, ogień palący na ziemię ich.
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 Także potłukł winnice ich, i figi ich, a pokruszył drzewa w granicach ich.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 Rzekł, a przyszła szarańcza, i chrząszczów niezliczone mnóstwo;
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 I pożarły wszelkie ziele w ziemi ich, a pojadły urodzaje ziemi ich.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 Nawet pobił wszystko pierworodztwo w ziemi ich, początek wszystkiej siły ich.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 Tedy ich wywiódł ze srebrem i ze złotem, a nie był nikt słaby między pokoleniem ich.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Radował się Egipt, gdy oni wychodzili; albowiem był przypadł na nich strach ich.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 Rozpostarł obłok na okrycie ich, a ogień na oświecanie nocy.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 Na żądanie ich przywiódł przepiórki, a chlebem niebieskim nasycił ich.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 Otworzył skałę i wypłynęły wody, a płynęły po suchych miejscach jako rzeka.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 Albowiem wspomniał na słowo świętobliwości swojej, które rzekł do Abrahama, sługi swego.
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 Przetoż wywiódł lud swój z weselem, a z śpiewaniem wybranych swoich.
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 I podał im ziemię pogan, a posiedli prace narodów.
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 Aby zachowali ustawy jego, a prawa jego przestrzegali. Halleluja.
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalmów 105 >